< Hoseya 6 >
1 “Bwerani, tiyeni tibwerere kwa Yehova. Iye watikhadzula, koma adzatichiritsa. Iye wativulaza, koma adzamanga mabala athu.
Come, and let us return to the LORD: for he hath torn, and he will heal us; he hath smitten, and he will bind us up.
2 Pakapita masiku awiri adzatitsitsimutsa; pa tsiku lachitatu Iye adzatiukitsa kuti tikhale ndi moyo pamaso pake.
After two days will he revive us: in the third day will he raise us up, and we shall live in his sight.
3 Tiyeni timudziwe Yehova, tiyeni tilimbike kumudziwa Iye. Adzabwera kwa ife mosakayikira konse ngati kutuluka kwa dzuwa; adzabwera kwa ife ngati mvula ya mʼchilimwe, ngati mvula ya nthawi yamphukira imene imakhathamiritsa nthaka.”
Then shall we know, [if] we follow on to know the LORD: his going forth is prepared as the morning; and he will come to us as the rain, as the latter [and] former rain to the earth.
4 Iwe Efereimu, kodi ndichite nawe chiyani? Kodi ndichite nawe chiyani, iwe Yuda? Chikondi chanu chili ngati nkhungu yammawa, ngati mame a mmamawa amene amakamuka msanga.
O Ephraim, what shall I do to thee? O Judah, what shall I do to thee? for your goodness [is] as the morning cloud, and as the early dew it goeth away.
5 Choncho ndakuwazani ngati nkhuni kudzera mwa aneneri anga, ndakuphani ndi mawu a pakamwa panga; chigamulo changa chinangʼanima ngati mphenzi pa inu.
Therefore have I hewed [them] by the prophets; I have slain them by the words of my mouth: and thy judgments [are as] the light [that] goeth forth.
6 Pakuti Ine ndimafuna chifundo osati nsembe, ndi kudziwa Mulungu kulekana ndi nsembe zopsereza.
For I desired mercy, and not sacrifice: and the knowledge of God more than burnt-offerings.
7 Monga Adamu, anthuwa aphwanya pangano langa, iwo sanakhulupirike kwa Ine.
But they like men have transgressed the covenant: there have they dealt treacherously against me.
8 Giliyadi ndi mzinda wa anthu ochita zoyipa, okhala ndi zizindikiro za kuphana.
Gilead [is] a city of them that work iniquity, [and is] polluted with blood.
9 Monga momwe mbala zimadikirira anthu, magulu a ansembe amachitanso motero; iwo amapha anthu pa njira yopita ku Sekemu, kupalamula milandu yochititsa manyazi.
And as troops of robbers wait for a man, [so] the company of priests murder in the way by consent: for they commit lewdness.
10 Ndaona chinthu choopsa kwambiri mʼnyumba ya Israeli. Kumeneko Efereimu akuchita zachiwerewere, ndipo Israeli wadzidetsa.
I have seen a horrible thing in the house of Israel: there [is] the prostitution of Ephraim, Israel is defiled.
11 “Kunenanso za iwe Yuda, udzakolola chilango. “Pamene ndiwabwezere anthu anga zinthu zabwino.”
Also, O Judah, he hath set a harvest for thee, when I returned the captivity of my people.