< Yesaya 12 >
1 Tsiku limenelo aliyense wa inu adzati: “Ndikukuyamikani, Inu Yehova; chifukwa ngakhale munandipsera mtima, mkwiyo wanu wachoka, ndipo mwanditonthoza.
Iti dayta nga aldaw ket ibagayonto, “Agyamanak kenka O Yahweh. Ta uray no kaungetnak, bimmaaw ti pungtotmo, ket liniwliwanak.
2 Zoonadi, Mulungu ndiye Mpulumutsi wanga; ndidzamudalira ndipo sindidzachita mantha. Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga; Iye wakhala chipulumutso changa.”
Kitaenyo, ti Dios ti manangisalakanko; agtalekak ken saanakto nga agbuteng, ta ni Yahweh, wen, ni Yahweh ti pigsak ken kantak. Isuna ti nangisalakan kaniak.”
3 Mudzakondwera popeza Yehova ali ngati chitsime cha chipulumutso chanu.
Siraragsakkayonto nga agsakdo iti danum manipud kadagiti bubon ti pannakaisalakan.
4 Tsiku limenelo mudzati: “Yamikani Yehova, tamandani dzina lake; mulengeze ntchito zake pakati pa mitundu ya anthu, ndipo mulalike kuti dzina lake ndi lopambana.
Iti dayta nga aldaw kunaenyonto, “Agyamantayo kenni Yahweh ken awagantayo ti naganna; ibagayo kadagiti tattao dagiti aramidna, ipakaammoyo a ti nagana ket natan-ok.
5 Imbirani Yehova, pakuti wachita ntchito zazikulu; zimenezi zidziwike pa dziko lonse lapansi.
Kantaanyo ni Yahweh, gapu kadagiti nadayag a banbanag nga inaramidna; maipakaammo koma daytoy iti entero a daga.
6 Fuwulani ndi kuyimba mwachimwemwe, inu anthu a ku Ziyoni; pakuti Woyerayo wa Israeli ndi wamkulu pakati panu.”
Agdir-i iti napigsa ken agpukkawkayo gapu iti rag-o, dakayo nga agnanaed iti Sion, ta naindaklan ti Nasantoan ti Israel nga adda iti nagtetengngaanyo.”