< Yesaya 12 >

1 Tsiku limenelo aliyense wa inu adzati: “Ndikukuyamikani, Inu Yehova; chifukwa ngakhale munandipsera mtima, mkwiyo wanu wachoka, ndipo mwanditonthoza.
On that day you will say, “I will give thanks to you, Yahweh. For though you were angry with me, your wrath has turned away, and you have comforted me.
2 Zoonadi, Mulungu ndiye Mpulumutsi wanga; ndidzamudalira ndipo sindidzachita mantha. Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga; Iye wakhala chipulumutso changa.”
See, God is my salvation; I will trust and will not fear, for Yahweh, yes, Yahweh is my strength and song. He has become my salvation.”
3 Mudzakondwera popeza Yehova ali ngati chitsime cha chipulumutso chanu.
With joy you will draw water from the wells of salvation.
4 Tsiku limenelo mudzati: “Yamikani Yehova, tamandani dzina lake; mulengeze ntchito zake pakati pa mitundu ya anthu, ndipo mulalike kuti dzina lake ndi lopambana.
On that day you will say, “Give thanks to Yahweh and call upon his name; declare his deeds among the peoples, proclaim that his name is exalted.
5 Imbirani Yehova, pakuti wachita ntchito zazikulu; zimenezi zidziwike pa dziko lonse lapansi.
Sing to Yahweh, for he has done glorious things; let this be known throughout the earth.
6 Fuwulani ndi kuyimba mwachimwemwe, inu anthu a ku Ziyoni; pakuti Woyerayo wa Israeli ndi wamkulu pakati panu.”
Cry aloud and shout for joy, you inhabitants of Zion, for great in your midst is the Holy One of Israel.”

< Yesaya 12 >