< Yesaya 11 >

1 Padzatuluka mphukira pa tsinde la Yese ndipo nthambi idzaphukira kuchokera ku mizu yake.
Et il sortira un rejeton de la racine de Jessé, et une fleur s’élèvera de sa racine,
2 Mzimu wa Yehova udzakhala pa iye Mzimu wanzeru ndi wa kumvetsa zinthu, Mzimu wauphungu ndi wamphamvu, Mzimu wachidziwitso ndi wakuopa Yehova.
Et l’esprit du Seigneur reposera sur lui; l’esprit de sagesse et d’intelligence, l’esprit de conseil et de force, l’esprit de science et de piété.
3 Ndipo kuopa Yehova ndiye chidzakhale chinthu chomukondweretsa. Iye sadzaweruza potsata zooneka pamaso, kapena kugamula mlandu potsata zakumva;
L’esprit de crainte du Seigneur le remplira. Il ne jugera pas d’après ce qu’auront vu les yeux, et il ne condamnera pas d’après ce qu’auront ouï les oreilles.
4 koma amphawi adzawaweruza mwachilungamo, adzaweruza mwachilungamo mlandu wa anthu osauka a dziko lapansi. Iye adzakantha dziko lapansi ndi mawu ake; atalamula Iyeyu anthu oyipa adzaphedwa.
Mais il jugera les pauvres dans la justice, et il se prononcera avec équité pour les hommes paisibles de la terre; et il frappera la terre de la verge de sa bouche, et du souffle de ses lèvres il tuera l’impie.
5 Chilungamo chidzakhala ngati lamba wake ndipo kukhulupirika kudzakhala ngati chomangira mʼchiwuno mwake.
Et la justice sera la ceinture de ses reins, et la fidélité le ceinturon de ses flancs
6 Mʼmbulu udzakhala pamodzi ndi mwana wankhosa, kambuku adzagona pansi pamodzi ndi mwana wambuzi, mwana wangʼombe ndi mwana wa mkango adzadyera limodzi ndipo mwana wamngʼono adzaziweta.
Le loup habitera avec l’agneau, et le léopard se couchera près du chevreau; le jeune taureau, et le Mon, et la brebis demeureront ensemble, et un petit enfant les conduira.
7 Ngʼombe yayikazi ndi chimbalangondo zidzadya pamodzi, ana awo adzagona pamodzi, ndipo mkango udzadya udzu ngati ngʼombe.
Le veau et l’ours iront aux mêmes pâturages; leurs petits se reposeront ensemble; le lion comme le bœuf mangera la paille.
8 Mwana wakhanda adzasewera pa dzenje la mamba, ndipo mwana wamngʼono adzapisa dzanja lake ku phanga la mphiri osalumidwa.
Et l’enfant à la mamelle se jouera sur le trou de l’aspic; et celui qui viendra d’être sevré portera sa main dans la caverne du basilic.
9 Sipadzakhala chilichonse chopweteka kapena chowononga pa phiri lopatulika la Yehova, pakuti anthu a dziko lapansi adzadzaza ndi nzeru yotha kudziwa Yehova monga momwe nyanja imadzazira ndi madzi.
Ils ne nuiront pas, et ils ne tueront pas sur toute ma montagne sainte; parce que la terre est remplie de la connaissance du Seigneur, comme les eaux qui couvrent la mer.
10 Tsiku limenelo mfumu yatsopano yochokera pa Muzu wa Yese idzakhala ngati chizindikiro kwa anthu a mitundu yonse. Mitundu ya anthu idzasonkhana kwa Iye, ndipo malo awo okhalapo adzakhala aulemerero.
En ce jour-là viendra la racine de Jessé qui est comme l’étendard des peuples; c’est à lui que les nations adresseront leurs prières, et son sépulcre sera glorieux.
11 Tsiku limenelo Ambuye adzatambasula dzanja lake kachiwiri kuti awombole anthu ake otsalira ku Asiriya, ku Igupto, ku Patirosi, Kusi, ku Elamu, ku Sinana, ku Hamati ndi pa zilumba za nyanja yamchere.
Et il arrivera en ce jour-là que le Seigneur étendra une seconde fois sa main pour posséder le reste de son peuple, qui aura échappé aux Assyriens, et à l’Egypte, et à Phétros, et à l’Ethiopie, et à Elam et à Sennaar, et à Emath, et aux îles de la mer.
12 Adzakwezera mitundu ya anthu mbendera, ndipo adzasonkhanitsa otayika a ku Israeli; Iye adzasonkhanitsa anthu obalalika a ku Yuda kuchokera ku mbali zonse zinayi za dziko lapansi.
Et il élèvera son étendard parmi les nations, il réunira les fugitifs d’Israël, et les dispersés de Juda, il les rassemblera des quatre coins de la terre.
13 Nsanje ya Efereimu idzatha, ndipo adani a Yuda adzatha; Efereimu sadzachitira nsanje Yuda, ngakhale Yuda sadzamuda Efereimu.
Et la jalousie d’Ephraïm sera détruite, et les ennemis de Juda périront; Ephraïm n’enviera pas Juda, et Juda ne combattra pas contre Ephraïm.
14 Yuda ndi Efereimu adzathira nkhondo pa Afilisti mbali ya kumadzulo; ndipo onsewo pamodzi adzalanda zinthu za anthu a kummawa. Adzalimbana ndi Edomu ndi Mowabu, ndipo Aamoni adzawagonjera.
Et ils voleront sur les épaules des Philistins par la mer; ils pilleront ensemble les fils de l’Orient. L’Idumée et Moab seront la première capture de leur main, et les fils d’Ammon leur obéiront.
15 Yehova adzaphwetsa mwendo wa nyanja ya Igupto; adzatambasula dzanja lake ndipo adzawombetsa mphepo yotentha pa mtsinje wa Yufurate. Iye adzawugawa mtsinjewo kukhala timitsinje tisanu ndi tiwiri kuti anthu athe kuwoloka powuma atavala nsapato.
Et le Seigneur mettra à sec la langue de la mer d’Égypte, et il lèvera sa main sur le fleuve, il l’agitera par la force de son souffle, et il le frappera dans ses sept ruisseaux, en sorte qu’on le passera tout chaussé.
16 Padzakhala msewu waukulu woti ayendepo anthu ake otsalira amene anatsalira ku Asiriya, monga mmene panali msewu waukulu woyendapo Israeli pamene amachokera ku Igupto.
Et il y aura une voie pour le reste de mon peuple qui aura échappé aux Assyriens, comme il y en eut une pour Israël, au jour auquel il monta de la terre d’Egypte.

< Yesaya 11 >