< Hoseya 9 >

1 Iwe Israeli, usakondwere; monga imachitira mitundu ina. Pakuti wakhala wosakhulupirika kwa Mulungu wako; umakonda malipiro a chiwerewere pa malo aliwonse opunthira tirigu.
Ну те букура, Исраеле, ну те весели ка попоареле, пентру кэ ай курвит, пэрэсинд пе Домнул, пентру кэ ай юбит о платэ некуратэ ын тоате арииле ку грыу!
2 Malo opunthira tirigu ndi malo opsinyira mphesa sadzadyetsa anthu; adzasowa vinyo watsopano.
Ария ши тяскул ну-й вор хрэни ши мустул ле ва липси.
3 Sadzakhalanso mʼdziko la Yehova. Efereimu adzabwerera ku Igupto ndipo mudzadya chakudya chodetsedwa ku Asiriya.
Ну вор рэмыне ын цара Домнулуй, чи Ефраим се ва ынтоарче ын Еӂипт ши вор мынка ын Асирия мынкэрурь некурате.
4 Iwo sadzaperekanso chopereka cha chakumwa kwa Yehova, kapena nsembe zawo kuti akondweretse Yehovayo. Nsembe zotere zidzakhala kwa iwo ngati chakudya cha anamfedwa; onse akudya chakudya chimenechi adzakhala odetsedwa. Chakudya ichi chidzakhala chodya okha, sichidzalowa mʼnyumba ya Yehova.
Ну вор адуче Домнулуй вин ка жертфэ де бэутурэ, кэч ну-Й ва фи плэкутэ. Пыня лор ле ва фи ка о пыне де жале; тоць чей че вор мынка дин еа се вор фаче некураць, кэч пыня лор ва фи нумай пентру ей, ну ва интра ын Каса Домнулуй!
5 Kodi mudzachita chiyani pa tsiku la maphwando anu oyikika; pa masiku a zikondwerero za Yehova?
Че вець фаче ын зилеле де празник, ла сэрбэториле Домнулуй?
6 Ngakhale iwo atathawa chiwonongeko, Igupto adzawasonkhanitsa, ndipo Mefisi adzawayika mʼmanda. Khwisa adzamera pa ziwiya zawo zasiliva, ndipo minga idzamera mʼmatenti awo.
Кэч ятэ кэ ей плякэ дин причина пустиирий; Еӂиптул ый ва адуна, Мофул ле ва да морминте; че ау май скумп, арӂинтул лор, ва фи прада мэрэчинилор ши вор креште спиний ын кортуриле лор.
7 Masiku achilango akubwera, masiku obwezera ali pafupi. Israeli adziwe zimenezi. Chifukwa machimo anu ndi ochuluka kwambiri ndipo udani wanu pa Mulungu ndi waukulu kwambiri. Mneneri amamuyesa chitsiru, munthu wanzeru za kwa Mulungu ngati wamisala.
Вин зилеле педепсей, вин зилеле рэсплэтирий: Исраел ва ведя сингур дакэ пророкул есте небун сау дакэ омул инсуфлат аюрязэ. Ши ачаста дин причина мэримий нелеӂюирилор ши рэзврэтирилор тале.
8 Mneneri pamodzi ndi Mulungu wanga ndiwo alonda a Efereimu, koma mneneri amutchera misampha mʼnjira zake zonse, ndipo udani ukumudikira mʼnyumba ya Mulungu wake.
Ефраим стэ ла пындэ ымпотрива Думнезеулуй меу, пророкулуй и се ынтинд лацурь де пэсэрь пе тоате кэиле луй, ыл врэжмэшеск ын Каса Думнезеулуй сэу.
9 Iwo azama mu zachinyengo monga masiku a Gibeya. Mulungu adzakumbukira zolakwa zawo ndipo adzawalanga chifukwa cha machimo awo.
С-ау афундат ын стрикэчуне, ка ын зилеле Гибеей; Домнул Ышь ва адуче аминте де нелеӂюиря лор, ле ва педепси пэкателе.
10 “Pamene ndinamupeza Israeli zinali ngati kupeza mphesa mʼchipululu. Nditaona makolo anu, zinali ngati ndikuona nkhuyu zoyambirira kupsa. Koma atafika ku Baala Peori, anadzipereka ku fano lija lochititsa manyazi ndipo anakhala onyansa ngati chinthu chimene anachikondacho.
„Ам гэсит пе Исраел ка пе ниште стругурь ын пустиу, ам вэзут пе пэринций воштри ка пе челе динтый роаде але унуй смокин, ын примэварэ, дар ей с-ау дус ла Баал-Пеор, с-ау пус ын служба идолулуй скырбос ши ау ажунс урычошь ка ши ачела пе каре ыл юбяу.
11 Ulemerero wa Efereimu udzawuluka ngati mbalame. Sipadzakhalanso kubereka ana, kuyembekezera kapena kutenga pathupi.
Слава луй Ефраим ва збура ка о пасэре: ну май есте нич о наштере, нич о ынсэрчинаре ши нич о зэмислире!
12 Ngakhale atalera ana ndidzachititsa kuti mwana aliyense amwalire. Tsoka kwa anthuwo pamene Ine ndidzawafulatira!
Кяр дакэ ышь вор креште копиий, ый вой липси де ей ынаинте ка сэ ажунгэ оамень марь, ши вай де ей кынд Ымь вой ынтоарче привириле де ла ей!
13 Ndaona Efereimu ngati Turo, atadzalidwa pa nthaka ya chonde. Koma Efereimu adzatsogolera ana ake kuti akaphedwe.”
Ефраим, дупэ кум вэд, ышь дэ копиий ла прадэ ши Ефраим ышь ва дуче сингур копиий ла чел че-й ва учиде!”
14 Inu Yehova, muwapatse. Kodi mudzawapatsa chiyani? Apatseni mimba yomangopita padera ndi mawere owuma.
Дэ-ле, Доамне!… Че сэ ле дай?… Дэ-ле ун пынтече каре сэ наскэ ынаинте де време ши цыце сечь!
15 “Chifukwa cha zoyipa zawo zonse ku Giligala, Ine ndinawada kumeneko. Chifukwa cha machitidwe awo auchimo, ndidzawapirikitsa mʼnyumba yanga. Sindidzawakondanso; atsogoleri awo onse ndi owukira.
„Тоатэ рэутатя лор есте ла Гилгал; аколо М-ам скырбит де ей. Дин причина рэутэций фаптелор лор, ый вой изгони дин Каса Мя. Ну-й май пот юби, тоате кэпетенииле лор сунт ниште ындэрэтничь.
16 Efereimu wathedwa, mizu yake yauma sakubalanso zipatso. Ngakhale atabereka ana, Ine ndidzapha ana awo okondedwawo.”
Ефраим есте ловит, рэдэчина и с-а ускат; ну май дау род ши, кяр дакэ ау копий, ле вой оморы родул юбит де ей.”
17 Mulungu wanga adzawakana chifukwa sanamumvere Iye; adzakhala oyendayenda pakati pa anthu a mitundu ina.
Думнезеул меу ый ва лепэда, пентру кэ ну Л-ау аскултат, де ачея вор рэтэчи принтре нямурь.

< Hoseya 9 >