< Yesaya 15 >

1 Uthenga wonena za Mowabu: Popeza kuti mu usiku umodzi wokha mzinda wa Ari wa ku Mowabu wawonongedwa, wawonongedwa pa usiku umodzi wokha. Mzinda wa Kiri wawonongedwa, wawonongedwa pa usiku umodzi wokha.
有關摩阿布的神諭:實在,摩阿布的阿爾經過一夜的蹂躪,就滅亡了!實在,摩阿布的克爾經過一夜的摧殘,就滅亡了!
2 Anthu a ku Diboni akupita ku nyumba ya milungu yawo, akupita ku malo awo achipembedzo kukalira; anthu a ku Mowabu akulirira mofuwula mzinda wa Nebo ndi wa Medeba. Mutu uliwonse wametedwa mpala, ndipo ndevu zonse zametedwa.
狄朋女兒走上高丘哭泣,摩阿布為乃波和默德巴悲號;眾人的頭都剃光了,眾人的鬍鬚都剪去了;
3 Mʼmisewu akuvala ziguduli; pa madenga ndi mʼmabwalo aliyense akulira mofuwula, misozi ili pupupu.
有的在街道上穿著苦衣,有的在屋頂上痛哭;在廣場上的人,人人哀號,流淚痛哭。
4 Anthu a ku Hesiboni ndi Eleali akulira mofuwula, mawu awo akumveka mpaka ku Yahazi. Kotero asilikali a ku Mowabu akulira mofuwula, ndipo ataya mtima.
赫市朋和厄肋阿肋號啕,雅哈茲都可聽到他們的哭聲;因此摩阿布的兩腰為之顫動,她的心靈為之恐怖。
5 Inenso ndikulirira Mowabu; chifukwa othawa nkhondo ake akupita akulira ku chikweza cha Luluti mpaka ku Zowari ndi Egilati-Selisiya akupita akulira ku chikweza cha Luhiti, Akulira mosweka mtima pa njira yopita ku Horonaimu; akulira mosweka mtima chifukwa cha chiwonongeko chawo.
我的心為摩阿布發出哀號,她的難民已逃至左哈爾。他們哭著攀上了路希特的山坡,在曷洛納因的道上揚起了失望的哀聲。
6 Madzi a ku Nimurimu aphwa ndipo udzu wauma; zomera zawonongeka ndipo palibe chomera chobiriwira chatsala.
尼默陵的水地成了荒野,青草枯焦了,嫩芽萎縮了,再也見不到青綠。
7 Kotero kuti chuma chomwe anachipeza ndi kuchisunga, achitenga kuti awoloke nacho chigwembe cha Misondozi.
為此,他們將所有的積蓄和財物,都帶過了「柳樹河。」
8 Kulira kwawo kukumveka mʼdziko lonse la Mowabu; kulira kwawo kosweka mtima kukumveka mpaka ku Egilaimu ndi Beeri-Elimu.
因為哀叫聲傳遍了摩阿布四境,她的哭聲已傳到厄革拉因,她的哭聲已達到貝爾厄林。
9 Madzi a ku Dimoni afiira ndi magazi, komabe ndidzabweretsa zina zambiri pa Dimoni, mkango woti udzagwire aliyense othawa mu Mowabu ndi aliyense wotsala mʼdzikomo.
狄孟的水已滿了鮮血,我還要加禍於狄孟:為摩阿布的難民和當地的遺民將有一隻獅子。

< Yesaya 15 >