< Hoseya 8 >
1 “Ika lipenga pakamwa pako. Ngati chiwombankhanga, kutsutsana ndi nyumba ya Yehova chifukwa anthu aphwanya pangano langa ndiponso agalukira lamulo langa.
“Place a trumpet at your lips! An eagle is coming over the house of Yahweh because the people have broken my covenant and rebelled against my law.
2 Israeli akulirira kwa Ine kuti, ‘Inu Mulungu wathu, ife timakudziwani!’
They cry out to me, 'My God, we in Israel know you.'
3 Koma Israeli wakana zabwino; mdani adzamuthamangitsa.
But Israel has rejected what is good, and the enemy will pursue him.
4 Amalonga mafumu mosatsata kufuna kwanga. Amasankha akalonga popanda chilolezo changa. Amadzipangira mafano asiliva ndi agolide koma adzawonongeka nawo.
They have set up kings, but not by me. They have made princes, but without my knowledge. With their silver and gold they have made idols for themselves, but it was only so they might be cut off.”
5 Iwe Samariya, taya fano lako la mwana wangʼombe! Mkwiyo wanga wayakira anthuwo. Padzapita nthawi yayitali chotani asanasinthike kukhala oyera mtima?
“Your calf has been rejected, Samaria. My anger is burning against these people. For how long will they stay guilty?
6 Mafanowa ndi ochokera ku Israeli! Mwana wa ngʼombe uyu anapangidwa ndi munthu waluso; si Mulungu amene anamupanga. Adzaphwanyidwa nʼkukhala zidutswa, mwana wangʼombe wa ku Samariya.
For this idol came from Israel; a workman made it; it is not God! The calf of Samaria will be broken to pieces.
7 “Aisraeli amadzala mphepo ndipo amakolola kamvuluvulu. Tirigu alibe ngala; sadzabala chakudya. Akanabala chakudya alendo akanadya chakudyacho.
For the people sow the wind and reap the whirlwind. The standing grain has no heads; it yields no flour. If it does come to maturity, foreigners will devour it.
8 Israeli wamezedwa, tsopano ali pakati pa anthu a mitundu ina ngati chinthu cha chabechabe.
Israel is swallowed up; now they lie among the nations like something useless.
9 Pakuti iwo anapita ku Asiriya ngati mbidzi yongodziyendera pa yokha. Efereimu wadzigulitsa kwa zibwenzi zake.
For they went up to Assyria like a wild donkey all alone. Ephraim has hired lovers for herself.
10 Ngakhale wadzigulitsa pakati pa mitundu ya anthu, Ine ndidzawasonkhanitsa pamodzi. Iwo adzayamba kuzunzika pansi pa ulamuliro wankhanza wa mfumu yamphamvu.
Even though they have hired lovers among the nations, I will now gather them together. They will begin to waste away because of the oppression of the king of princes.
11 “Ngakhale Efereimu anamanga maguwa ambiri a nsembe zoperekedwa chifukwa cha tchimo, maguwa amenewa akhala malo ochimwirapo.
For Ephraim has multiplied altars for sin offerings, but they have become altars for committing sins instead.
12 Ndinawalembera zinthu zambiri za malamulo anga, koma iwo anaziyesa ngati zinthu zachilendo.
I could write down my law for them ten thousand times, but they would view it as something strange to them.
13 Amapereka nsembe za nyama kwa Ine ndipo iwo amadya nyamayo, koma Yehova sakondwera nazo. Tsopano Iye adzakumbukira zoyipa zawo ndi kuwalanga chifukwa cha machimo awo: iwowo adzabwerera ku Igupto.
As for the sacrifices of my offerings, they sacrifice meat and eat it, but I, Yahweh, do not accept them. Now I will think about their iniquity and punish their sins. They will return to Egypt.
14 Israeli wayiwala Mlengi wake ndipo wamanga nyumba zaufumu; Yuda wachulukitsa mizinda ya malinga. Koma Ine ndidzaponya moto pa mizinda yawoyo, moto umene udzatenthe malinga awo.”
Israel has forgotten me, his Maker, and has built palaces. Judah has fortified many cities, but I will send fire on his cities; it will destroy his fortresses.