< Hoseya 7 >

1 Pamene ndichiritsa Israeli, machimo a Efereimu amaonekera poyera ndiponso milandu ya Samariya sibisika. Iwo amachita zachinyengo, mbala zimathyola nyumba, achifwamba amalanda anthu katundu mʼmisewu.
Když léčím Izraele, tedy zjevuje se nepravost Efraimova a zlosti Samařské; nebo provodí faleš. Vnitř zlodějství, a vně provozují loupežnictví.
2 Koma sazindikira kuti Ine ndimakumbukira zoyipa zawo zonse. Azunguliridwa ndi zolakwa zawo; ndipo sizichoka mʼmaso mwanga.
Aniž na to pomýšlejí v srdci svém, že na všecku nešlechetnost jejich pamatují; již je obkličují skutkové jejich, a před mým oblíčejem jsou.
3 “Anthuwa amasangalatsa mfumu ndi zoyipa zawozo, akalonga amasekerera mabodza awo.
Nešlechetností svou obveselují krále, a klamy svými knížata.
4 Onsewa ndi anthu azigololo, otentha ngati moto wa mu uvuni, umene wophika buledi sasonkhezera kuyambira pamene akukanda buledi mpaka atafufuma.
Všickni napořád cizoloží, podobni jsouce peci zanícené od pekaře, kterýž přestává bdíti, jen ažby zadělané těsto zkynulo.
5 Pa tsiku la chikondwerero cha mfumu yathu akalonga amaledzera ndi vinyo, ndipo amalowa mʼgulu la anthu achipongwe.
V den krále našeho k nemoci jej přivodí knížata láhvicí vína; vztahuje ruku svou s posměvači.
6 Mitima yawo ili ngati uvuni; amayandikira Mulungu mwachiwembu. Ukali wawo umanyeka usiku wonse, mmawa umayaka ngati malawi a moto.
Nebo přiložili k úkladům svým srdce své podobné peci; celou noc spí pekař jejich, v jitře hoří jako plamen ohně.
7 Onsewa ndi otentha ngati uvuni, amapha olamulira awo. Mafumu awo onse amagwa, ndipo palibe ndi mmodzi yemwe amandiyitana Ine.
Všickni napořád rozpáleni jsou jako pec, a zžírají soudce své; všickni králové jejich padají, aniž kdo z nich volá ke mně.
8 “Efereimu wasakanikirana ndi mitundu ya anthu ena; Efereimu ndi buledi amene wapsa mbali imodzi.
Efraim s národy smísil se, Efraim bude chléb podpopelný neobrácený.
9 Alendo atha mphamvu zake, koma iye sakuzindikira. Tsitsi lake layamba imvi koma iye sakudziwa.
Cizozemci zžírají sílu jeho, ačkoli on toho nezná; i šedinami prokvítaje, však vždy toho nezná.
10 Kunyada kwake Israeli kukumutsutsa, koma pa zonsezi iye sakubwerera kwa Yehova Mulungu wake kapena kumufunafuna.
A ačkoli pýcha Izraelova svědčí vůči proti němu, však se nenavracují k Hospodinu Bohu svému, aniž ho hledají s tím se vším.
11 “Efereimu ali ngati nkhunda yopusa yopanda nzeru. Amayitana Igupto namapita ku Asiriya.
A Efraim jest jako holubice hloupá bez srdce; k Egyptskému králi volají, k Assyrskému se utíkají.
12 Akamadzapita, ndidzawakola ndi ukonde wanga; ndidzawagwetsa pansi ngati mbalame zamumlengalenga. Ndikadzamva kuti asonkhana pamodzi ndidzawakola.
Když odejdou, roztáhnu na ně sítku svou, a jako ptactvo nebeské přitrhnu je; kárati je budu tak, jakž slýcháno bylo o tom v shromáždění jejich.
13 Tsoka kwa iwo, chifukwa andisiya Ine! Chiwonongeko kwa iwo, chifukwa andiwukira! Ndimafunitsitsa kuwapulumutsa koma amayankhula za Ine monama.
Běda jim, že jsou poběhli mne. Zpuštění na ně, proto že se mi zpronevěřili, ješto jsem já je vykoupil, ale oni mluvili proti mně lži.
14 Iwo salirira kwa Ine kuchokera pansi pa mtima, koma amalira mofuwula ali pa bedi pawo. Amadzichekacheka chifukwa chofuna tirigu ndi vinyo watsopano, koma amandifulatira.
Aniž volají ke mně z srdce svého, když kvílí na ložcích svých, a když pro obilé a mest shromažďujíce se, obracejí se ke mně,
15 Ine ndinawaphunzitsa ndikuwalimbitsa, koma amandikonzera chiwembu.
Ješto já potrestav, posiloval jsem ramen jejich, ale oni proti mně zlé vymýšlejí.
16 Iwo satembenukira kwa Wammwambamwamba; ali ngati uta woonongeka. Atsogoleri awo adzaphedwa ndi lupanga chifukwa cha mawu awo achipongwe. Motero iwo adzasekedwa mʼdziko la Igupto.
Navracujíť se, ale ne k Nejvyššímu, jsou jako lučiště omylné, padají od meče knížata jejich, od rozhněvání jazyka jejich, což jim ku posměchu jest v zemi Egyptské.

< Hoseya 7 >