< Hoseya 6 >

1 “Bwerani, tiyeni tibwerere kwa Yehova. Iye watikhadzula, koma adzatichiritsa. Iye wativulaza, koma adzamanga mabala athu.
“Wozani sibuyele kuThixo. Usesidabule saba yizicucu kodwa uzaselapha; usilimazile kodwa uzawabopha amanxeba ethu.
2 Pakapita masiku awiri adzatitsitsimutsa; pa tsiku lachitatu Iye adzatiukitsa kuti tikhale ndi moyo pamaso pake.
Emva kwensuku ezimbili uzasivuselela; ngosuku lwesithathu uzasibuyisela ukuze sihlale lapho akhona.
3 Tiyeni timudziwe Yehova, tiyeni tilimbike kumudziwa Iye. Adzabwera kwa ife mosakayikira konse ngati kutuluka kwa dzuwa; adzabwera kwa ife ngati mvula ya mʼchilimwe, ngati mvula ya nthawi yamphukira imene imakhathamiritsa nthaka.”
Kasimamukeleni uThixo; kasiqiniseni ukumamukela. Ngoqotho njengoba ilanga liphuma, uzabonakala; uzakuza kithi njengezulu lebusika, lanjengezulu lentwasa elithambisa umhlaba.”
4 Iwe Efereimu, kodi ndichite nawe chiyani? Kodi ndichite nawe chiyani, iwe Yuda? Chikondi chanu chili ngati nkhungu yammawa, ngati mame a mmamawa amene amakamuka msanga.
“Ngingenzani ngawe, Efrayimi na? Ngingenzani ngawe, Juda na? Uthando lwenu lunjengenkungu yekuseni, lunjengamazolo ekuseni anyamalalayo.
5 Choncho ndakuwazani ngati nkhuni kudzera mwa aneneri anga, ndakuphani ndi mawu a pakamwa panga; chigamulo changa chinangʼanima ngati mphenzi pa inu.
Ngakho ngaliqumaquma ngabaphrofethi bami, ngalibulala ngamazwi omlomo wami; ukwahlulela kwami kwaphazima njengombane phezu kwenu.
6 Pakuti Ine ndimafuna chifundo osati nsembe, ndi kudziwa Mulungu kulekana ndi nsembe zopsereza.
Ngoba mina ngifuna isihawu, hatshi umhlatshelo, lokwamukela uNkulunkulu kuleminikelo yokutshiswa.
7 Monga Adamu, anthuwa aphwanya pangano langa, iwo sanakhulupirike kwa Ine.
Njengo-Adamu, sebesephule isivumelwano babengathembekanga khonale.
8 Giliyadi ndi mzinda wa anthu ochita zoyipa, okhala ndi zizindikiro za kuphana.
IGiliyadi lidolobho labantu abaxhwalileyo. Lingcolile ngezinyathelo zegazi
9 Monga momwe mbala zimadikirira anthu, magulu a ansembe amachitanso motero; iwo amapha anthu pa njira yopita ku Sekemu, kupalamula milandu yochititsa manyazi.
Njengezigebenga zicathamela umuntu, zenzanjalo izigangi zabaphristi; zibulala abantu emgwaqweni oya eShekhemu zisenza izinto ezimbi.
10 Ndaona chinthu choopsa kwambiri mʼnyumba ya Israeli. Kumeneko Efereimu akuchita zachiwerewere, ndipo Israeli wadzidetsa.
Sengibone into etshaqisayo endlini ka-Israyeli. U-Efrayimi uwela khonapho, lo-Israyeli ungcolisiwe.
11 “Kunenanso za iwe Yuda, udzakolola chilango. “Pamene ndiwabwezere anthu anga zinthu zabwino.”
Lakuwe futhi Juda, ukuvuna sekulungiselwe. Lapho ngingabuyisela inotho yabantu bami.

< Hoseya 6 >