< Yesaya 10 >

1 Tsoka kwa anthu amene amapanga malamulo opanda chilungamo, kwa iwo amene amalemba zongovutitsa anzawo,
Тешко онима који постављају законе неправедне и који пишу неправду,
2 kuwalanda anthu osauka ufulu wawo ndi kumana chilungamo osautsidwa pakati pa anthu anga, amalanda zinthu za akazi amasiye ndi kubera ana amasiye.
Да одбију од суда убоге, и да отимају правицу сиромасима народа мог, да би им плен биле удовице и сироте грабеж.
3 Kodi mudzatani pa tsiku la chilango, pofika chiwonongeko chochokera kutali? Kodi mudzathawira kwa yani kuti akuthandizeni? Nanga chuma chanu mudzachisiya kuti?
А шта ћете чинити у дан похођења и погибли која ће доћи издалека? Коме ћете прибећи за помоћ? Где ли ћете оставити славу своју?
4 Kudzatsala nʼkungozolika mwamanyazi pakati pa anthu ogwidwa kapena kufa pamodzi ndi ophedwa. Komabe pa zonsezi mkwiyo wake sunawachokere, mkono wake uli chitambasulire.
Да се не би унизила међу робље и међу побијене пала? Код свега тога неће се одвратити гнев Његов, него ће рука Његова још бити подигнута.
5 “Tsoka kwa mfumu ya ku Asiriya, chikwapu cha mkwiyo wanga, iye ndiye ndodo ya mkwiyo wanga!
Тешко Асиру, шиби гнева мог, ако и јесте палица у руци његовој моја јарост.
6 Ndidzamutuma kukalimbana ndi mtundu wosapembedza Mulungu, ndidzamutumiza kukalimbana ndi anthu amene amandikwiyitsa Ine, kukafunkha ndi kulanda chuma, ndi kuwapondereza pansi ngati matope a mʼmisewu.
На народ лицемерни послаћу га, и заповедићу му за народ на који се гневим, да плени и отима, и да га изгази као блато на улицама.
7 Koma izi si zimene akufuna kukachita, izi si zimene zili mʼmaganizo mwake; cholinga chake ndi kukawononga, kukapulula mitundu yambiri ya anthu.
Али он неће тако мислити и срце његово неће тако судити, него му је у срцу да затре и истреби многе народе.
8 Iye akuti, ‘Kodi atsogoleri anga ankhondo si mafumu okhaokha?’
Јер ће рећи: Кнезови моји нису ли сви цареви?
9 ‘Kodi Kalino sanagonjetsedwe monga Karikemesi? Kodi Hamati sali ngati Aripadi, nanga Samariya sali ngati Damasiko?
Није ли Халан као Хархемис? Није ли Емат као Арфад? Није ли Самарија као Дамаск?
10 Dzanja langa linakantha maufumu a anthu opembedza mafano, mafumu amene mafano awo ndi aakulu kupambana Yerusalemu ndi Samariya;
Како је рука моја нашла царства лажних богова, којих ликови беху јачи од јерусалимских и самаријских,
11 nanga Ine nʼkulephera kodi kuwononga Yerusalemu pamodzi ndi mafano ake monga ndinakanthira Samariya pamodzi ndi mafano ake?’”
Нећу ли учинити Јерусалиму и његовим лажним боговима онако како сам учинио Самарији и њеним лажним боговима?
12 Ambuye akadzamaliza ntchito yonse yolanga phiri la Ziyoni ndi Yerusalemu adzalanganso mfumu ya ku Asiriya chifukwa cha kudzitama ndi kunyada kwake.
Али кад сврши Господ све дело своје на гори сионској и у Јерусалиму, тада ћу обићи плод охолог срца цара асирског и славу поноситих очију његових.
13 Pakuti mfumuyo ikuti, “‘Ndachita zimenezi ndi dzanja langa, ndiponso ndi nzeru zanga, chifukwa ndine wozindikira zinthu. Ndinachotsa malire a mitundu ya anthu, ndinafunkha chuma chawo; ndinagonjetsa mafumu awo monga munthu wamphamvu.
Јер рече: Крепошћу руке своје учиних и мудрошћу својом, јер сам разуман; и преместих међе народима и благо њихово заплених и као јунак оборих становнике.
14 Dzanja langa lagwira chuma cha mitundu ya anthu ngati momwe munthu amagwirira chisa cha mbalame, ngati momwe anthu amatolera mazira osiyidwa, motero inenso ndinasonkhanitsa mayiko onse; palibe mbalame imene inakupiza mapiko ake, kapena kuyasama kukamwa kuti ilire.’”
И рука моја нађе као гнездо богатство у народа, и како се купе јаја остављена тако покупих сву земљу, и не би никога да махне крилом или да отвори уста и писне.
15 Kodi nkhwangwa ingathe kudzikuza kupambana woyigwiritsa ntchito, kapena macheka angathe kudzikuza kupambana wowagwiritsa ntchito? Ndiye kukhala ngati kuti chikwapu chikuzunguza munthu amene wachinyamula, kapena ngati kuti ndodo ikuopseza amene wayinyamula!
Хоће ли се секира величати над оним који њом сече? Хоће ли се пила разметати над оним који њом ради? Као да би прут махао оним који га дигне, као да би се хвалио штап да није од дрвета.
16 Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova Wamphamvuzonse adzatumiza matenda owondetsa kwa ankhondo amphamvu; kunyada kwa mfumuyo kudzapsa ndi moto wosazima.
Зато ће Господ, Господ над војскама, пустити на претиле његове мршу, и славу ће његову потпалити да гори као огањ.
17 Mulungu, Kuwala kwa Israeli, adzakhala ngati moto, Woyera uja wa Israeli adzakhala ngati malawi a moto. Motowo udzawatentha ndi kuwapsereza ngati minga ndi mkandankhuku pa tsiku limodzi.
Јер ће видело Израиљево бити огањ, и Светац ће његов бити пламен, и упалиће и сажећи трње његово и чкаљ његов у један дан.
18 Ankhondo ake adzawonongedwa ngati nkhalango yayikulu ndi ngati nthaka yachonde.
И красоту шуме његове и њиве његове, од душе до тела, уништиће, и биће као бегунац кад изнемогне.
19 Mitengo yotsalira ya mʼnkhalango zake idzakhala yochepa kwambiri, yoti ndi mwana yemwe ndi kuyiwerenga.
И шта остане дрвета шуме његове, биће мало, да би их дете могло пописати.
20 Tsiku limenelo otsalira a ku Israeli, opulumuka a nyumba ya Yakobo, sadzadaliranso anthu amene anawakantha, koma adzadalira Yehova, Woyerayo wa Israeli.
И у то време остатак Израиљев и који се избаве у дому Јаковљевом неће се више ослањати на оног ко их бије, него ће се ослањати на Господа Свеца Израиљевог истином.
21 Otsalira adzabwerera, otsalira a Yakobo adzabwerera kwa Mulungu Wamphamvu.
Остатак ће се обратити, остатак Јаковљев, к Богу силном.
22 Iwe Israeli, ngakhale anthu ako achuluke ngati mchenga wa ku nyanja, otsala okha ndiwo adzabwerere. Chiwonongeko chalamulidwa, chidzaonetsa chilungamo chosefukira.
Јер ако буде народа твог, Израиљу, као песка морског, остатак ће се његов обратити. Погибао је одређена, разлиће се правда.
23 Ambuye Yehova Wamphamvuzonse adzawononga ndithu dziko lonse monga momwe analamulira.
Јер ће Господ, Господ над војскама, извршити погибао одређену у свој земљи.
24 Nʼchifukwa chake, Ambuye Yehova Wamphamvuzonse akunena kuti, “Inu anthu anga okhala mu Ziyoni, musawaope Asiriya, amene amakukanthani ndi ndodo nakumenyani ndi zibonga monga mmene Igupto anachitira.
Зато овако вели Господ, Господ над војскама: Не бој се Асирца, народе мој, који наставаш на гори Сиону; прутом ће те ударити и штап свој подигнуће на те као у Мисиру.
25 Patsala pangʼonongʼono kuti mkwiyo wanga uchoke pa inu ndipo ndidzaonetsa ukali wanga pa iwo mpaka kuwawononga.”
Јер још мало, и гнев ће престати; тада ће се јарост моја обратити на њихову погибао.
26 Yehova Wamphamvuzonse adzawakwapula ndi chikwapu, monga momwe anakwapulira Amidiyani ku thanthwe la Orebu; ndipo adzatukula ndodo yake pa madzi ndikuwalanga monga analangira Igupto pa nyanja.
Јер ће подигнути на њ Господ над војскама бич, те ће бити као расап мадијански код камена Орива и као штап његов на мору, и подигнуће га као у Мисиру.
27 Tsiku limenelo katundu wawo adzachotsedwa pa mapewa anu, goli lawo lidzachoka mʼkhosi mwanu; golilo lidzathyoka chifukwa cha kunenepa kwambiri.
И тада ће се скинути бреме његово с рамена твог и јарам његов с врата твог, и изломиће се јарам од помазања.
28 Adani alowa mu Ayati apyola ku Migironi; asunga katundu wawo ku Mikimasi.
Дође у Ајат, прође у Мигрон, у Михмасу распрти пртљаг свој.
29 Adutsa pa mpata uja, ndipo akuti, “Tikagona ku Geba” Rama akunjenjemera; Gibeya, mzinda wa Saulo ukuthawa.
Пођоше кланцем, у Гаваји заноћише, препаде се Рама, Гаваја Саулова побеже.
30 Lilani mokweza, inu anthu a ku Galimu! Tchera khutu, iwe Laisa! Iwe Anatoti wosauka!
Вичи гласно, кћери Галимова; нек се чује у Лаис, јадни Анатоте!
31 Anthu a ku Madimena akuthawa; anthu a ku Gebimu bisalani.
Мадмина побеже, становници гевимски утекоше.
32 Lero lomwe lino adaniwo adzayima ku Nobu; adzagwedeza mikono yawo, kuopseza anthu a ku Ziyoni, pa phiri la Yerusalemu.
Још један дан, па ће стајати у Нову, махнуће руком својом на гору кћери сионске, на хум јерусалимски.
33 Taonani, Ambuye Yehova Wamphamvuzonse, adzadula mwamphamvu nthambi za mitengo, mitengo yodzikweza idzadulidwa, mitengo yayitali idzagwetsedwa.
Гле, Господ, Господ над војскама, окресаће силом гране; шта је високо посећи ће, и шта је уздигнуто снизиће.
34 Yehova adzadula ndi nkhwangwa mitengo ya mʼnkhalango yowirira; Lebanoni adzagwa pamaso pa Wamphamvu.
И густу ће шуму исећи секиром, и Ливан ће пасти од Силнога.

< Yesaya 10 >