< Yesaya 1 >

1 Masomphenya wonena za Yuda ndi Yerusalemu, amene Yesaya mwana wa Amozi, anaona pa nthawi ya ulamuliro wa Uziya, Yotamu, Ahazi ndi Hezekiya, mafumu a Yuda.
Saa anisoadehu a ɛfa Yuda ne Yerusalem ho no baa Amos babarima Yesaia so wɔ Yuda ahemfo Usia, Yotam, Ahas ne Hesekia mmere so.
2 Tamverani, miyamba inu! Tchera khutu, iwe dziko lapansi! Pakuti Yehova wanena kuti, “Ndinabala ana ndi kuwalera, koma anawo andiwukira Ine.
Ɔsoro, muntie! Asase, yɛ aso! Na Awurade akasa: “Matetew mma ama wɔanyinyin, nanso wɔatew me so atua.
3 Ngʼombe imadziwa mwini wake, bulu amadziwa kumene kuli gome la mbuye wake, koma Israeli sadziwa, anthu anga samvetsa konse.”
Nantwi nim ne wura, afurum nso nim ne wura mmoa adididaka, nanso Israel nnim, me nkurɔfo nte ase.”
4 Haa, mtundu wochimwa, anthu olemedwa ndi machimo, obadwa kwa anthu ochita zoyipa, ana odzipereka ku zoyipa! Iwo asiya Yehova; anyoza Woyerayo wa Israeli ndipo afulatira Iyeyo.
Nnome nka, amumɔyɛ man, ɔman a wɔn afɔdi so, nnebɔneyɛfo kuw, mma a porɔwee ahyɛ wɔn ma! Wɔatwe wɔn ho afi Awurade ho; wɔapo Israel Kronkronni no, wɔadan wɔn akyi akyerɛ no.
5 Chifukwa chiyani mukufuna kuti muzingolangidwabe? Chifukwa chiyani mukupitirira kukhala mʼmoyo wowukira? Mutu wanu wonse uli ndi mabala, mtima wanu wonse wafowokeratu.
Adɛn nti na mopɛ sɛ wɔkɔ so boro mo? Adɛn nti na moda so tew atua? Wɔapira mo ti, na mo koma nso di yaw.
6 Kuchokera ku phazi mpaka ku mutu palibe pabwino, paliponse pali mikwingwirima ndi zilonda, mabala ali magazi chuchuchu, mabala ake ngosatsuka, ngosamanga ndiponso ngosapaka mafuta ofewetsa.
Efi mo nan ase kosi mo ti so, ahomeka biara nni mu, apirakuru ne ahonhon nko ara akuru a anim deda hɔ na wɔnhohoro so anaa wɔnkyekyeree anaa wɔmfaa ngo nsrasraa so ɛ.
7 Dziko lanu lasanduka bwinja, mizinda yanu yatenthedwa ndi moto; minda yanu ikukololedwa ndi alendo inu muli pomwepo, dziko lanu lasanduka bwinja monga ngati lagonjetsedwa ndi alendo.
Mo man ada mpan, wɔde ogya ahyehyew mo nkuropɔn; ananafo regye mo mfuw a mo ani tua, na asɛe sɛnea ɛyɛɛ bere a ahɔho tuu mo gui no.
8 Mwana wamkazi wa Ziyoni watsala yekha ngati nsanja mʼmunda wampesa, ngati chisimba mʼmunda wa minkhaka, ngati mzinda wozingidwa ndi nkhondo.
Wɔagyaw Ɔbabea Sion te sɛ bobeturo mu sese te sɛ akuraa a esi ɛfere afuw mu, te sɛ kuropɔn a atamfo atwa ho ahyia.
9 Yehova Wamphamvuzonse akanapanda kutisiyira opulumuka, tikanawonongeka ngati Sodomu, tikanakhala ngati anthu a ku Gomora.
Sɛ Asafo Awurade annyaw yɛn asefo a, anka yɛayɛ sɛ Sodom, na yɛadan ayɛ sɛ Gomora.
10 Imvani mawu a Yehova, inu olamulira Sodomu; mverani lamulo la Mulungu wathu, inu anthu a ku Gomora!
Muntie Awurade asɛm, mo Sodom sodifo; muntie yɛn Nyankopɔn mmara, mo Gomorafo!
11 Yehova akuti, “Kodi ndili nazo chiyani nsembe zanu zochuluka?” “Zandikola nsembe zanu zopsereza za nkhosa zazimuna ndiponso mafuta a nyama zonenepa; sindikusangalatsidwanso ndi magazi angʼombe zamphongo ndi a ana ankhosa ndi ambuzi zazimuna.
“Mo afɔrebɔ ahorow bebree no, dɛn na ɛyɛ ma me?” Sɛnea Awurade se ni. “Mewɔ ɔhyew afɔrebɔde ma ɛboro so, nea ɛyɛ adwennini ne mmoa a wɔadɔ srade; mʼani nnye anantwinini, nguantenmma ne mpapo mogya ho.
12 Ndani anakulamulirani kuti mubwere nazo pamaso panga? Ndani anakuwuzani kuti muzipondaponda mʼmabwalo a nyumba yanga?
Sɛ moba mʼanim a hena na obisa eyi fi mo hɔ, sɛ mutiatia me fi yi?
13 Siyani kubweretsa nsembe zachabechabezo! Nsembe zanu zofukiza zimandinyansa Ine. Sindingapirire misonkhano yanu yoyipa, kapenanso zikondwerero za Mwezi Watsopano ndi Masabata.
Munnyae afɔrebɔde a ɛmfra a mode ba no! Mo aduhuam yɛ me tan. Ɔsram foforo, homenna ne nhyiamu ahorow, mo nhyiamu hunu no afono me.
14 Zikondwerero zanu za Mwezi Watsopano ndi masiku anu opatulika ndimadana nazo. Zasanduka katundu wondilemera; ndatopa kuzinyamula.
Mo ɔsram foforo afahyɛ ne mo aponto a moahyehyɛ, me kra kyi. Ayɛ adesoa ama me; masoa abrɛ.
15 Mukamatambasula manja anu popemphera, Ine sindidzakuyangʼanani; ngakhale muchulukitse mapemphero anu, sindidzakumverani. Manja anu ndi odzaza ndi magazi;
Sɛ momema mo nsa so bɔ mpae a, meyi mʼani ato nkyɛn. Sɛ mobɔ mpae bebree mpo a merentie. “Mogya bebree agu mo nsa ho fi.
16 sambani, dziyeretseni. Chotsani pamaso panu ntchito zanu zoyipa! Lekani kuchita zoyipa,
“Munnwira mo ho na mo ho ntew. Munnyi mo nnebɔne mfi mʼani so! Munnyae bɔneyɛ,
17 phunzirani kuchita zabwino! Funafunani chilungamo, thandizani oponderezedwa. Tetezani ana amasiye, muwayimirire akazi amasiye pa milandu yawo.”
Monyɛ papa! Monhwehwɛ atɛntrenee. Monhyɛ wɔn a wɔhyɛ wɔn so nkuran Munni mma ayisaa, monka akunafo nsɛm mma wɔn.
18 Yehova akuti, “Tiyeni tsono tikambe mlandu wanu. Ngakhale machimo anu ali ofiira, adzayera ngati thonje. Ngakhale ali ofiira ngati kapezi, adzayera ngati ubweya wankhosa.
“Afei mommra na yennwen mmɔ mu,” sɛnea Awurade se ni. “Sɛ mo bɔne te sɛ ɔkɔben a, ɛbɛyɛ fitaa sɛ sukyerɛmma; mpo sɛ ɛyɛ kɔkɔɔ te sɛ mogya a ɛbɛyɛ fitaa sɛ asaawa mfuturu.
19 Ngati muli okonzeka kundimvera mudzadya zinthu zabwino za mʼdziko;
Sɛ mopene so na moyɛ osetie a, mubedi asase no so nnepa.
20 koma mukakana ndi kuwukira mudzaphedwa ndi lupanga.” Pakuti Yehova wayankhula.
Na sɛ moampene na motew atua a, afoa bedi mo nam.” Awurade na wakasa.
21 Taonani momwe mzinda wokhulupirika wasandukira wadama! Mzinda umene kale unali wodzaza ndi chiweruzo cholungama; mu mzindamo munali chilungamo, koma tsopano muli anthu opha anzawo!
Hwɛ sɛnea kuropɔn nokwafo no adan oguamanfo. Bere bi, na atɛntrenee ahyɛ no ma na anka trenee te ne mu, nanso mprempren, awudifo ahyɛ mu ma!
22 Siliva wako wasanduka wachabechabe, vinyo wako wabwino wasungunulidwa ndi madzi.
Wo dwetɛ adan ade a so nni mfaso, wɔde nsu afra wo nsa papa mu.
23 Atsogoleri ako ndi owukira, anthu ogwirizana ndi mbala; onse amakonda ziphuphu ndipo amathamangira mphatso. Iwo sateteza ana amasiye; ndipo samvera madandawulo a akazi amasiye.
Wo sodifo yɛ atuatewfo, akorɔmfo yɔnkonom; wɔn nyinaa pɛ adanmude, na wɔpere akyɛde ho. Wonni mma ayisaa; na akunafo nsɛm nkɔ wɔn anim.
24 Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova Wamphamvu, Wamphamvuyo wa Israeli, akunena kuti, “Haa, odana nane ndidzawatha, ndipo ndidzawabwezera ndekha adani anga.
Enti, Awurade, Asafo Awurade, nea ɔyɛ Ɔkɛse ma Israel no ka se, “Aa, menya ahomegye afi mʼatamfo hɔ na matɔ wɔn so were.
25 Ndidzatambasula dzanja langa kuti ndilimbane nawe; ndidzasungunula machimo ako nʼkuwachotsa, monga mmene amachotsera dzimbiri ndi mankhwala.
Mɛma me nsa so, atia mo; mɛhohoro mo ho fi korakora na mayi mo ho nkekae nyinaa.
26 Ndidzabwezeretsa oweruza ako ngati masiku amakedzana, aphungu ako ndidzawabwezeretsa ngati poyamba paja. Kenaka iweyo udzatchedwa mzinda wolungama, mzinda wokhulupirika.”
Mɛma mo atemmufo bio sɛ kan no, ne mo afotufo sɛnea na ɛte, mfiase no. Eyi akyi no, wɔbɛfrɛ wo Kuropɔn Trenee, Kuropɔn Nokwafo.”
27 Ziyoni adzawomboledwa mwa chiweruzo cholungama, anthu ake olapadi adzapulumutsidwa mwachilungamo.
Wɔde atɛntrenee begye Sion bio, na wɔn a wonu wɔn ho no, wɔde trenee begye wɔn.
28 Koma owukira ndi ochimwa adzawawonongera pamodzi, ndipo amene asiya Yehova adzatheratu.
Nanso atuatewfo ne nnebɔneyɛfo de, wɔbɛdwerɛw wɔn abɔ mu, na wɔn a wɔpa Awurade akyi bɛyera.
29 “Mudzachita nayo manyazi mitengo ya thundu imene inkakusangalatsani; mudzagwetsa nkhope chifukwa cha minda imene munayipatula.
“Mo ani bewu, esiane odum anyame a munyaa wɔn mu anigye no; wobegu mo anim ase, esiane nturo a mosom abosom wɔ mu no nti.
30 Mudzakhala ngati mtengo wa thundu umene masamba ake akufota, mudzakhala ngati munda wopanda madzi.
Mobɛyɛ sɛ odum a ne nhaban apo, ne turo a ennya nsu.
31 Munthu wamphamvu adzasanduka ngati udzu wowuma, ndipo ntchito zake zidzakhala ngati mbaliwali; motero zonse zidzayakira limodzi, popanda woti azimitse motowo.”
Ɔhoɔdenfo bɛyɛ sɛ ade a ɛhyew ntɛm nʼadwuma bɛyɛ sɛ ogya a aturuw; abien no bɛhyew abɔ mu, a obiara rentumi nnum.”

< Yesaya 1 >