< Hoseya 7 >

1 Pamene ndichiritsa Israeli, machimo a Efereimu amaonekera poyera ndiponso milandu ya Samariya sibisika. Iwo amachita zachinyengo, mbala zimathyola nyumba, achifwamba amalanda anthu katundu mʼmisewu.
when I would heal Israel, then Ephrain’s guilt is revealed, and Samaria’s crimes are seen, how they practise fraud and the thief enters in, while outside bandits plunder.
2 Koma sazindikira kuti Ine ndimakumbukira zoyipa zawo zonse. Azunguliridwa ndi zolakwa zawo; ndipo sizichoka mʼmaso mwanga.
But it never crosses their minds that I remember their wickedness. Now their misdeeds surround them, they are always before my face.
3 “Anthuwa amasangalatsa mfumu ndi zoyipa zawozo, akalonga amasekerera mabodza awo.
Their wickedness amuses the king, and their lying gladdens the princes,
4 Onsewa ndi anthu azigololo, otentha ngati moto wa mu uvuni, umene wophika buledi sasonkhezera kuyambira pamene akukanda buledi mpaka atafufuma.
since they are all of them adulterers. Their desire to do evil burns like an oven heated by the baker, so hot that he need not stir the fire, from the kneading of the dough, until it rises.
5 Pa tsiku la chikondwerero cha mfumu yathu akalonga amaledzera ndi vinyo, ndipo amalowa mʼgulu la anthu achipongwe.
On our king’s festival day, the princes are flushed with fever from wine. He stretched forth his hand with the contemptuous,
6 Mitima yawo ili ngati uvuni; amayandikira Mulungu mwachiwembu. Ukali wawo umanyeka usiku wonse, mmawa umayaka ngati malawi a moto.
for like an oven their heart burns with treachery, all night their anger smoulders, in the morning it blazes into a flame of fire.
7 Onsewa ndi otentha ngati uvuni, amapha olamulira awo. Mafumu awo onse amagwa, ndipo palibe ndi mmodzi yemwe amandiyitana Ine.
All of them glow like an oven, they devour their rulers. All their kings have fallen. There is none among them who calls to me.
8 “Efereimu wasakanikirana ndi mitundu ya anthu ena; Efereimu ndi buledi amene wapsa mbali imodzi.
Ephraim – he lets himself be mixed among the peoples, Ephraim – he has become a cake unturned.
9 Alendo atha mphamvu zake, koma iye sakuzindikira. Tsitsi lake layamba imvi koma iye sakudziwa.
Strangers have devoured his strength, but he does not know it. His hair is sprinkled with grey, but he does not notice.
10 Kunyada kwake Israeli kukumutsutsa, koma pa zonsezi iye sakubwerera kwa Yehova Mulungu wake kapena kumufunafuna.
Israel’s arrogance testifies against them yet they do not return to the Lord their God, and in all this they do not seek him.
11 “Efereimu ali ngati nkhunda yopusa yopanda nzeru. Amayitana Igupto namapita ku Asiriya.
Ephraim is like a simple, silly dove: to Egypt they call, after Assyria they go,
12 Akamadzapita, ndidzawakola ndi ukonde wanga; ndidzawagwetsa pansi ngati mbalame zamumlengalenga. Ndikadzamva kuti asonkhana pamodzi ndidzawakola.
wherever they turn I will spread my net over them, like birds of the sky I will bring them down, I will catch them when I hear them gathering.
13 Tsoka kwa iwo, chifukwa andisiya Ine! Chiwonongeko kwa iwo, chifukwa andiwukira! Ndimafunitsitsa kuwapulumutsa koma amayankhula za Ine monama.
Woe to them, for they have strayed from me! Destruction to them, for they have been untrue to me. Although it was I who redeemed them, they speak lies about me.
14 Iwo salirira kwa Ine kuchokera pansi pa mtima, koma amalira mofuwula ali pa bedi pawo. Amadzichekacheka chifukwa chofuna tirigu ndi vinyo watsopano, koma amandifulatira.
They have never cried to me with their hearts, but they are always wailing on their beds. They gather to beg for corn and new wine, but they turn away from me.
15 Ine ndinawaphunzitsa ndikuwalimbitsa, koma amandikonzera chiwembu.
Although it was I who trained and strengthened their arms, concerning me they plan only evil.
16 Iwo satembenukira kwa Wammwambamwamba; ali ngati uta woonongeka. Atsogoleri awo adzaphedwa ndi lupanga chifukwa cha mawu awo achipongwe. Motero iwo adzasekedwa mʼdziko la Igupto.
They turn away from the Most High. They have become like a bow that swerves. Their princes will fall by the sword, because of the insolence of their tongues. The land of Egypt will mock them.

< Hoseya 7 >