< Yesaya 14 >

1 Yehova adzachitira chifundo Yakobo; adzasankhanso Israeli ndi kuwalola kuti akhalenso mʼdziko lawo. Alendo adzabwera kudzakhala nawo ndi kudziphatika okha kukhala ngati a mʼnyumba ya Yakobo.
خداوند بر قوم اسرائیل ترحم خواهد کرد و بار دیگر آنها را برخواهد گزید و در سرزمینشان ساکن خواهد ساخت. بیگانگان مهاجر در آنجا با خاندان یعقوب زندگی خواهند کرد.
2 Anthu a mitundu ina adzaperekeza a Israeli ku dziko lawo. Tsono Aisraeli adzasandutsa anthu a mitundu ina aja kukhala antchito awo aamuna ndi aakazi mʼdziko la Yehova. Ndiye kuti Aisraeli adzasandutsa akapolo anthu amene kale anali ambuye awo. Iwo adzasandutsa akapolo anthu amene kale ankawalamulira ndi kuwazunza.
قومهای جهان به ایشان کمک خواهند کرد تا به وطن خود بازگردند. قوم اسرائیل در سرزمینی که خداوند به ایشان داده قومهای دیگر را به بردگی خواهند گرفت. آنانی که قوم اسرائیل را اسیر کرده بودند، خود به اسارت ایشان در خواهند آمد و بنی‌اسرائیل بر دشمنان خود فرمانروایی خواهند کرد.
3 Yehova akadzakupumitsani ku zowawa ndi mavuto, ndiponso kuntchito yakalavulagaga imene ankakugwiritsani,
هنگامی که خداوند قوم خود را از درد و اضطراب، بندگی و بردگی رهایی بخشد،
4 mudzayankhula monyogodola mfumu ya Babuloni kuti, Wopsinja uja watha! Ukali wake uja watha!
آنگاه ایشان با ریشخند به پادشاه بابِل چنین خواهند گفت: «ای پادشاه ظالم سرانجام نابود شدی و ستمکاریهایت پایان گرفت
5 Yehova wathyola chikwapu cha anthu oyipa, Iye waphwanya ndodo ya olamulira.
خداوند حکومت ظالمانه و شرارت‌آمیز تو را در هم شکست.
6 Mfumu ya ku Babuloni inkakantha mitundu ya anthu mwaukali powamenya kosalekeza, Iyo inkagonjetsa anthu a mitundu ina mwaukali ndikuwazunza kosalekeza.
تو با خشم و غضب، مردم را پیوسته شکنجه و آزار می‌دادی،
7 Koma tsopano mayiko onse ali pa mpumulo ndi pa mtendere; ndipo akuyimba mokondwa.
اما اکنون تمام مردم از دست تو آسوده شده، در آرامش زندگی می‌کنند و از شادی سرود می‌خوانند.
8 Ngakhale mitengo ya payini ndi mikungudza ya ku Lebanoni ikuyimba za iwe mokondwa ndipo ikuti, “Chigwetsedwere chako pansi, palibe wina anabwera kudzatigwetsa.”
حتی صنوبرها و سروهای لبنان نیز با شادمانی می‌سرایند:”از زمانی که تو سقوط کردی دیگر کسی نیست که ما را قطع کند!“
9 Ku manda kwatekeseka kuti akulandire ukamabwera; mizimu ya anthu akufa, aja amene anali atsogoleri a dziko lapansi, yadzutsidwa. Onse amene anali mafumu a mitundu ya anthu ayimiritsidwa pa mipando yawo. (Sheol h7585)
«دنیای مردگان آماده می‌شود تا به استقبال تو بیاید. رهبران و پادشاهان دنیا که سالها پیش مرده‌اند، آنجا در انتظار تو هستند. (Sheol h7585)
10 Onse adzayankha; adzanena kwa iwe kuti, “Iwenso watheratu mphamvu ngati ife; Iwe wafanana ndi ife.”
آنها وقتی تو را ببینند به تو خواهند گفت:”تو نیز مانند ما ضعیف شدی و با ما فرقی نداری!
11 Ulemerero wako wonse walowa mʼmanda, pamodzi ndi nyimbo za azeze ako; mphutsi zayalana pogona pako ndipo chofunda chako ndi nyongolotsi. (Sheol h7585)
حشمت تو از دست رفته است و نوای دلنشین بربطهای کاخ تو دیگر به گوش نمی‌رسد. اکنون تشک تو کرمها هستند و لحافت موریانه‌ها.“ (Sheol h7585)
12 Wagwa pansi bwanji kuchoka kumwamba, iwe nthanda, mwana wa mʼbandakucha! Wagwetsedwa pansi pa dziko lapansi, Iwe amene unagonjetsapo mitundu ya anthu!
«ای ستارهٔ درخشان صبح، چگونه از آسمان افتادی! ای که بر قومهای جهان مسلط بودی، چگونه بر زمین افکنده شدی!
13 Mu mtima mwako unkanena kuti, “Ndidzakwera mpaka kumwamba; ndidzakhazika mpando wanga waufumu pamwamba pa nyenyezi za Mulungu; ndidzakhala pa mpando waufumu pa phiri losonkhanirako, pamwamba penipeni pa phiri la kumpoto.
در دل خود می‌گفتی:”تا به آسمان بالا خواهم رفت، تخت سلطنتم را بالای ستارگان خدا خواهم نهاد و بر قلهٔ کوهی در شمال که خدایان بر آن اجتماع می‌کنند جلوس خواهم کرد.
14 Ndidzakwera pamwamba pa mitambo; ndidzafanana ndi Wammwambamwamba.”
به بالای ابرها خواهم رفت و مانند خدای متعال خواهم شد.“
15 Koma watsitsidwa mʼmanda pansi penipeni pa dzenje. (Sheol h7585)
اما تو به دنیای مردگان که در قعر زمین است، سرنگون شدی. (Sheol h7585)
16 Anthu akufa adzakupenyetsetsa nadzamalingalira za iwe nʼkumati, “Kodi uyu ndi munthu uja anagwedeza dziko lapansi ndi kunjenjemeretsa maufumu,
اینک وقتی مردگان تو را می‌بینند به تو خیره شده، می‌پرسند:”آیا این همان کسی است که زمین و قدرتهای جهان را می‌لرزاند؟
17 munthu amene anasandutsa dziko lonse chipululu, amene anagwetsa mizinda yake ndipo sankalola kuti anthu ogwidwa abwerere kwawo?”
آیا این همان کسی است که دنیا را ویران می‌کرد و شهرها را از بین می‌برد و بر اسیران خود رحم نمی‌کرد؟“
18 Mafumu onse a mitundu ya anthu akugona mwaulemu aliyense mʼmanda akeake.
«پادشاهان جهان، شکوهمندانه در قبرهایشان آرامیده‌اند،
19 Koma iwe watayidwa kunja kwa manda ako, ngati nthambi yowola ndi yonyansa. Mtembo wako waphimbidwa ndi anthu ophedwa; amene anabayidwa ndi lupanga, anatsikira mʼdzenje lamiyala ngati mtembo woponderezedwa.
ولی جنازهٔ تو مثل شاخه‌ای شکسته، دور انداخته شده است. نعش تو در قبر روباز است و روی آن را جنازه‌های کشته‌شدگان جنگ پوشانده و مانند لاشۀ پایمال شده، تا به سنگهای ته گودال فرو رفته است.
20 Sudzayikidwa nawo mʼmanda mwaulemu, chifukwa unawononga dziko lako ndi kupha anthu ako. Zidzukulu za anthu oyipa sizidzakumbukika nʼpangʼono pomwe.
تو مانند پادشاهان دیگر دفن نخواهی شد، زیرا مملکت خود را از بین بردی و قوم خود را به نابودی کشاندی. از خاندان شرور تو کسی زنده نخواهد ماند.
21 Konzani malo woti muphere ana ake aamuna chifukwa cha machimo a makolo awo; kuti angadzuke ndi kulanda dziko lapansi ndi kulidzaza dziko lonselo ndi mizinda yawo.
پسران تو به خاطر شرارت اجدادشان کشته خواهند شد، و کسی از آنها باقی نخواهد ماند تا دنیا را فتح کند و شهرها در آن بسازد.»
22 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ine ndidzathira nkhondo mzinda wa Babuloni. Ndidzachotseratu mu Babuloni dzina lake ndi onse otsaliramo. Ndiye kuti sipadzakhala ana kapena zidzukulu,” akutero Yehova.
خداوند لشکرهای آسمان می‌فرماید: «من خود بر ضد بابِل برخواهم خاست و آن را نابود خواهم کرد. نسل بابِلی‌ها را ریشه‌کن خواهم کرد تا دیگر کسی از آنها زنده نماند.»
23 “Ndidzawusandutsa mzindawo malo okhalamo anungu ndiponso dambo lamatope; ndidzawusesa ndi tsache lowononga,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
خداوند لشکرهای آسمان می‌فرماید: «بابِل را به باتلاق تبدیل خواهم کرد تا جغدها در آن منزل کنند. با جاروی هلاکت، بابِل را جارو خواهم کرد تا هر چه دارد از بین برود.»
24 Yehova Wamphamvuzonse walumbira kuti, “Ndithudi, monga ndaganizira ndidzachitadi choncho, ndipo monga momwe ndatsimikizira zidzakhala momwemo ndithu.
خداوند لشکرهای آسمان قسم خورده، می‌گوید: «آنچه اراده نموده و تقدیر کرده‌ام به یقین واقع خواهد شد.
25 Ndidzawawononga Asiriya mʼdziko langa; ndidzawapondereza ndi mapazi pa mapiri anga; ndidzachotsa goli lawo pa anthu anga, ndipo ndidzachotsa katundu wawo pa mapewa awo.”
من سپاه آشور را هنگامی که به سرزمین من اسرائیل برسد، شکست خواهم داد و سربازانش را روی کوههایم تار و مار خواهم کرد. قوم من دیگر بردهٔ آنها نخواهد بود و آنها را بندگی نخواهد کرد.
26 Izi ndizo ndakonza kuti zichitike pa dziko lonse lapansi, ndatambasula dzanja pa anthu a mitundu yonse.
دست توانای خود را دراز خواهم کرد و قومها را مجازات خواهم نمود. این است آنچه برای قومها تقدیر کرده‌ام.»
27 Pakuti Yehova Wamphamvuzonse watsimikiza, ndipo ndani angamuletse? Dzanja lake latambasulidwa ndipo ndani angalibweze?
بله خداوند لشکرهای آسمان این را تقدیر کرده است. پس چه کسی می‌تواند آن را باطل کند؟ این دست اوست که دراز شده است، بنابراین چه کسی می‌تواند آن را بازگرداند؟
28 Uthenga uwu unabwera chaka chimene mfumu Ahazi anamwalira:
در سالی که آحاز پادشاه درگذشت، این پیغام از سوی خدا نازل شد:
29 Musakondwere inu Afilisti nonse kuti Asiriya amene anali ngati ndodo yokukanthani anathedwa; chifukwa kuchokera ku njoka yomweyi (mfumu ya Aasiriya) mudzatuluka mphiri, ndipo chipatso chake chidzakhala njoka yaliwiro ndiponso yaululu.
ای فلسطینی‌ها، از مرگ پادشاهی که بر شما ظلم می‌کرد شادی نکنید، زیرا پسرش از او بدتر خواهد کرد! از مار، افعی به وجود می‌آید و از افعی، اژدهای آتشین!
30 Osaukitsitsa adzapeza chakudya ndipo amphawi adzakhala mwamtendere. Koma anthu ako ndidzawawononga ndi njala, ndipo njalayo idzapha ngakhale opulumuka ako.
خداوند بیچارگان قوم خود را شبانی خواهد کرد و آنها در چراگاه او راحت خواهند خوابید، اما بر شما فلسطینی‌ها قحطی خواهد فرستاد و شما را هلاک خواهد کرد.
31 Lirani kwambiri, anthu a pa chipata! Fuwulani kwambiri, anthu a mu mzinda! Njenjemerani ndi mantha, inu Afilisti nonse! Mtambo wa utsi ukuchokera kumpoto, ndipo palibe wamantha pakati pa ankhondo ake.
ای شهرهای فلسطین گریه و شیون کنید و بلرزید، زیرا قشونی قدرتمند همچون دودی سیاه از شمال در حرکت است و سربازانش برای جنگیدن به جلو می‌تازند!
32 Kodi tidzawayankha chiyani amithenga a ku Filisitiya? “Yehova wakhazikitsa Ziyoni, ndipo mu mzinda wakewu, anthu ozunzika apeza populumukira.”
پس به فرستادگانی که از فلسطین می‌آیند چه باید گفت؟ باید گفت که خداوند اورشلیم را بنیاد نهاده تا قوم رنجدیدهٔ او در آن پناه گیرند.

< Yesaya 14 >