< Hoseya 1 >

1 Awa ndi mawu amene Yehova anayankhula kwa Hoseya mwana wa Beeri pa nthawi ya ulamuliro wa Uziya, Yotamu, Ahazi ndi Hezekiya, mafumu a ku Yuda ndiponso pa nthawi ya ulamuliro wa Yeroboamu mwana wa Yowasi mfumu ya ku Israeli.
BOEIPA ol tah Judah manghai rhoek Uzziah, Jotham, Ahaz, Hezekiah tue neh Israel manghai Joash capa Jeroboam tue vaengah Beeri capa Hosea taengla pawk.
2 Yehova atayamba kuyankhula kudzera mwa Hoseya, Yehova anati kwa Hoseyayo, “Pita kakwatire mkazi wachiwerewere ndipo ubereke naye ana mʼchiwerewere chake pakuti anthu a mʼdziko muno achimwa pochita chigololo choyipitsitsa, posiya Yehova.”
BOEIPA tah Hosea dong lamloh lamhma la cal. Te vaengah BOEIPA loh Hosea te, “Cet lamtah pumyoi nu neh pumyoihnah kah camoe rhoek te namah taengla lo laeh. Khohmuen he BOEIPA hnuk lamloh cukhalh rhoe cukhalh,” a ti nah.
3 Motero Hoseya anakwatira Gomeri mwana wamkazi wa Dibulaimu, ndipo mkaziyo anakhala woyembekezera nabala mwana wamwamuna.
Te dongah cet tih Diblaim canu Gomer te a loh. Te vaengah vawn tih anih hamla capa pakhat a sak pah.
4 Tsono Yehova anati kwa Hoseya, “Umutche dzina loti Yezireeli, pakuti ndili pafupi kulanga banja la Yehu chifukwa cha anthu amene anawapha ku Yezireeli ndipo ndidzathetsa ufumu wa Israeli.
Te vaengah BOEIPA loh anih te, “A ming te Jezreel sui. Jehu im kah Jezreel thii te ka cawh vetih Israel imkhui kah ram te ka paa sak pawn ni.
5 Tsiku limenelo ndidzathyola uta wa Israeli mʼchigwa cha Yezireeli.”
Te khohnin te a pha vaengah tah Israel kah lii te Jezreel kol ah ka khaem pah ni,” a ti.
6 Gomeri anakhala woyembekezeranso ndipo anabereka mwana wamkazi. Ndipo Yehova anati kwa Hoseya, “Umutche dzina loti ‘Sakondedwa’ pakuti sindidzaonetsanso chikondi changa pa nyumba ya Israeli, kuti ndingawakhululukire konse.
Te phoeiah koep vawn tih canu a sak hatah, “Israel imkhui te koep ka haidam voel pawt vetih amih te ka khuen rhoe ka khuen ham coeng dongah a ming te Loruhamah sui.
7 Komatu ndidzaonetsa chikondi pa nyumba ya Yuda; ndipo ndidzawapulumutsa, osati ndi uta, lupanga kapena nkhondo, kapena akavalo ndi okwerapo ake, koma ine Yehova Mulungu wawo ndidzawapulumutsa.”
Tedae Judah imkhui tah ka haidam vetih amih te amamih kah Pathen BOEIPA rhangneh ka khang ni. Te vaengah amih te lii neh, tumca neh, caemtloek neh, marhang neh, marhang caem neh ka khang mahpawh,” a ti nah.
8 Sakondedwa ataleka kuyamwa, Gomeri anabereka mwana wina wamwamuna.
Loruhamah te suk a kan phoeiah vawn tih capa a sak.
9 Pamenepo Yehova anati, “Umutche dzina loti Sianthuanga,” pakuti inu si ndinu anthu anga ndipo Ine si ndine Mulungu wanu.
Te vaengah, “Nangmih te ka pilnam voel pawt tih kai khaw nangmih hut la ka om voel pawt dongah a ming te Loami sui,” a ti nah.
10 “Komabe Aisraeli adzachuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja umene sangathe kuwuyeza kapena kuwuwerenga. Pamalo omwe ananena kuti, ‘Sindinu anthu anga,’ pomweponso adzawatchula kuti ‘Ana a Mulungu wamoyo.’
Tedae Israel ca hlangmi tah tuitunli kah laivin bangla om ni. Te te loeng lek pawt tih tae lek pawh. Amih te, 'Nangmih te ka pilnam moenih,’ a ti nah hmuen ah a om sak vetih amih te aka hing Pathen ca rhoek a ti ni.
11 Anthu a ku Yuda ndi anthu a ku Israeli adzasonkhananso pamodzi ndipo adzasankha mtsogoleri mmodzi ndi kutuluka mʼdzikomo, pakuti tsiku la Yezireeli lidzakhala lalikulu kwambiri.”
Te vaengah Judah ca rhoek neh Israel ca tun tingtun uh ni. Amamih ham boeilu pakhat a khueh uh tih Jezreel khohnin puei ham khohmuen lamloh cet uh ni,” a ti nah.

< Hoseya 1 >