< Yesaya 10 >
1 Tsoka kwa anthu amene amapanga malamulo opanda chilungamo, kwa iwo amene amalemba zongovutitsa anzawo,
Malheur à ceux qui décrètent des ordonnances injustes, Et aux rédacteurs qui écrivent des ordonnances oppressives
2 kuwalanda anthu osauka ufulu wawo ndi kumana chilungamo osautsidwa pakati pa anthu anga, amalanda zinthu za akazi amasiye ndi kubera ana amasiye.
pour priver de justice les indigents, Et pour dépouiller de leurs droits les pauvres de mon peuple, Afin que les veuves soient leur butin, Et qu'ils fassent de l'orphelin leur proie!
3 Kodi mudzatani pa tsiku la chilango, pofika chiwonongeko chochokera kutali? Kodi mudzathawira kwa yani kuti akuthandizeni? Nanga chuma chanu mudzachisiya kuti?
Que ferez-vous au jour du châtiment, au jour de la désolation qui viendra de loin? Vers qui fuiras-tu pour demander du secours? Où laisserez-vous vos richesses?
4 Kudzatsala nʼkungozolika mwamanyazi pakati pa anthu ogwidwa kapena kufa pamodzi ndi ophedwa. Komabe pa zonsezi mkwiyo wake sunawachokere, mkono wake uli chitambasulire.
Ils ne se prosterneront que sous les prisonniers, et tomberont sous les morts. Pour autant, sa colère n'est pas détournée, mais sa main est encore tendue.
5 “Tsoka kwa mfumu ya ku Asiriya, chikwapu cha mkwiyo wanga, iye ndiye ndodo ya mkwiyo wanga!
Hélas Assyrien, la verge de ma colère, le bâton dans la main duquel est ma fureur!
6 Ndidzamutuma kukalimbana ndi mtundu wosapembedza Mulungu, ndidzamutumiza kukalimbana ndi anthu amene amandikwiyitsa Ine, kukafunkha ndi kulanda chuma, ndi kuwapondereza pansi ngati matope a mʼmisewu.
Je l'envoie contre une nation profane, et contre le peuple qui m'irrite, je lui donne l'ordre de prendre le pillage et le butin, et de les fouler comme la boue des rues.
7 Koma izi si zimene akufuna kukachita, izi si zimene zili mʼmaganizo mwake; cholinga chake ndi kukawononga, kukapulula mitundu yambiri ya anthu.
Mais ce n'est pas ce qu'il veut, et ce n'est pas ce que son cœur pense; mais il a dans le cœur de détruire, et d'exterminer non pas quelques nations.
8 Iye akuti, ‘Kodi atsogoleri anga ankhondo si mafumu okhaokha?’
Car il dit: « Tous mes princes ne sont-ils pas des rois?
9 ‘Kodi Kalino sanagonjetsedwe monga Karikemesi? Kodi Hamati sali ngati Aripadi, nanga Samariya sali ngati Damasiko?
Calno n'est-elle pas comme Carménich? Hamath n`est-elle pas comme Arpad? Samarie n'est-elle pas comme Damas? »
10 Dzanja langa linakantha maufumu a anthu opembedza mafano, mafumu amene mafano awo ndi aakulu kupambana Yerusalemu ndi Samariya;
Comme ma main a trouvé les royaumes des idoles, dont les images gravées dépassaient celles de Jérusalem et de Samarie,
11 nanga Ine nʼkulephera kodi kuwononga Yerusalemu pamodzi ndi mafano ake monga ndinakanthira Samariya pamodzi ndi mafano ake?’”
ne ferai-je pas, comme j'ai fait à Samarie et à ses idoles, à Jérusalem et à ses idoles?
12 Ambuye akadzamaliza ntchito yonse yolanga phiri la Ziyoni ndi Yerusalemu adzalanganso mfumu ya ku Asiriya chifukwa cha kudzitama ndi kunyada kwake.
C'est pourquoi, lorsque l'Éternel aura accompli toute son œuvre sur la montagne de Sion et sur Jérusalem, je punirai le fruit du cœur orgueilleux et volontaire du roi d'Assyrie, et l'insolence de ses regards arrogants.
13 Pakuti mfumuyo ikuti, “‘Ndachita zimenezi ndi dzanja langa, ndiponso ndi nzeru zanga, chifukwa ndine wozindikira zinthu. Ndinachotsa malire a mitundu ya anthu, ndinafunkha chuma chawo; ndinagonjetsa mafumu awo monga munthu wamphamvu.
Car il a dit: « C'est par la force de ma main que j'ai agi, et par ma sagesse, car j'ai de l'intelligence. J'ai fait disparaître les limites des peuples, et j'ai dérobé leurs trésors. Comme un vaillant homme, j'ai abattu leurs chefs.
14 Dzanja langa lagwira chuma cha mitundu ya anthu ngati momwe munthu amagwirira chisa cha mbalame, ngati momwe anthu amatolera mazira osiyidwa, motero inenso ndinasonkhanitsa mayiko onse; palibe mbalame imene inakupiza mapiko ake, kapena kuyasama kukamwa kuti ilire.’”
Ma main a trouvé les richesses des peuples comme un nid, et comme on recueille des œufs abandonnés, j'ai recueilli toute la terre. Il n'y en a pas un qui ait remué l'aile, qui ait ouvert la bouche, ou qui ait gazouillé. »
15 Kodi nkhwangwa ingathe kudzikuza kupambana woyigwiritsa ntchito, kapena macheka angathe kudzikuza kupambana wowagwiritsa ntchito? Ndiye kukhala ngati kuti chikwapu chikuzunguza munthu amene wachinyamula, kapena ngati kuti ndodo ikuopseza amene wayinyamula!
La hache se vante-t-elle de celui qui coupe? La scie doit-elle s'élever au-dessus de celui qui la scie? Comme si une verge devait élever ceux qui la soulèvent, ou comme si un bâton devait élever quelqu'un qui n'est pas du bois.
16 Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova Wamphamvuzonse adzatumiza matenda owondetsa kwa ankhondo amphamvu; kunyada kwa mfumuyo kudzapsa ndi moto wosazima.
C'est pourquoi l'Éternel, l'Éternel des armées, enverra parmi ses gros la maigreur, et sous sa gloire s'allumera une ardeur comme celle d'un feu.
17 Mulungu, Kuwala kwa Israeli, adzakhala ngati moto, Woyera uja wa Israeli adzakhala ngati malawi a moto. Motowo udzawatentha ndi kuwapsereza ngati minga ndi mkandankhuku pa tsiku limodzi.
La lumière d'Israël sera comme un feu, et son Saint comme une flamme; et il brûlera et dévorera ses épines et ses ronces en un seul jour.
18 Ankhondo ake adzawonongedwa ngati nkhalango yayikulu ndi ngati nthaka yachonde.
Il consumera la gloire de sa forêt et de son champ fertile, l'âme et le corps. Ce sera comme lorsqu'un porte-étendard s'évanouit.
19 Mitengo yotsalira ya mʼnkhalango zake idzakhala yochepa kwambiri, yoti ndi mwana yemwe ndi kuyiwerenga.
Le reste des arbres de sa forêt sera peu nombreux, au point qu'un enfant pourrait écrire leur nombre.
20 Tsiku limenelo otsalira a ku Israeli, opulumuka a nyumba ya Yakobo, sadzadaliranso anthu amene anawakantha, koma adzadalira Yehova, Woyerayo wa Israeli.
En ce jour-là, le reste d'Israël et les réchappés de la maison de Jacob ne s'appuieront plus sur celui qui les frappait, mais ils s'appuieront sur Yahvé, le Saint d'Israël, dans la vérité.
21 Otsalira adzabwerera, otsalira a Yakobo adzabwerera kwa Mulungu Wamphamvu.
Un reste reviendra, le reste de Jacob, vers le Dieu puissant.
22 Iwe Israeli, ngakhale anthu ako achuluke ngati mchenga wa ku nyanja, otsala okha ndiwo adzabwerere. Chiwonongeko chalamulidwa, chidzaonetsa chilungamo chosefukira.
Car si ton peuple, Israël, est comme le sable de la mer, un reste seulement reviendra. Une destruction est prévue, débordante de justice.
23 Ambuye Yehova Wamphamvuzonse adzawononga ndithu dziko lonse monga momwe analamulira.
Car l'Éternel, le Yahvé des armées, fera une destruction complète, et déterminée, sur toute la terre.
24 Nʼchifukwa chake, Ambuye Yehova Wamphamvuzonse akunena kuti, “Inu anthu anga okhala mu Ziyoni, musawaope Asiriya, amene amakukanthani ndi ndodo nakumenyani ndi zibonga monga mmene Igupto anachitira.
C'est pourquoi l'Éternel, le Yahvé des armées, dit: « Mon peuple qui habite Sion, ne craignez pas l'Assyrien, même s'il vous frappe de sa verge et qu'il lève son bâton contre vous, comme l'Égypte.
25 Patsala pangʼonongʼono kuti mkwiyo wanga uchoke pa inu ndipo ndidzaonetsa ukali wanga pa iwo mpaka kuwawononga.”
Car encore un tout petit moment, et l'indignation contre vous s'accomplira, et ma colère se portera sur sa destruction. »
26 Yehova Wamphamvuzonse adzawakwapula ndi chikwapu, monga momwe anakwapulira Amidiyani ku thanthwe la Orebu; ndipo adzatukula ndodo yake pa madzi ndikuwalanga monga analangira Igupto pa nyanja.
Yahvé des armées suscitera contre lui un fléau, comme lors du massacre de Madian au rocher d'Oreb. Sa verge sera au-dessus de la mer, et il la lèvera comme il l'a fait contre l'Égypte.
27 Tsiku limenelo katundu wawo adzachotsedwa pa mapewa anu, goli lawo lidzachoka mʼkhosi mwanu; golilo lidzathyoka chifukwa cha kunenepa kwambiri.
En ce jour-là, son fardeau disparaîtra de ton épaule, et son joug de ton cou, et le joug sera détruit à cause de l'huile d'onction.
28 Adani alowa mu Ayati apyola ku Migironi; asunga katundu wawo ku Mikimasi.
Il est arrivé à Aiath. Il passe par Migron. A Michmash, il range ses bagages.
29 Adutsa pa mpata uja, ndipo akuti, “Tikagona ku Geba” Rama akunjenjemera; Gibeya, mzinda wa Saulo ukuthawa.
Ils ont franchi le col. Ils se logent à Guéba. Rama tremble. Gibéa de Saül s'est enfuie.
30 Lilani mokweza, inu anthu a ku Galimu! Tchera khutu, iwe Laisa! Iwe Anatoti wosauka!
Crie de ta voix, fille de Gallim! Écoute, Laisha! Pauvre Anathoth!
31 Anthu a ku Madimena akuthawa; anthu a ku Gebimu bisalani.
Madmena est une fugitive. Les habitants de Guébim fuient pour se mettre en sûreté.
32 Lero lomwe lino adaniwo adzayima ku Nobu; adzagwedeza mikono yawo, kuopseza anthu a ku Ziyoni, pa phiri la Yerusalemu.
Aujourd'hui même, il s'arrête à Nob. Il serre la main à la montagne de la fille de Sion, à la colline de Jérusalem.
33 Taonani, Ambuye Yehova Wamphamvuzonse, adzadula mwamphamvu nthambi za mitengo, mitengo yodzikweza idzadulidwa, mitengo yayitali idzagwetsedwa.
Voici que le Seigneur, l'Éternel des armées, fauche les rameaux avec terreur. Les grands seront abattus, et les grands seront abaissés.
34 Yehova adzadula ndi nkhwangwa mitengo ya mʼnkhalango yowirira; Lebanoni adzagwa pamaso pa Wamphamvu.
Ilabattra avec le fer les fourrés de la forêt, et le Liban tombera sous les coups du Puissant.