< Hoseya 5 >

1 “Ansembe inu, imvani izi! Inu Aisraeli, tcherani khutu! Inu nyumba yaufumu, mvetserani! Chiweruzo ichi ndi chotsutsa inu: Inu munali ngati msampha ku Mizipa, munali ngati ukonde woyalidwa pa phiri la Tabori.
Écoutez ceci, sacrificateurs; et sois attentive, maison d’Israël, et prête l’oreille, maison du roi, car c’est contre vous qu’est le jugement; car vous avez été un piège à Mitspa, et un filet étendu sur le Thabor.
2 Owukira azama mʼmoyo wakupha, Ine ndidzawalanga onsewo.
Ils se sont enfoncés dans la corruption de l’apostasie, et moi, je les châtierai tous.
3 Ndimadziwa zonse za Efereimu; Aisraeli ndi osabisika kwa Ine. Efereimu wayamba tsopano kuchita zachiwerewere; Israeli wadziyipitsa.
Je connais Éphraïm, et Israël ne m’est point caché; car maintenant, Éphraïm, tu as commis la fornication; Israël s’est souillé.
4 “Ntchito zawo siziwalola kubwerera kwa Mulungu wawo. Mʼmitima mwawo muli mzimu wachiwerewere; Iwo sadziwa Yehova.
Leurs méfaits ne leur permettent pas de retourner à leur Dieu; car l’esprit de fornication est au milieu d’eux et ils ne connaissent pas l’Éternel.
5 Kudzikuza kwa Israeli kwakhala umboni womutsutsa; Aisraeli, ngakhale Aefereimu, anagwa mʼmachimo awo; Yudanso anagwa nawo pamodzi.
Et l’orgueil d’Israël témoigne en face contre lui; et Israël et Éphraïm tomberont par leur iniquité; Juda aussi tombera avec eux.
6 Pamene adzapita ndi nkhosa zawo ndi ngʼombe zawo kukapereka nsembe kwa Yehova, iwo sadzamupeza; Iye wawachokera.
Avec leurs brebis et avec leurs bœufs, ils iront pour chercher l’Éternel, mais ils ne le trouveront pas: il s’est retiré d’eux.
7 Iwo ndi osakhulupirika kwa Yehova; amabereka ana amʼchigololo ndipo chikondwerero chawo cha mwezi watsopano chidzawawononga pamodzi ndi minda yawo.
Ils ont agi perfidement envers l’Éternel, car ils ont engendré des fils étrangers: maintenant, un mois les dévorera avec leurs biens.
8 “Womba lipenga mu Gibeya, liza mbetete mu Rama. Fuwulani mfuwu wankhondo mu Beti-Aveni; iwe Benjamini tsogolera.
Sonnez du cor en Guibha, de la trompette à Rama. Criez dans Beth-Aven: Derrière toi, Benjamin!
9 Efereimu adzasanduka bwinja pa tsiku la chilango. Ine ndikulengeza zomwe zidzachitikadi pakati pa mafuko a Israeli.
Éphraïm sera une désolation au jour du châtiment: je fais savoir parmi les tribus d’Israël une chose certaine.
10 Atsogoleri a Yuda ali ngati anthu amene amasuntha miyala ya mʼmalire. Ndidzawakhutulira ukali wanga ngati madzi a chigumula.
Les princes de Juda sont comme ceux qui reculent les bornes: je répandrai sur eux ma fureur comme de l’eau.
11 Efereimu waponderezedwa, akulangidwa chifukwa chotsatira mafano.
Éphraïm est opprimé, brisé par le jugement, parce que, selon sa propre volonté, il est allé après le commandement [de l’homme];
12 Ine ndili ngati njenjete kwa Efereimu, ngati chinthu chowola kwa anthu a ku Yuda.
et moi, je serai comme une teigne pour Éphraïm, et comme de la vermoulure pour la maison de Juda.
13 “Efereimu ataona nthenda yake, ndi Yuda ataona zilonda zake, pamenepo Efereimu anatembenukira kwa Asiriya, ndipo anawatumizira mfumu yayikulu kudzawathandiza. Koma mfumuyo singathe kukuchizani, singathe kuchiritsa mabala anu.
Et Éphraïm a vu sa maladie, et Juda, sa plaie; et Éphraïm s’en est allé en Assyrie et a envoyé vers le roi Jareb; mais lui n’a pu vous guérir, et ne vous a pas ôté votre plaie.
14 Pakuti Ine ndidzakhala ngati mkango kwa Efereimu. Ngati mkango wamphamvu kwa Yuda. Ndidzawakhadzula nʼkuchokapo; ndidzawatenga ndipo palibe amene adzawalanditse.
Car je serai comme un lion à Éphraïm, et comme un jeune lion à la maison de Juda: moi, moi, je déchirerai, et je m’en irai; j’emporterai, et il n’y aura personne qui délivre!
15 Ndipo ndidzabwerera ku malo anga mpaka anthu anga atavomereza kulakwa kwawo. Ndipo iwo adzafunafuna nkhope yanga; mʼmasautso awo adzandifunitsitsa Ine.”
Je m’en irai, je retournerai en mon lieu, jusqu’à ce qu’ils se reconnaissent coupables et recherchent ma face. Dans leur détresse, ils me chercheront dès le matin.

< Hoseya 5 >