< Hoseya 1 >

1 Awa ndi mawu amene Yehova anayankhula kwa Hoseya mwana wa Beeri pa nthawi ya ulamuliro wa Uziya, Yotamu, Ahazi ndi Hezekiya, mafumu a ku Yuda ndiponso pa nthawi ya ulamuliro wa Yeroboamu mwana wa Yowasi mfumu ya ku Israeli.
Słowo PANA, które doszło do Ozeasza, syna Beeriego, za dni Uzjasza, Jotama, Achaza, Ezechiasza, królów Judy, i za dni Jeroboama, syna Joasza, króla Izraela.
2 Yehova atayamba kuyankhula kudzera mwa Hoseya, Yehova anati kwa Hoseyayo, “Pita kakwatire mkazi wachiwerewere ndipo ubereke naye ana mʼchiwerewere chake pakuti anthu a mʼdziko muno achimwa pochita chigololo choyipitsitsa, posiya Yehova.”
Początek słowa PANA przez Ozeasza. PAN powiedział do Ozeasza: Idź, weź sobie nierządnicę za żonę i dzieci nierządu. Ziemia bowiem uprawiała wstydliwy nierząd, odwróciła się od PANA.
3 Motero Hoseya anakwatira Gomeri mwana wamkazi wa Dibulaimu, ndipo mkaziyo anakhala woyembekezera nabala mwana wamwamuna.
Poszedł więc i wziął sobie za żonę Gomerę, córkę Diblaima, a ona poczęła i urodziła mu syna.
4 Tsono Yehova anati kwa Hoseya, “Umutche dzina loti Yezireeli, pakuti ndili pafupi kulanga banja la Yehu chifukwa cha anthu amene anawapha ku Yezireeli ndipo ndidzathetsa ufumu wa Israeli.
PAN powiedział do niego: Nadaj mu imię Jizreel, bo już niedługo pomszczę na domu Jehu krew Jizreel i sprawię, [że] ustanie królestwo domu Izraela.
5 Tsiku limenelo ndidzathyola uta wa Israeli mʼchigwa cha Yezireeli.”
W tym dniu złamię łuk Izraela w dolinie Jizreel.
6 Gomeri anakhala woyembekezeranso ndipo anabereka mwana wamkazi. Ndipo Yehova anati kwa Hoseya, “Umutche dzina loti ‘Sakondedwa’ pakuti sindidzaonetsanso chikondi changa pa nyumba ya Israeli, kuti ndingawakhululukire konse.
I poczęła znowu, i urodziła córkę. [PAN] powiedział do niego: Nadaj jej imię Lo-Ruchama, bo już nie zlituję się nad domem Izraela, lecz na pewno go wytępię.
7 Komatu ndidzaonetsa chikondi pa nyumba ya Yuda; ndipo ndidzawapulumutsa, osati ndi uta, lupanga kapena nkhondo, kapena akavalo ndi okwerapo ake, koma ine Yehova Mulungu wawo ndidzawapulumutsa.”
Ale zlituję się nad domem Judy i wybawię go przez PANA, jego Boga, lecz nie wybawię łukiem ani mieczem, ani wojną, ani końmi, ani jeźdźcami.
8 Sakondedwa ataleka kuyamwa, Gomeri anabereka mwana wina wamwamuna.
Gdy odstawiła [od piersi] Lo-Ruchamę, znowu poczęła i urodziła syna.
9 Pamenepo Yehova anati, “Umutche dzina loti Sianthuanga,” pakuti inu si ndinu anthu anga ndipo Ine si ndine Mulungu wanu.
I [PAN] powiedział: Nadaj mu imię Lo-Ammi, bo wy nie jesteście moim ludem, ja też nie będę waszym [Bogiem].
10 “Komabe Aisraeli adzachuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja umene sangathe kuwuyeza kapena kuwuwerenga. Pamalo omwe ananena kuti, ‘Sindinu anthu anga,’ pomweponso adzawatchula kuti ‘Ana a Mulungu wamoyo.’
Jednak liczba synów Izraela będzie jak piasek morski, którego nie można zmierzyć ani zliczyć. I stanie się, że w miejscu, gdzie im mówiono: Nie jesteście moim ludem, będzie się do nich mówić: Wy jesteście synami Boga żywego.
11 Anthu a ku Yuda ndi anthu a ku Israeli adzasonkhananso pamodzi ndipo adzasankha mtsogoleri mmodzi ndi kutuluka mʼdzikomo, pakuti tsiku la Yezireeli lidzakhala lalikulu kwambiri.”
I będą zgromadzeni razem synowie Judy i synowie Izraela, ustanowią sobie jedną głowę i wyjdą z tej ziemi. Wielki bowiem [będzie] dzień Jizreel.

< Hoseya 1 >