< Yesaya 14 >

1 Yehova adzachitira chifundo Yakobo; adzasankhanso Israeli ndi kuwalola kuti akhalenso mʼdziko lawo. Alendo adzabwera kudzakhala nawo ndi kudziphatika okha kukhala ngati a mʼnyumba ya Yakobo.
Près de venir est son temps, et ses jours ne seront pas différés. Car le Seigneur aura pitié de Jacob, il fera encore choix d’Israël, et il les fera reposer dans leur terre; l’étranger se joindra à eux, et il s’attachera à la maison de Jacob.
2 Anthu a mitundu ina adzaperekeza a Israeli ku dziko lawo. Tsono Aisraeli adzasandutsa anthu a mitundu ina aja kukhala antchito awo aamuna ndi aakazi mʼdziko la Yehova. Ndiye kuti Aisraeli adzasandutsa akapolo anthu amene kale anali ambuye awo. Iwo adzasandutsa akapolo anthu amene kale ankawalamulira ndi kuwazunza.
Et les peuples les prendront et les ramèneront en leur lieu; et la maison d’Israël les possédera dans la terre du Seigneur comme serviteurs et comme servantes; et ils prendront ainsi ceux qui les avaient pris; et ils soumettront leurs exacteurs.
3 Yehova akadzakupumitsani ku zowawa ndi mavuto, ndiponso kuntchito yakalavulagaga imene ankakugwiritsani,
Et il arrivera en ce jour-là, que lorsque le Seigneur t’aura donné du repos après ton travail, et après ton oppression, et après la dure servitude à laquelle tu as été auparavant assujetti;
4 mudzayankhula monyogodola mfumu ya Babuloni kuti, Wopsinja uja watha! Ukali wake uja watha!
Tu emploieras cette parabole contre le roi de Babylone, et tu diras: Comment a cessé l’exacteur, et a discontinué le tribut?
5 Yehova wathyola chikwapu cha anthu oyipa, Iye waphwanya ndodo ya olamulira.
Le Seigneur a brisé le bâton des impies, la verge des dominateurs,
6 Mfumu ya ku Babuloni inkakantha mitundu ya anthu mwaukali powamenya kosalekeza, Iyo inkagonjetsa anthu a mitundu ina mwaukali ndikuwazunza kosalekeza.
Qui, dans son indignation, frappait des peuples d’une plaie incurable, qui, dans sa fureur, assujettissait des nations, qui les persécutait cruellement.
7 Koma tsopano mayiko onse ali pa mpumulo ndi pa mtendere; ndipo akuyimba mokondwa.
Toute la terre se repose et est en silence, elle est dans la joie et dans l’exultation;
8 Ngakhale mitengo ya payini ndi mikungudza ya ku Lebanoni ikuyimba za iwe mokondwa ndipo ikuti, “Chigwetsedwere chako pansi, palibe wina anabwera kudzatigwetsa.”
Les sapins même et les cèdres du Liban se sont réjouis à ton sujet, disant: Depuis que tu dors, il ne monte personne qui nous abatte.
9 Ku manda kwatekeseka kuti akulandire ukamabwera; mizimu ya anthu akufa, aja amene anali atsogoleri a dziko lapansi, yadzutsidwa. Onse amene anali mafumu a mitundu ya anthu ayimiritsidwa pa mipando yawo. (Sheol h7585)
L’enfer au-dessous a été tout troublé au moment de ton arrivée, il t’a suscité les géants. Tous les princes de la terre se sont levés de leurs trônes, ainsi que tous les princes des nations. (Sheol h7585)
10 Onse adzayankha; adzanena kwa iwe kuti, “Iwenso watheratu mphamvu ngati ife; Iwe wafanana ndi ife.”
Tous élèveront la voix, et te diront: Toi aussi tu as reçu des blessures comme nous, tu es devenu semblable à nous.
11 Ulemerero wako wonse walowa mʼmanda, pamodzi ndi nyimbo za azeze ako; mphutsi zayalana pogona pako ndipo chofunda chako ndi nyongolotsi. (Sheol h7585)
Ton orgueil a été précipité dans les enfers, ton cadavre est tombé par terre; au-dessous de toi la teigne formera ta couche, et ta couverture seront les vers. (Sheol h7585)
12 Wagwa pansi bwanji kuchoka kumwamba, iwe nthanda, mwana wa mʼbandakucha! Wagwetsedwa pansi pa dziko lapansi, Iwe amene unagonjetsapo mitundu ya anthu!
Comment es-tu tombé du ciel, lucifer qui dès le matin te levais? Comment as-tu été renversé sur la terre, toi qui faisais des blessures aux nations?
13 Mu mtima mwako unkanena kuti, “Ndidzakwera mpaka kumwamba; ndidzakhazika mpando wanga waufumu pamwamba pa nyenyezi za Mulungu; ndidzakhala pa mpando waufumu pa phiri losonkhanirako, pamwamba penipeni pa phiri la kumpoto.
Qui disais dans ton cœur: Je monterai au ciel, sur les astres de Dieu j’élèverai mon trône; je m’assiérai sur la montagne du Testament, aux côtés de l’aquilon.
14 Ndidzakwera pamwamba pa mitambo; ndidzafanana ndi Wammwambamwamba.”
Je monterai sur la hauteur des nues, je serai semblable au Très-Haut.
15 Koma watsitsidwa mʼmanda pansi penipeni pa dzenje. (Sheol h7585)
Mais cependant tu seras traîné dans l’enfer, au profond de la fosse; (Sheol h7585)
16 Anthu akufa adzakupenyetsetsa nadzamalingalira za iwe nʼkumati, “Kodi uyu ndi munthu uja anagwedeza dziko lapansi ndi kunjenjemeretsa maufumu,
Ceux qui te verront se pencheront vers toi, et ils te considéreront et te diront: Est-ce là cet homme qui a troublé la terre, qui a ébranlé les royaumes;
17 munthu amene anasandutsa dziko lonse chipululu, amene anagwetsa mizinda yake ndipo sankalola kuti anthu ogwidwa abwerere kwawo?”
Qui a fait de l’univers un désert, et a détruit ses villes, et à ses captifs n’a pas ouvert la prison?
18 Mafumu onse a mitundu ya anthu akugona mwaulemu aliyense mʼmanda akeake.
Tous les rois des nations, tous se seront endormis dans la gloire, chacun dans sa maison.
19 Koma iwe watayidwa kunja kwa manda ako, ngati nthambi yowola ndi yonyansa. Mtembo wako waphimbidwa ndi anthu ophedwa; amene anabayidwa ndi lupanga, anatsikira mʼdzenje lamiyala ngati mtembo woponderezedwa.
Mais toi, tu as été jeté loin de ton sépulcre, comme un tronc inutile, et souillé, et enveloppé avec ceux qui ont été tués par le glaive et qui sont descendus au fond de la fosse comme un cadavre putréfié.
20 Sudzayikidwa nawo mʼmanda mwaulemu, chifukwa unawononga dziko lako ndi kupha anthu ako. Zidzukulu za anthu oyipa sizidzakumbukika nʼpangʼono pomwe.
Tu n’auras pas même part avec eux à la sépulture, parce que c’est toi qui as détruit entièrement ta terre, toi qui as tué ton peuple; la race des méchants n’existera pas éternellement.
21 Konzani malo woti muphere ana ake aamuna chifukwa cha machimo a makolo awo; kuti angadzuke ndi kulanda dziko lapansi ndi kulidzaza dziko lonselo ndi mizinda yawo.
Préparez ses enfants au massacre, à cause de l’iniquité de leurs pères ils ne s’élèveront pas, ils n’hériteront pas de la terre, et ils ne rempliront pas la face du globe de cités.
22 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ine ndidzathira nkhondo mzinda wa Babuloni. Ndidzachotseratu mu Babuloni dzina lake ndi onse otsaliramo. Ndiye kuti sipadzakhala ana kapena zidzukulu,” akutero Yehova.
Et je m’élèverai contre eux, dit le Seigneur des armées, et je perdrai le nom de Babylone, et les restes, et le germe, et la race, dit le Seigneur.
23 “Ndidzawusandutsa mzindawo malo okhalamo anungu ndiponso dambo lamatope; ndidzawusesa ndi tsache lowononga,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Et j’en ferai la possession du hérisson; j’en ferai des marais d’eaux, et je la balayerai avec un balai en la raclant, dit le Seigneur des armées.
24 Yehova Wamphamvuzonse walumbira kuti, “Ndithudi, monga ndaganizira ndidzachitadi choncho, ndipo monga momwe ndatsimikizira zidzakhala momwemo ndithu.
Le Seigneur des armées a juré, disant: Certainement, comme j’ai pensé, de même il en sera, et comme j’ai arrêté dans mon esprit,
25 Ndidzawawononga Asiriya mʼdziko langa; ndidzawapondereza ndi mapazi pa mapiri anga; ndidzachotsa goli lawo pa anthu anga, ndipo ndidzachotsa katundu wawo pa mapewa awo.”
Ainsi il arrivera; afin que je brise l’Assyrien dans ma terre, et que sur mes montagnes je le foule aux pieds, que son joug soit emporté loin d’eux, et que son fardeau soit enlevé de leur épaule.
26 Izi ndizo ndakonza kuti zichitike pa dziko lonse lapansi, ndatambasula dzanja pa anthu a mitundu yonse.
C’est là le dessein que j’ai formé sur toute la terre, et c’est là la main étendue sur toutes les nations.
27 Pakuti Yehova Wamphamvuzonse watsimikiza, ndipo ndani angamuletse? Dzanja lake latambasulidwa ndipo ndani angalibweze?
Car le Seigneur des armées l’a décrété; qui pourra infirmer son décret? et sa main est étendue, qui la détournera?
28 Uthenga uwu unabwera chaka chimene mfumu Ahazi anamwalira:
En l’année, à laquelle est mort le roi Achaz, a été faite cette prophétie accablante:
29 Musakondwere inu Afilisti nonse kuti Asiriya amene anali ngati ndodo yokukanthani anathedwa; chifukwa kuchokera ku njoka yomweyi (mfumu ya Aasiriya) mudzatuluka mphiri, ndipo chipatso chake chidzakhala njoka yaliwiro ndiponso yaululu.
Ne te réjouis pas, toi terre entière de Palestine, de ce qu’a été brisée la verge de celui qui te frappait; car de la race du serpent sortira un basilic, et ce qui en naîtra dévorera l’oiseau.
30 Osaukitsitsa adzapeza chakudya ndipo amphawi adzakhala mwamtendere. Koma anthu ako ndidzawawononga ndi njala, ndipo njalayo idzapha ngakhale opulumuka ako.
Et les plus indigents seront nourris, et les pauvres reposeront avec confiance; et je ferai mourir ta racine, et tes restes, je les tuerai.
31 Lirani kwambiri, anthu a pa chipata! Fuwulani kwambiri, anthu a mu mzinda! Njenjemerani ndi mantha, inu Afilisti nonse! Mtambo wa utsi ukuchokera kumpoto, ndipo palibe wamantha pakati pa ankhondo ake.
Pousse des hurlements, porte; crie, cité; toute la Palestine a été renversée; car c’est de l’aquilon que la fumée viendra; et il n’est personne qui fuira son armée.
32 Kodi tidzawayankha chiyani amithenga a ku Filisitiya? “Yehova wakhazikitsa Ziyoni, ndipo mu mzinda wakewu, anthu ozunzika apeza populumukira.”
Et que répondra-t-on aux messagers de la nation? Que c’est le Seigneur qui a fondé Sion, et qu’en lui espéreront les pauvres de son peuple.

< Yesaya 14 >