< Yesaya 10 >
1 Tsoka kwa anthu amene amapanga malamulo opanda chilungamo, kwa iwo amene amalemba zongovutitsa anzawo,
Wo to them that maken wickid lawis, and thei writynge han wryte vnriytfulnesse, for to oppresse pore men in doom,
2 kuwalanda anthu osauka ufulu wawo ndi kumana chilungamo osautsidwa pakati pa anthu anga, amalanda zinthu za akazi amasiye ndi kubera ana amasiye.
and to do violence to the cause of meke men of my puple; that widewis schulen be the prey of them, and that thei schulden rauysche fadirles children.
3 Kodi mudzatani pa tsiku la chilango, pofika chiwonongeko chochokera kutali? Kodi mudzathawira kwa yani kuti akuthandizeni? Nanga chuma chanu mudzachisiya kuti?
What schulen ye do in the dai of visitacioun, and of wretchidnesse comynge fro fer? To whos help schulen ye fle? and where schulen ye leeue youre glorie,
4 Kudzatsala nʼkungozolika mwamanyazi pakati pa anthu ogwidwa kapena kufa pamodzi ndi ophedwa. Komabe pa zonsezi mkwiyo wake sunawachokere, mkono wake uli chitambasulire.
that ye be not bowid doun vndur boond, and falle not doun with slayn men? On alle these thingis his strong veniaunce is not turned awei, but yit his hond is stretchid forth.
5 “Tsoka kwa mfumu ya ku Asiriya, chikwapu cha mkwiyo wanga, iye ndiye ndodo ya mkwiyo wanga!
Wo to Assur, he is the yerde and staf of my strong veniaunce; myn indignacioun is in the hond of them.
6 Ndidzamutuma kukalimbana ndi mtundu wosapembedza Mulungu, ndidzamutumiza kukalimbana ndi anthu amene amandikwiyitsa Ine, kukafunkha ndi kulanda chuma, ndi kuwapondereza pansi ngati matope a mʼmisewu.
Y schal send hym to a fals folk, and Y schal comaunde to hym ayens the puple of my strong veniaunce; that he take awei the spuylis, and departe prey, and that he sette that puple in to defouling, as the fen of stretis.
7 Koma izi si zimene akufuna kukachita, izi si zimene zili mʼmaganizo mwake; cholinga chake ndi kukawononga, kukapulula mitundu yambiri ya anthu.
Forsothe he schal not deme so, and his herte schal not gesse so, but his herte schal be for to al to-breke, and to the sleynge of many folkis.
8 Iye akuti, ‘Kodi atsogoleri anga ankhondo si mafumu okhaokha?’
For he schal seie, Whether my princes ben not kyngis to gidere?
9 ‘Kodi Kalino sanagonjetsedwe monga Karikemesi? Kodi Hamati sali ngati Aripadi, nanga Samariya sali ngati Damasiko?
Whether not as Carcamys, so Calanno; and as Arphat, so Emath? whether not as Damask, so Samarie?
10 Dzanja langa linakantha maufumu a anthu opembedza mafano, mafumu amene mafano awo ndi aakulu kupambana Yerusalemu ndi Samariya;
As myn hond foond the rewmes of idol, so and the symylacris of hem of Jerusalem and of Samarie.
11 nanga Ine nʼkulephera kodi kuwononga Yerusalemu pamodzi ndi mafano ake monga ndinakanthira Samariya pamodzi ndi mafano ake?’”
Whether not as Y dide to Samarie, and to the idols therof, so Y schal do to Jerusalem, and to the simylacris therof?
12 Ambuye akadzamaliza ntchito yonse yolanga phiri la Ziyoni ndi Yerusalemu adzalanganso mfumu ya ku Asiriya chifukwa cha kudzitama ndi kunyada kwake.
And it schal be, whanne the Lord hath fillid alle hise werkis in the hil of Syon and in Jerusalem, Y schal visite on the fruit of the greet doynge herte of the kyng of Assur, and on the glorie of the hiynesse of hise iyen.
13 Pakuti mfumuyo ikuti, “‘Ndachita zimenezi ndi dzanja langa, ndiponso ndi nzeru zanga, chifukwa ndine wozindikira zinthu. Ndinachotsa malire a mitundu ya anthu, ndinafunkha chuma chawo; ndinagonjetsa mafumu awo monga munthu wamphamvu.
For he seide, Y haue do in the strengthe of myn honde, and Y haue understonde in my wisdom; and Y haue take awei the endis of peplis, and Y haue robbid the princes of them, and Y as a myyti man haue drawun doun them that saten an hiy.
14 Dzanja langa lagwira chuma cha mitundu ya anthu ngati momwe munthu amagwirira chisa cha mbalame, ngati momwe anthu amatolera mazira osiyidwa, motero inenso ndinasonkhanitsa mayiko onse; palibe mbalame imene inakupiza mapiko ake, kapena kuyasama kukamwa kuti ilire.’”
And myn hond foond the strengthe of puplis as a nest, and as eirun ben gaderid togidere that ben forsakun, so Y gaderid togidere al erthe; and noon was that mouyde a fethere, and openyde the mouth, and grutchide.
15 Kodi nkhwangwa ingathe kudzikuza kupambana woyigwiritsa ntchito, kapena macheka angathe kudzikuza kupambana wowagwiritsa ntchito? Ndiye kukhala ngati kuti chikwapu chikuzunguza munthu amene wachinyamula, kapena ngati kuti ndodo ikuopseza amene wayinyamula!
Whether an ax schal haue glorie ayens hym that kittith with it? ether a sawe schal be enhaunsid ayens hym of whom it is drawun? as if a yerde is reisid ayens hym that reisith it, and a staf is enhaunsid, which sotheli is a tre.
16 Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova Wamphamvuzonse adzatumiza matenda owondetsa kwa ankhondo amphamvu; kunyada kwa mfumuyo kudzapsa ndi moto wosazima.
For this thing the lordli gouernour, Lord of oostis, schal sende thinnesse in the fatte men of hym, and his glorie kyndlid vndur schal brenne as `the brenning of fier.
17 Mulungu, Kuwala kwa Israeli, adzakhala ngati moto, Woyera uja wa Israeli adzakhala ngati malawi a moto. Motowo udzawatentha ndi kuwapsereza ngati minga ndi mkandankhuku pa tsiku limodzi.
And the liyt of Israel schal be in fier, and the hooli of it in flawme; and the thorn of him and brere schal be kyndlid and deuourid in o dai.
18 Ankhondo ake adzawonongedwa ngati nkhalango yayikulu ndi ngati nthaka yachonde.
And the glorie of his forest and of his Carmele schal be wastid, fro the soule `til to fleisch; and he schal be fleynge awei for drede.
19 Mitengo yotsalira ya mʼnkhalango zake idzakhala yochepa kwambiri, yoti ndi mwana yemwe ndi kuyiwerenga.
And the relifs of the tree of his forest schulen be noumbrid for fewnesse, and a child schal write hem.
20 Tsiku limenelo otsalira a ku Israeli, opulumuka a nyumba ya Yakobo, sadzadaliranso anthu amene anawakantha, koma adzadalira Yehova, Woyerayo wa Israeli.
And it schal be in that dai, the remenaunt of Israel, and thei that fledden of the house of Jacob, schal not adde for to triste on hym that smytith hem; but it schal triste on the hooli Lord of Israel, in treuthe.
21 Otsalira adzabwerera, otsalira a Yakobo adzabwerera kwa Mulungu Wamphamvu.
The relifs, Y seie, the relifs of Jacob, schulen be conuertid to the stronge Lord.
22 Iwe Israeli, ngakhale anthu ako achuluke ngati mchenga wa ku nyanja, otsala okha ndiwo adzabwerere. Chiwonongeko chalamulidwa, chidzaonetsa chilungamo chosefukira.
Forwhi, Israel, if thi puple is as the grauel of the see, the relifs schulen be turned therof; an endyng maad schort schal make riytfulnesse to be plenteuouse.
23 Ambuye Yehova Wamphamvuzonse adzawononga ndithu dziko lonse monga momwe analamulira.
For whi the Lord God of oostis schal make an endyng and a breggyng in the myddis of al erthe.
24 Nʼchifukwa chake, Ambuye Yehova Wamphamvuzonse akunena kuti, “Inu anthu anga okhala mu Ziyoni, musawaope Asiriya, amene amakukanthani ndi ndodo nakumenyani ndi zibonga monga mmene Igupto anachitira.
For this thing the Lord God of oostis seith these thingis, My puple, the dwellere of Sion, nyle thou drede of Assur, for he schal smite thee in a yerde, and he schal reise his staf on thee in the weie of Egipt.
25 Patsala pangʼonongʼono kuti mkwiyo wanga uchoke pa inu ndipo ndidzaonetsa ukali wanga pa iwo mpaka kuwawononga.”
Forwhi yit a litil, and a litil, and myn indignacioun and my strong veniaunce schal be endid on the greet trespas of hem.
26 Yehova Wamphamvuzonse adzawakwapula ndi chikwapu, monga momwe anakwapulira Amidiyani ku thanthwe la Orebu; ndipo adzatukula ndodo yake pa madzi ndikuwalanga monga analangira Igupto pa nyanja.
And the Lord of oostis schal reise a scourge on hym bi the veniaunce of Madian in the stoon of Oreb, and bi his yerde on the see; and he schal reise that yerde in the wei of Egipt.
27 Tsiku limenelo katundu wawo adzachotsedwa pa mapewa anu, goli lawo lidzachoka mʼkhosi mwanu; golilo lidzathyoka chifukwa cha kunenepa kwambiri.
And it schal be in that dai, his birthun schal be takun awei fro thi schuldre, and his yok fro thi necke; and the yok schal wexe rotun fro the face of oile.
28 Adani alowa mu Ayati apyola ku Migironi; asunga katundu wawo ku Mikimasi.
He schal come in to Aioth, he schal passe in to Magron, at Magynas he schal bitake his vessels to kepyng.
29 Adutsa pa mpata uja, ndipo akuti, “Tikagona ku Geba” Rama akunjenjemera; Gibeya, mzinda wa Saulo ukuthawa.
Thei passiden swiftli, Gabaa is oure seete, Rama was astonyed, Gabaa of Saul fled.
30 Lilani mokweza, inu anthu a ku Galimu! Tchera khutu, iwe Laisa! Iwe Anatoti wosauka!
Thou douytir of Gallym, weile with thi vois; thou Laisa, perseyue, thou pore Anatot.
31 Anthu a ku Madimena akuthawa; anthu a ku Gebimu bisalani.
Medemena passide; the dwelleris of Gabyn fledden; be ye coumfortid.
32 Lero lomwe lino adaniwo adzayima ku Nobu; adzagwedeza mikono yawo, kuopseza anthu a ku Ziyoni, pa phiri la Yerusalemu.
Yit it is dai, that me stonde in Nobe; he schal dryue his hond on the hil of the douyter of Syon, on the litil hil of Jerusalem.
33 Taonani, Ambuye Yehova Wamphamvuzonse, adzadula mwamphamvu nthambi za mitengo, mitengo yodzikweza idzadulidwa, mitengo yayitali idzagwetsedwa.
Lo! the lordli gouernour, the Lord of oostis, schal breke a potel in drede, and hiy men of stature schulen be kit doun.
34 Yehova adzadula ndi nkhwangwa mitengo ya mʼnkhalango yowirira; Lebanoni adzagwa pamaso pa Wamphamvu.
And proude men schulen be maade low, and the thicke thingis of the forest schulen be distried bi irun; and the Liban with hiy thingis schal falle doun.