< Hoseya 9 >
1 Iwe Israeli, usakondwere; monga imachitira mitundu ina. Pakuti wakhala wosakhulupirika kwa Mulungu wako; umakonda malipiro a chiwerewere pa malo aliwonse opunthira tirigu.
Ne te réjouis pas, Israël; n’exulte pas comme les peuples: parce que tu as forniqué en te séparant de ton Dieu, tu as aimé la récompense plus que toutes les aires de blé.
2 Malo opunthira tirigu ndi malo opsinyira mphesa sadzadyetsa anthu; adzasowa vinyo watsopano.
L’aire et le pressoir ne les nourriront pas, et le vin trompera leur attente.
3 Sadzakhalanso mʼdziko la Yehova. Efereimu adzabwerera ku Igupto ndipo mudzadya chakudya chodetsedwa ku Asiriya.
Ils n’habiteront pas dans la terre du Seigneur; Ephraïm est retourné en Egypte, il mange parmi les Assyriens ce qui est impur.
4 Iwo sadzaperekanso chopereka cha chakumwa kwa Yehova, kapena nsembe zawo kuti akondweretse Yehovayo. Nsembe zotere zidzakhala kwa iwo ngati chakudya cha anamfedwa; onse akudya chakudya chimenechi adzakhala odetsedwa. Chakudya ichi chidzakhala chodya okha, sichidzalowa mʼnyumba ya Yehova.
Ils ne feront pas au Seigneur de libations de vin, et ils ne lui plairont pas; leurs sacrifices seront comme le pain de ceux qui sont en deuil; tous ceux qui en mangeront seront souillés; parce que leur pain sera pour leur âme, il n’entrera pas dans la maison du Seigneur.
5 Kodi mudzachita chiyani pa tsiku la maphwando anu oyikika; pa masiku a zikondwerero za Yehova?
Que ferez-vous au jour solennel, au jour de la fête du Seigneur?
6 Ngakhale iwo atathawa chiwonongeko, Igupto adzawasonkhanitsa, ndipo Mefisi adzawayika mʼmanda. Khwisa adzamera pa ziwiya zawo zasiliva, ndipo minga idzamera mʼmatenti awo.
Car voilà qu’ils sont partis à cause de la dévastation; l’Egypte les ramassera, Memphis les ensevelira; l’argent, objet de leurs désirs, l’ortie en héritera, la bardane croîtra dans leurs tabernacles.
7 Masiku achilango akubwera, masiku obwezera ali pafupi. Israeli adziwe zimenezi. Chifukwa machimo anu ndi ochuluka kwambiri ndipo udani wanu pa Mulungu ndi waukulu kwambiri. Mneneri amamuyesa chitsiru, munthu wanzeru za kwa Mulungu ngati wamisala.
Ils sont venus, les jours de la visite; ils sont venus, les jours de la rétribution; sachez, Israël, que le prophète est un fou, et l’homme inspiré, un insensé, à cause de la grandeur de ta démence.
8 Mneneri pamodzi ndi Mulungu wanga ndiwo alonda a Efereimu, koma mneneri amutchera misampha mʼnjira zake zonse, ndipo udani ukumudikira mʼnyumba ya Mulungu wake.
Ephraïm est une sentinelle avec mon Dieu; le prophète est devenu un lacs de ruine sur toutes ses voies, une démence dans la maison de son Dieu.
9 Iwo azama mu zachinyengo monga masiku a Gibeya. Mulungu adzakumbukira zolakwa zawo ndipo adzawalanga chifukwa cha machimo awo.
Ils ont péché profondément, comme aux jours de Gabaa; le Seigneur se souviendra de leur iniquité, et il visitera leurs péchés.
10 “Pamene ndinamupeza Israeli zinali ngati kupeza mphesa mʼchipululu. Nditaona makolo anu, zinali ngati ndikuona nkhuyu zoyambirira kupsa. Koma atafika ku Baala Peori, anadzipereka ku fano lija lochititsa manyazi ndipo anakhala onyansa ngati chinthu chimene anachikondacho.
J’ai trouvé Israël comme on rencontre des grappes de raisin dans le désert; j’ai vu leurs pères comme les premiers fruits qui paraissent au sommet d’un figuier; pour eux, ils sont entrés à Béelphégor, et ils se sont éloignés de moi pour leur confusion, et ils sont devenus abominables comme les choses qu’ils ont aimées.
11 Ulemerero wa Efereimu udzawuluka ngati mbalame. Sipadzakhalanso kubereka ana, kuyembekezera kapena kutenga pathupi.
Ephraïm, sa gloire a disparu comme l’oiseau, dès son enfantement et dès le sein de sa mère, et dès sa conception.
12 Ngakhale atalera ana ndidzachititsa kuti mwana aliyense amwalire. Tsoka kwa anthuwo pamene Ine ndidzawafulatira!
Et que s’ils ont élevé des fils, je ferai qu’ils seront sans enfants parmi les hommes; mais aussi malheur à eux. quand je me serai retiré d’eux.
13 Ndaona Efereimu ngati Turo, atadzalidwa pa nthaka ya chonde. Koma Efereimu adzatsogolera ana ake kuti akaphedwe.”
Ephraïm, comme je l’ai vu, était une autre Tyr, fondée sur la beauté; et Ephraïm conduira ses fils au meurtrier.
14 Inu Yehova, muwapatse. Kodi mudzawapatsa chiyani? Apatseni mimba yomangopita padera ndi mawere owuma.
Donnez-leur, Seigneur, Que leur donnerez-vous? Donnez-leur un sein sans enfants, et des mamelles arides.
15 “Chifukwa cha zoyipa zawo zonse ku Giligala, Ine ndinawada kumeneko. Chifukwa cha machitidwe awo auchimo, ndidzawapirikitsa mʼnyumba yanga. Sindidzawakondanso; atsogoleri awo onse ndi owukira.
Toutes leurs méchancetés se sont montrées à Galgal; parce que c’est là que je les ai eus en horreur; à cause de la malice de leurs inventions, je les chasserai de ma maison, je ne les aimerai plus; tous leurs princes se retirent de moi.
16 Efereimu wathedwa, mizu yake yauma sakubalanso zipatso. Ngakhale atabereka ana, Ine ndidzapha ana awo okondedwawo.”
Ephraïm a été frappé, leur racine a été desséchée; ils ne porteront pas du tout de fruit. Et que s’ils ont engendré, je ferai périr les fruits de leur sein qui leur sont les plus chers.
17 Mulungu wanga adzawakana chifukwa sanamumvere Iye; adzakhala oyendayenda pakati pa anthu a mitundu ina.
Mon Dieu les rejettera, parce qu’ils ne l’ont pas écouté; et ils seront errants parmi les nations.