< Hoseya 7 >

1 Pamene ndichiritsa Israeli, machimo a Efereimu amaonekera poyera ndiponso milandu ya Samariya sibisika. Iwo amachita zachinyengo, mbala zimathyola nyumba, achifwamba amalanda anthu katundu mʼmisewu.
Кад лечим Израиља, тада се показује безакоње Јефремово и злоћа самаријска; јер чине лаж, и лупеж улази, и напољу удара чета.
2 Koma sazindikira kuti Ine ndimakumbukira zoyipa zawo zonse. Azunguliridwa ndi zolakwa zawo; ndipo sizichoka mʼmaso mwanga.
И не говоре у срцу свом да ја памтим свако безакоње њихово; сада стоје око њих дела њихова, преда мном су.
3 “Anthuwa amasangalatsa mfumu ndi zoyipa zawozo, akalonga amasekerera mabodza awo.
Неваљалством својим веселе цара и лажима својим кнезове.
4 Onsewa ndi anthu azigololo, otentha ngati moto wa mu uvuni, umene wophika buledi sasonkhezera kuyambira pamene akukanda buledi mpaka atafufuma.
Сви чине прељубу; као пећ су коју ужари хлебар, који престане стражити кад замеси тесто па докле ускисне.
5 Pa tsiku la chikondwerero cha mfumu yathu akalonga amaledzera ndi vinyo, ndipo amalowa mʼgulu la anthu achipongwe.
На дан цара нашег разболеше се кнезови од меха вина, и он пружи руку своју подсмевачима.
6 Mitima yawo ili ngati uvuni; amayandikira Mulungu mwachiwembu. Ukali wawo umanyeka usiku wonse, mmawa umayaka ngati malawi a moto.
Јер на заседе своје управљају срце своје, које је као пећ; хлебар њихов спава целу ноћ, ујутру гори као пламен огњени.
7 Onsewa ndi otentha ngati uvuni, amapha olamulira awo. Mafumu awo onse amagwa, ndipo palibe ndi mmodzi yemwe amandiyitana Ine.
Сви су као пећ угрејани и прождиру своје судије; сви цареви њихови падају, ниједан између њих не виче к мени.
8 “Efereimu wasakanikirana ndi mitundu ya anthu ena; Efereimu ndi buledi amene wapsa mbali imodzi.
Јефрем се помешао с народима; Јефрем је погача непреврнута.
9 Alendo atha mphamvu zake, koma iye sakuzindikira. Tsitsi lake layamba imvi koma iye sakudziwa.
Иностранци једу му силу, а он не зна; седе косе попадају га, а он не зна.
10 Kunyada kwake Israeli kukumutsutsa, koma pa zonsezi iye sakubwerera kwa Yehova Mulungu wake kapena kumufunafuna.
И поноситост Израиљева сведочи му у очи, али се не враћају ка Господу Богу свом нити Га траже уза све то.
11 “Efereimu ali ngati nkhunda yopusa yopanda nzeru. Amayitana Igupto namapita ku Asiriya.
И Јефрем је као голуб, луд, безуман; зову Мисир, иду у Асирску.
12 Akamadzapita, ndidzawakola ndi ukonde wanga; ndidzawagwetsa pansi ngati mbalame zamumlengalenga. Ndikadzamva kuti asonkhana pamodzi ndidzawakola.
Кад отиду, разапећу на њих мрежу своју, као птице небеске свући ћу их, караћу их како је казивано у збору њиховом.
13 Tsoka kwa iwo, chifukwa andisiya Ine! Chiwonongeko kwa iwo, chifukwa andiwukira! Ndimafunitsitsa kuwapulumutsa koma amayankhula za Ine monama.
Тешко њима, јер зађоше од мене; погибао ће им бити, јер ме изневерише; ја их искупих, а они говорише на ме лаж.
14 Iwo salirira kwa Ine kuchokera pansi pa mtima, koma amalira mofuwula ali pa bedi pawo. Amadzichekacheka chifukwa chofuna tirigu ndi vinyo watsopano, koma amandifulatira.
Нити ме призиваше из срца свог, него ридаше на одрима својим; жита и вина ради скупљајући се одступају од мене.
15 Ine ndinawaphunzitsa ndikuwalimbitsa, koma amandikonzera chiwembu.
Кад их карах, укрепих им мишице; али они мислише зло на ме.
16 Iwo satembenukira kwa Wammwambamwamba; ali ngati uta woonongeka. Atsogoleri awo adzaphedwa ndi lupanga chifukwa cha mawu awo achipongwe. Motero iwo adzasekedwa mʼdziko la Igupto.
Враћају се, али не ка Вишњем, посташе као лук лажљив; кнезови ће њихови попадати од мача с обести језика свог; то ће им бити подсмех у земљи мисирској.

< Hoseya 7 >