< Yesaya 12 >

1 Tsiku limenelo aliyense wa inu adzati: “Ndikukuyamikani, Inu Yehova; chifukwa ngakhale munandipsera mtima, mkwiyo wanu wachoka, ndipo mwanditonthoza.
And thou schalt seie in that dai, Lord, Y schal knouleche to thee, for thou were wrooth to me; thi strong venieaunce is turned, and thou hast coumfortid me.
2 Zoonadi, Mulungu ndiye Mpulumutsi wanga; ndidzamudalira ndipo sindidzachita mantha. Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga; Iye wakhala chipulumutso changa.”
Lo! God is my sauyour, Y schal do feithfuli, and Y schal not drede. For whi the Lord is my strengthe and my preysyng, and he is maad to me in to helthe.
3 Mudzakondwera popeza Yehova ali ngati chitsime cha chipulumutso chanu.
Ye schulen drawe watris with ioie of the wellis of the sauyour.
4 Tsiku limenelo mudzati: “Yamikani Yehova, tamandani dzina lake; mulengeze ntchito zake pakati pa mitundu ya anthu, ndipo mulalike kuti dzina lake ndi lopambana.
And ye schulen seie in that dai, Knouleche ye to the Lord, and clepe ye his name in to help; make ye knowun hise fyndyngis among puplis; haue ye mynde, that his name is hiy.
5 Imbirani Yehova, pakuti wachita ntchito zazikulu; zimenezi zidziwike pa dziko lonse lapansi.
Synge ye to the Lord, for he hath do worschipfuli; telle ye this in al erthe.
6 Fuwulani ndi kuyimba mwachimwemwe, inu anthu a ku Ziyoni; pakuti Woyerayo wa Israeli ndi wamkulu pakati panu.”
Thou dwellyng of Syon, make ful out ioie, and preise; for whi the hooli of Israel is greet in the myddis of thee.

< Yesaya 12 >