< Yesaya 12 >

1 Tsiku limenelo aliyense wa inu adzati: “Ndikukuyamikani, Inu Yehova; chifukwa ngakhale munandipsera mtima, mkwiyo wanu wachoka, ndipo mwanditonthoza.
Et tu diras en ce jour-là: Je vous glorifierai. Seigneur, parce que vous avez été irrité contre moi; mais votre fureur s’est tournée, et vous m’avez consolé.
2 Zoonadi, Mulungu ndiye Mpulumutsi wanga; ndidzamudalira ndipo sindidzachita mantha. Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga; Iye wakhala chipulumutso changa.”
Voilà que Dieu est mon sauveur, j’agirai avec confiance, et je ne craindrai pas, parce que ma force et ma louange, c’est le Seigneur, et qu’il est devenu mon salut.
3 Mudzakondwera popeza Yehova ali ngati chitsime cha chipulumutso chanu.
Vous puiserez avec joie des eaux des fontaines du Sauveur;
4 Tsiku limenelo mudzati: “Yamikani Yehova, tamandani dzina lake; mulengeze ntchito zake pakati pa mitundu ya anthu, ndipo mulalike kuti dzina lake ndi lopambana.
Et vous direz en ce jour-là: Glorifiez le Seigneur, et invoquez son nom; faites connaître parmi les nations ses œuvres; souvenez-vous que sublime est son nom.
5 Imbirani Yehova, pakuti wachita ntchito zazikulu; zimenezi zidziwike pa dziko lonse lapansi.
Chantez le Seigneur, il a agi avec magnificence; annoncez cela dans toute la terre.
6 Fuwulani ndi kuyimba mwachimwemwe, inu anthu a ku Ziyoni; pakuti Woyerayo wa Israeli ndi wamkulu pakati panu.”
Exulte et loue, habitation de Sion, parce que grand est au milieu de toi le saint d’Israël.

< Yesaya 12 >