< Yesaya 11 >
1 Padzatuluka mphukira pa tsinde la Yese ndipo nthambi idzaphukira kuchokera ku mizu yake.
И изыдет жезл из корене Иессеова, и цвет от корене его взыдет:
2 Mzimu wa Yehova udzakhala pa iye Mzimu wanzeru ndi wa kumvetsa zinthu, Mzimu wauphungu ndi wamphamvu, Mzimu wachidziwitso ndi wakuopa Yehova.
и почиет на нем Дух Божий, дух премудрости и разума, дух совета и крепости, дух ведения и благочестия:
3 Ndipo kuopa Yehova ndiye chidzakhale chinthu chomukondweretsa. Iye sadzaweruza potsata zooneka pamaso, kapena kugamula mlandu potsata zakumva;
исполнит его дух страха Божия: не по славе судити имать, ниже по глаголанию обличит,
4 koma amphawi adzawaweruza mwachilungamo, adzaweruza mwachilungamo mlandu wa anthu osauka a dziko lapansi. Iye adzakantha dziko lapansi ndi mawu ake; atalamula Iyeyu anthu oyipa adzaphedwa.
но судит правдою смиренному суд и обличит правостию смиренныя земли, и поразит землю словом уст Своих и духом устен убиет нечестиваго:
5 Chilungamo chidzakhala ngati lamba wake ndipo kukhulupirika kudzakhala ngati chomangira mʼchiwuno mwake.
и будет препоясан правдою о чреслех Своих и истиною обвит по ребрам Своим:
6 Mʼmbulu udzakhala pamodzi ndi mwana wankhosa, kambuku adzagona pansi pamodzi ndi mwana wambuzi, mwana wangʼombe ndi mwana wa mkango adzadyera limodzi ndipo mwana wamngʼono adzaziweta.
и пастися будут вкупе волк с агнцем, и рысь почиет со козлищем, и телец и юнец и лев вкупе пастися будут, и отроча мало поведет я:
7 Ngʼombe yayikazi ndi chimbalangondo zidzadya pamodzi, ana awo adzagona pamodzi, ndipo mkango udzadya udzu ngati ngʼombe.
и вол и медведь вкупе пастися будут, и вкупе дети их будут, и лев аки вол ясти будет плевы:
8 Mwana wakhanda adzasewera pa dzenje la mamba, ndipo mwana wamngʼono adzapisa dzanja lake ku phanga la mphiri osalumidwa.
и отроча младо на пещеры аспидов и на ложе изчадий аспидских руку возложит:
9 Sipadzakhala chilichonse chopweteka kapena chowononga pa phiri lopatulika la Yehova, pakuti anthu a dziko lapansi adzadzaza ndi nzeru yotha kudziwa Yehova monga momwe nyanja imadzazira ndi madzi.
и не сотворят зла, ни возмогут погубити ни когоже на горе святей Моей: яко наполнися вся земля ведения Господня, аки вода многа покры море.
10 Tsiku limenelo mfumu yatsopano yochokera pa Muzu wa Yese idzakhala ngati chizindikiro kwa anthu a mitundu yonse. Mitundu ya anthu idzasonkhana kwa Iye, ndipo malo awo okhalapo adzakhala aulemerero.
И будет в день оный корень Иессеов, и востаяй владети языки, на того языцы уповати будут: и будет покой его честь.
11 Tsiku limenelo Ambuye adzatambasula dzanja lake kachiwiri kuti awombole anthu ake otsalira ku Asiriya, ku Igupto, ku Patirosi, Kusi, ku Elamu, ku Sinana, ku Hamati ndi pa zilumba za nyanja yamchere.
И будет в день оный, приложит Господь показати руку Свою, еже возревновати по останку прочему людий, иже аще останет от Ассириов и от Египта, и Вавилона и от Ефиопии, и от Еламитов и от Востоков солнца, и от Аравии и от островов морских.
12 Adzakwezera mitundu ya anthu mbendera, ndipo adzasonkhanitsa otayika a ku Israeli; Iye adzasonkhanitsa anthu obalalika a ku Yuda kuchokera ku mbali zonse zinayi za dziko lapansi.
И воздвигнет знамение в языки, и соберет погибшыя Израилевы, и расточенныя Иудины соберет от четырех крил земли.
13 Nsanje ya Efereimu idzatha, ndipo adani a Yuda adzatha; Efereimu sadzachitira nsanje Yuda, ngakhale Yuda sadzamuda Efereimu.
И отимется ревность Ефремова, и врази Иудины погибнут: Ефрем не возревнует Иуде, и Иуда не оскорбит Ефрема.
14 Yuda ndi Efereimu adzathira nkhondo pa Afilisti mbali ya kumadzulo; ndipo onsewo pamodzi adzalanda zinthu za anthu a kummawa. Adzalimbana ndi Edomu ndi Mowabu, ndipo Aamoni adzawagonjera.
И полетят в кораблех иноплеменничих, море купно пленят, и сущих от Восток солнца, и Идумею: и на Моава первее руки возложат, сынове же Аммони первии покорятся.
15 Yehova adzaphwetsa mwendo wa nyanja ya Igupto; adzatambasula dzanja lake ndipo adzawombetsa mphepo yotentha pa mtsinje wa Yufurate. Iye adzawugawa mtsinjewo kukhala timitsinje tisanu ndi tiwiri kuti anthu athe kuwoloka powuma atavala nsapato.
И опустошит Господь море Египетское и возложит руку Свою на реку духом пресильным: и поразит на седмь дебрий, якоже преходити ю во обувении:
16 Padzakhala msewu waukulu woti ayendepo anthu ake otsalira amene anatsalira ku Asiriya, monga mmene panali msewu waukulu woyendapo Israeli pamene amachokera ku Igupto.
и будет прошествие людем Моим оставшым во Египте, и будет Израилю, якоже в день, егда изыде от земли Египетския.