< Yesaya 12 >

1 Tsiku limenelo aliyense wa inu adzati: “Ndikukuyamikani, Inu Yehova; chifukwa ngakhale munandipsera mtima, mkwiyo wanu wachoka, ndipo mwanditonthoza.
Ын зиуа ачея вей зиче: „Те лауд, Доамне, кэч ай фост супэрат пе мине, дар мыния Та с-а потолит ши м-ай мынгыят!
2 Zoonadi, Mulungu ndiye Mpulumutsi wanga; ndidzamudalira ndipo sindidzachita mantha. Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga; Iye wakhala chipulumutso changa.”
Ятэ, Думнезеу есте избэвиря мя, вой фи плин де ынкредере ши ну мэ вой теме де нимик, кэч Домнул Думнезеу есте тэрия мя ши причина лауделор меле ши Ел м-а мынтуит.”
3 Mudzakondwera popeza Yehova ali ngati chitsime cha chipulumutso chanu.
Вець скоате апэ ку букурие дин извоареле мынтуирий
4 Tsiku limenelo mudzati: “Yamikani Yehova, tamandani dzina lake; mulengeze ntchito zake pakati pa mitundu ya anthu, ndipo mulalike kuti dzina lake ndi lopambana.
ши вець зиче ын зиуа ачея: „Лэудаць пе Домнул, кемаць Нумеле Луй, вестиць лукрэриле Луй принтре попоаре, помениць мэримя Нумелуй Луй!
5 Imbirani Yehova, pakuti wachita ntchito zazikulu; zimenezi zidziwike pa dziko lonse lapansi.
Кынтаць Домнулуй, кэч а фэкут лукрурь стрэлучите: сэ фие куноскуте ын тот пэмынтул!”
6 Fuwulani ndi kuyimba mwachimwemwe, inu anthu a ku Ziyoni; pakuti Woyerayo wa Israeli ndi wamkulu pakati panu.”
Стригэ де букурие ши веселие, локуитоаре а Сионулуй, кэч маре есте ын мижлокул тэу Сфынтул луй Исраел!

< Yesaya 12 >