< Hoseya 1 >

1 Awa ndi mawu amene Yehova anayankhula kwa Hoseya mwana wa Beeri pa nthawi ya ulamuliro wa Uziya, Yotamu, Ahazi ndi Hezekiya, mafumu a ku Yuda ndiponso pa nthawi ya ulamuliro wa Yeroboamu mwana wa Yowasi mfumu ya ku Israeli.
Niheo amy Hosea ana’ i Bierý ty tsara’ Iehovà faha’ i Ozià naho Iotame naho i Akhaze naho Khizkiia mpanjaka Iehodà, vaho Iarobàme ana’ Ioàse, mpanjaka’ Israele.
2 Yehova atayamba kuyankhula kudzera mwa Hoseya, Yehova anati kwa Hoseyayo, “Pita kakwatire mkazi wachiwerewere ndipo ubereke naye ana mʼchiwerewere chake pakuti anthu a mʼdziko muno achimwa pochita chigololo choyipitsitsa, posiya Yehova.”
Ie namotsotse nitsara amy Hosea t’Iehovà, le hoe t’Iehovà amy Hosea, Akia mañengà karapilo ho vali’o, ty anak’ ampela boak’ an-kàrapiloañe ao; fa toe mpanao hakarapiloan-kalalijake naho miamboho am’ Iehovà o taneo.
3 Motero Hoseya anakwatira Gomeri mwana wamkazi wa Dibulaimu, ndipo mkaziyo anakhala woyembekezera nabala mwana wamwamuna.
Aa le nimb’eo re nañenga i Gomere, ana’ i Diblaime, le niaren-dre vaho nisamaha’e anadahy.
4 Tsono Yehova anati kwa Hoseya, “Umutche dzina loti Yezireeli, pakuti ndili pafupi kulanga banja la Yehu chifukwa cha anthu amene anawapha ku Yezireeli ndipo ndidzathetsa ufumu wa Israeli.
Le hoe t’Iehovà ama’e, Toñono ty hoe Iezreèle ty añara’e; fa tsy ho ela te havaleko ami’ty anjomba’ Iehò ty lio’ Iezreèle, vaho hagàdoko ty fifehean’ anjomba’ Israele.
5 Tsiku limenelo ndidzathyola uta wa Israeli mʼchigwa cha Yezireeli.”
Ie amy andro zay, ho pozaheko ty fale’ Israele am-bavatane’ Iezreèle ao.
6 Gomeri anakhala woyembekezeranso ndipo anabereka mwana wamkazi. Ndipo Yehova anati kwa Hoseya, “Umutche dzina loti ‘Sakondedwa’ pakuti sindidzaonetsanso chikondi changa pa nyumba ya Israeli, kuti ndingawakhululukire konse.
Niareñe indraike re nahatoly anak’ ampela, le hoe re tama’e, Toñono ty hoe Lorokamà ty añara’e: fa tsy ho ferenaiñako ka ty anjomba’ Israele, toe tsy iheveako.
7 Komatu ndidzaonetsa chikondi pa nyumba ya Yuda; ndipo ndidzawapulumutsa, osati ndi uta, lupanga kapena nkhondo, kapena akavalo ndi okwerapo ake, koma ine Yehova Mulungu wawo ndidzawapulumutsa.”
Fe ho tretrezeko ty anjomba’ Iehodà le ho rombaheko añam’ Iehovà Andrianañahare’ iareoy, fa tsy ho rombaheko am-pale ndra fibara ndra hotakotake ndra soavala ndra mpiningi-tsoavala.
8 Sakondedwa ataleka kuyamwa, Gomeri anabereka mwana wina wamwamuna.
Aa ie notañe’e t’i Lorokamà, le niareñe indraike nisamak’ anadahy.
9 Pamenepo Yehova anati, “Umutche dzina loti Sianthuanga,” pakuti inu si ndinu anthu anga ndipo Ine si ndine Mulungu wanu.
Le hoe re, Toñono ty hoe Loamý fa tsy ondatiko nahareo vaho tsy ho Andrianañahare’ areo iraho.
10 “Komabe Aisraeli adzachuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja umene sangathe kuwuyeza kapena kuwuwerenga. Pamalo omwe ananena kuti, ‘Sindinu anthu anga,’ pomweponso adzawatchula kuti ‘Ana a Mulungu wamoyo.’
Fe mbe ho mira amo fasen-driakeo ty ia’ o ana’ Israeleo, ze tsy ho mete zeheñe ndra iaheñe; ie amy zay, amy tane nanoañe ama’ areo te Tsy ondatiko nahareoy, ty hafetse am’ iereo te Anan’ Añahare Veloñe.
11 Anthu a ku Yuda ndi anthu a ku Israeli adzasonkhananso pamodzi ndipo adzasankha mtsogoleri mmodzi ndi kutuluka mʼdzikomo, pakuti tsiku la Yezireeli lidzakhala lalikulu kwambiri.”
Le hifanontoñe o ana’ Iehodào naho o ana’ Israeleo, naho ho tendrè’ iareo ty mpiaolo raike ho a iareo, vaho hitombo an-tane eo: fa jabajaba ty andro’ Iezreèle.

< Hoseya 1 >