< Yesaya 12 >
1 Tsiku limenelo aliyense wa inu adzati: “Ndikukuyamikani, Inu Yehova; chifukwa ngakhale munandipsera mtima, mkwiyo wanu wachoka, ndipo mwanditonthoza.
En ce jour-là, tu diras: « Je te louerai, Yahvé, car tu t'es mis en colère contre moi, mais ta colère s'est détournée et tu m'as consolé.
2 Zoonadi, Mulungu ndiye Mpulumutsi wanga; ndidzamudalira ndipo sindidzachita mantha. Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga; Iye wakhala chipulumutso changa.”
Voici, Dieu est mon salut. Je me confie, je ne crains rien, car Yahvé est ma force et mon chant, et il est mon salut ».
3 Mudzakondwera popeza Yehova ali ngati chitsime cha chipulumutso chanu.
C'est donc avec joie que vous puiserez de l'eau aux puits du salut.
4 Tsiku limenelo mudzati: “Yamikani Yehova, tamandani dzina lake; mulengeze ntchito zake pakati pa mitundu ya anthu, ndipo mulalike kuti dzina lake ndi lopambana.
En ce jour-là, vous direz: « Rendez grâce à Yahvé! Invoquez son nom! Annoncez ses exploits parmi les peuples! Proclamez que son nom est exalté!
5 Imbirani Yehova, pakuti wachita ntchito zazikulu; zimenezi zidziwike pa dziko lonse lapansi.
Chantez à Yahvé, car il a fait des choses excellentes! Qu'on le sache par toute la terre!
6 Fuwulani ndi kuyimba mwachimwemwe, inu anthu a ku Ziyoni; pakuti Woyerayo wa Israeli ndi wamkulu pakati panu.”
Criez à haute voix et poussez des cris, habitants de Sion, car le Saint d'Israël est grand au milieu de vous! »