< Hoseya 9 >

1 Iwe Israeli, usakondwere; monga imachitira mitundu ina. Pakuti wakhala wosakhulupirika kwa Mulungu wako; umakonda malipiro a chiwerewere pa malo aliwonse opunthira tirigu.
Glæd dig ikke, Israel! indtil Jubel, som Folkene; thi du har bedrevet Hor og vendt dig fra din Gud, du har elsket Bolerlønnen paa alle Kornloer.
2 Malo opunthira tirigu ndi malo opsinyira mphesa sadzadyetsa anthu; adzasowa vinyo watsopano.
Loen og Persen skulle ikke føde dem, og Mosten skal slaa dem fejl.
3 Sadzakhalanso mʼdziko la Yehova. Efereimu adzabwerera ku Igupto ndipo mudzadya chakudya chodetsedwa ku Asiriya.
De skulle ikke blive boende i Herrens Land; men Efraim skal komme tilbage til Ægypten, og i Assyrien skulle de æde, hvad der er urent.
4 Iwo sadzaperekanso chopereka cha chakumwa kwa Yehova, kapena nsembe zawo kuti akondweretse Yehovayo. Nsembe zotere zidzakhala kwa iwo ngati chakudya cha anamfedwa; onse akudya chakudya chimenechi adzakhala odetsedwa. Chakudya ichi chidzakhala chodya okha, sichidzalowa mʼnyumba ya Yehova.
De skulle ikke udøse Vin til Drikoffer for Herren, og deres Slagtofre skulle ikke behage ham; deres Brød er som Sorgens Brød, alle, som æde det, skulle blive urene; thi deres Brød er for deres egen Trang, det kommer ikke i Herrens Hus.
5 Kodi mudzachita chiyani pa tsiku la maphwando anu oyikika; pa masiku a zikondwerero za Yehova?
Hvad ville I gøre paa Højtidsdagen og paa Herrens Festdag?
6 Ngakhale iwo atathawa chiwonongeko, Igupto adzawasonkhanitsa, ndipo Mefisi adzawayika mʼmanda. Khwisa adzamera pa ziwiya zawo zasiliva, ndipo minga idzamera mʼmatenti awo.
Thi se, de gaa bort for Ødelæggelsen, Ægypten skal samle dem, Mof skal begrave dem; Nælder skulle arve deres yndige Ting af Sølv, Torne skulle vokse op i deres Telte.
7 Masiku achilango akubwera, masiku obwezera ali pafupi. Israeli adziwe zimenezi. Chifukwa machimo anu ndi ochuluka kwambiri ndipo udani wanu pa Mulungu ndi waukulu kwambiri. Mneneri amamuyesa chitsiru, munthu wanzeru za kwa Mulungu ngati wamisala.
Hjemsøgelsens Dage ere komne, Betalingens Dage ere komne, Israel skal fornemme det; en Daare er Profeten, en gal er Aandens Mand — for din store Misgernings og den heftige Efterstræbelses Skyld.
8 Mneneri pamodzi ndi Mulungu wanga ndiwo alonda a Efereimu, koma mneneri amutchera misampha mʼnjira zake zonse, ndipo udani ukumudikira mʼnyumba ya Mulungu wake.
Efraim ser sig om, foruden til min Gud; Profeten er en Fuglefængers Snare paa alle hans Veje, der er Efterstræbelser i hans Guds Hus.
9 Iwo azama mu zachinyengo monga masiku a Gibeya. Mulungu adzakumbukira zolakwa zawo ndipo adzawalanga chifukwa cha machimo awo.
De ere sunkne dybt i Fordærvelse som i Gibeas Dage; han skal ihukomme deres Misgerning, han skal hjemsøge deres Synder.
10 “Pamene ndinamupeza Israeli zinali ngati kupeza mphesa mʼchipululu. Nditaona makolo anu, zinali ngati ndikuona nkhuyu zoyambirira kupsa. Koma atafika ku Baala Peori, anadzipereka ku fano lija lochititsa manyazi ndipo anakhala onyansa ngati chinthu chimene anachikondacho.
Jeg fandt Israel som Druer i Ørken, jeg saa eders Fædre som den tidlige Frugt paa Figentræet i dets første Tid; men de gik ind til Baal-Peor og viede sig til Skændsel, og de bleve en Vederstyggelighed ligesom deres Boler.
11 Ulemerero wa Efereimu udzawuluka ngati mbalame. Sipadzakhalanso kubereka ana, kuyembekezera kapena kutenga pathupi.
Efraims Herlighed skal bortflyve som en Fugl; ingen føder, og ingen bliver frugtsommelig, og ingen undfanger.
12 Ngakhale atalera ana ndidzachititsa kuti mwana aliyense amwalire. Tsoka kwa anthuwo pamene Ine ndidzawafulatira!
Thi om de end opføde deres Børn, vil jeg dog berøve dem deres Børn, saa at intet Menneske bliver tilbage; thi ve dem selv, naar jeg viger fra dem!
13 Ndaona Efereimu ngati Turo, atadzalidwa pa nthaka ya chonde. Koma Efereimu adzatsogolera ana ake kuti akaphedwe.”
Efraim er, som om jeg ser hen til Tyrus, plantet paa en Eng; men Efraim maa føre sine Børn ud til Manddraberen.
14 Inu Yehova, muwapatse. Kodi mudzawapatsa chiyani? Apatseni mimba yomangopita padera ndi mawere owuma.
Giv dem, Herre! — ja, hvad skal du give? Giv dem ufrugtbart Moderliv og udtørrede Bryster.
15 “Chifukwa cha zoyipa zawo zonse ku Giligala, Ine ndinawada kumeneko. Chifukwa cha machitidwe awo auchimo, ndidzawapirikitsa mʼnyumba yanga. Sindidzawakondanso; atsogoleri awo onse ndi owukira.
Al deres Ondskab er i Gilgal; thi der har jeg fattet Had til dem, for deres Idrætters Ondskabs Skyld vil jeg udstøde dem af mit Hus, jeg vil ikke blive ved at elske dem; alle deres Fyrster ere genstridige.
16 Efereimu wathedwa, mizu yake yauma sakubalanso zipatso. Ngakhale atabereka ana, Ine ndidzapha ana awo okondedwawo.”
Ramt er Efraim, deres Rod er bleven tør, de skulle ikke bære Frugt; og om de end føde, vil jeg dog dræbe deres elskede Livsfrugt.
17 Mulungu wanga adzawakana chifukwa sanamumvere Iye; adzakhala oyendayenda pakati pa anthu a mitundu ina.
Min Gud skal forkaste dem, thi de have ikke hørt ham, og de skulle vanke hid og did iblandt Hedningerne.

< Hoseya 9 >