< Hoseya 5 >

1 “Ansembe inu, imvani izi! Inu Aisraeli, tcherani khutu! Inu nyumba yaufumu, mvetserani! Chiweruzo ichi ndi chotsutsa inu: Inu munali ngati msampha ku Mizipa, munali ngati ukonde woyalidwa pa phiri la Tabori.
“Muntie, mo asɔfo! Monhyɛ eyi nso, mo Israelfo! Monyɛ asow, adehyefi! Saa atemmu yi tia mo: Moayɛ afiri wɔ Mispa, ne asau a wɔagu no Tabor so.
2 Owukira azama mʼmoyo wakupha, Ine ndidzawalanga onsewo.
Atuatewfo adɔ mogyahwiegu mu asukɔ. Mɛtwe wɔn nyinaa aso.
3 Ndimadziwa zonse za Efereimu; Aisraeli ndi osabisika kwa Ine. Efereimu wayamba tsopano kuchita zachiwerewere; Israeli wadziyipitsa.
Minim Efraim ho nsɛm nyinaa; wɔmfaa Israel nhintaw me ɛ. Efraim, mprempren de wobɔ aguaman; na Israel aporɔw.
4 “Ntchito zawo siziwalola kubwerera kwa Mulungu wawo. Mʼmitima mwawo muli mzimu wachiwerewere; Iwo sadziwa Yehova.
“Wɔn nneyɛe mma wɔ kwan mma wɔnnkɔ Nyankopɔn nkyɛn. Aguamammɔ honhom wɔ wɔn koma mu; wonnye Awurade nto mu.
5 Kudzikuza kwa Israeli kwakhala umboni womutsutsa; Aisraeli, ngakhale Aefereimu, anagwa mʼmachimo awo; Yudanso anagwa nawo pamodzi.
Israel ahantan di tia no. Israelfo no, mpo Efraim hintihintiw wɔ wɔn amumɔyɛ mu; Yuda nso ne wɔn hintiw saa ara.
6 Pamene adzapita ndi nkhosa zawo ndi ngʼombe zawo kukapereka nsembe kwa Yehova, iwo sadzamupeza; Iye wawachokera.
Sɛ wɔne wɔn nguan ne wɔn anantwi kɔhwehwɛ Awurade a Wɔrenhu no, efisɛ watwe ne ho afi wɔn ho.
7 Iwo ndi osakhulupirika kwa Yehova; amabereka ana amʼchigololo ndipo chikondwerero chawo cha mwezi watsopano chidzawawononga pamodzi ndi minda yawo.
Wɔanni Awurade nokware. Wɔwowoo aguaman mma. Sɛ wodi wɔn Ɔsram Foforo Afahyɛ a, ɔbɛsɛe wɔn nsase.
8 “Womba lipenga mu Gibeya, liza mbetete mu Rama. Fuwulani mfuwu wankhondo mu Beti-Aveni; iwe Benjamini tsogolera.
“Hyɛn torobɛnto no wɔ Gibea. Hyɛn mmɛn no wɔ Rama. Momma ɔko nteɛmu so wɔ Bet Awen; Benyamin, monsɔre nni anim.
9 Efereimu adzasanduka bwinja pa tsiku la chilango. Ine ndikulengeza zomwe zidzachitikadi pakati pa mafuko a Israeli.
Efraim bɛda mpan wɔ akontaabu da. Israel mmusuakuw no mu no mepae mu ka nea ɛwɔ mu.
10 Atsogoleri a Yuda ali ngati anthu amene amasuntha miyala ya mʼmalire. Ndidzawakhutulira ukali wanga ngati madzi a chigumula.
Yuda sodifo no te sɛ wɔn a woyiyi ahye so abo. Mehwie mʼabufuw agu wɔn so te sɛ nsuyiri.
11 Efereimu waponderezedwa, akulangidwa chifukwa chotsatira mafano.
Wɔhyɛ Efraim so, wotiatia ne so wɔ atemmu mu, wasi nʼadwene pi sɛ obedi ahoni akyi.
12 Ine ndili ngati njenjete kwa Efereimu, ngati chinthu chowola kwa anthu a ku Yuda.
Mɛyɛ sɛ nwewee ama Efraim na mayɛ Yudafo sɛ dua a aporɔw.
13 “Efereimu ataona nthenda yake, ndi Yuda ataona zilonda zake, pamenepo Efereimu anatembenukira kwa Asiriya, ndipo anawatumizira mfumu yayikulu kudzawathandiza. Koma mfumuyo singathe kukuchizani, singathe kuchiritsa mabala anu.
“Bere a Efraim huu ne yare, na Yuda nso huu nʼakuru no, Efraim de nʼani kyerɛɛ Asiria. Ɔsoma kɔɔ ɔhenkɛse no hɔ kɔpɛɛ mmoa. Nanso wantumi ansa no yare, na akuru no nso anwuwu.
14 Pakuti Ine ndidzakhala ngati mkango kwa Efereimu. Ngati mkango wamphamvu kwa Yuda. Ndidzawakhadzula nʼkuchokapo; ndidzawatenga ndipo palibe amene adzawalanditse.
Enti mɛyɛ sɛ gyata ama Efraim na mayɛ sɛ gyata hoɔdenfo ama Yuda. Mɛtetew wɔn mu nketenkete, na makɔ; Mɛsoa wɔn akɔ, na obiara rentumi nnye wɔn.
15 Ndipo ndidzabwerera ku malo anga mpaka anthu anga atavomereza kulakwa kwawo. Ndipo iwo adzafunafuna nkhope yanga; mʼmasautso awo adzandifunitsitsa Ine.”
Afei mɛsan akɔ me nkyi kosi sɛ wobenya ahonu. Na wɔbɛhwehwɛ mʼakyi kwan; wɔn awerɛhow mu, wɔbɛhwehwɛ me anibere so.”

< Hoseya 5 >