< Hoseya 8 >

1 “Ika lipenga pakamwa pako. Ngati chiwombankhanga, kutsutsana ndi nyumba ya Yehova chifukwa anthu aphwanya pangano langa ndiponso agalukira lamulo langa.
Basunen for din Gane! Som en Ørn over Herrens Hus! fordi de have overtraadt min Pagt og forbrudt sig imod min Lov.
2 Israeli akulirira kwa Ine kuti, ‘Inu Mulungu wathu, ife timakudziwani!’
Til mig raabe de: Min Gud! vi, Israel, kende dig.
3 Koma Israeli wakana zabwino; mdani adzamuthamangitsa.
Israel har forkastet det gode; Fjenden forfølge ham!
4 Amalonga mafumu mosatsata kufuna kwanga. Amasankha akalonga popanda chilolezo changa. Amadzipangira mafano asiliva ndi agolide koma adzawonongeka nawo.
De have indsat Konger, men ikke fra mig; de have indsat Fyrster, men jeg vidste det ikke; de have gjort sig Afguder af deres Sølv og deres Guld, for at det kan udryddes.
5 Iwe Samariya, taya fano lako la mwana wangʼombe! Mkwiyo wanga wayakira anthuwo. Padzapita nthawi yayitali chotani asanasinthike kukhala oyera mtima?
Din Kalv, Samaria! er forkastet, min Vrede er optændt imod dem, hvor længe? de taale ikke Renhed.
6 Mafanowa ndi ochokera ku Israeli! Mwana wa ngʼombe uyu anapangidwa ndi munthu waluso; si Mulungu amene anamupanga. Adzaphwanyidwa nʼkukhala zidutswa, mwana wangʼombe wa ku Samariya.
Thi af Israel er ogsaa den, en Mester har gjort den, og den er ikke en Gud; men til Splinter bliver Samarias Kalv.
7 “Aisraeli amadzala mphepo ndipo amakolola kamvuluvulu. Tirigu alibe ngala; sadzabala chakudya. Akanabala chakudya alendo akanadya chakudyacho.
Thi Vind saa de, og Storm høste de; Korn paa Roden have de ej, Grøden giver ikke Mel, og om den end giver det, skulle fremmede opsluge det.
8 Israeli wamezedwa, tsopano ali pakati pa anthu a mitundu ina ngati chinthu cha chabechabe.
Opslugt er Israel; nu ere de blevne iblandt Hedningerne som et Kar, hvortil ingen har Lyst.
9 Pakuti iwo anapita ku Asiriya ngati mbidzi yongodziyendera pa yokha. Efereimu wadzigulitsa kwa zibwenzi zake.
Thi de droge op til Assyrien som et Vildæsel, der gaar sine egne Veje; Efraim tingede om Elskov.
10 Ngakhale wadzigulitsa pakati pa mitundu ya anthu, Ine ndidzawasonkhanitsa pamodzi. Iwo adzayamba kuzunzika pansi pa ulamuliro wankhanza wa mfumu yamphamvu.
Men tinge de iblandt Folkene, saa vil jeg dog nu samle dem; og de skulle begynde at mindskes under Trykket af Fyrsternes Konge.
11 “Ngakhale Efereimu anamanga maguwa ambiri a nsembe zoperekedwa chifukwa cha tchimo, maguwa amenewa akhala malo ochimwirapo.
Thi Efraim byggede mange Altre til at synde ved; han har faaet Altre til at synde ved.
12 Ndinawalembera zinthu zambiri za malamulo anga, koma iwo anaziyesa ngati zinthu zachilendo.
Jeg skriver ham mine mangfoldige Love; de ere blevne agtede som noget fremmed.
13 Amapereka nsembe za nyama kwa Ine ndipo iwo amadya nyamayo, koma Yehova sakondwera nazo. Tsopano Iye adzakumbukira zoyipa zawo ndi kuwalanga chifukwa cha machimo awo: iwowo adzabwerera ku Igupto.
Som Ofre, de bringe mig, ofre de Kød og æde; Herren finder ikke Behag i dem; nu vil han komme deres Misgerning i Hu og hjemsøge deres Synder; de skulle komme tilbage til Ægypten.
14 Israeli wayiwala Mlengi wake ndipo wamanga nyumba zaufumu; Yuda wachulukitsa mizinda ya malinga. Koma Ine ndidzaponya moto pa mizinda yawoyo, moto umene udzatenthe malinga awo.”
Og Israel forglemte sin Skaber og byggede Paladser, og Juda opførte mange faste Stæder; men jeg vil sende Ild i hans Stæder, og den skal fortære hans Paladser.

< Hoseya 8 >