< Hoseya 5 >

1 “Ansembe inu, imvani izi! Inu Aisraeli, tcherani khutu! Inu nyumba yaufumu, mvetserani! Chiweruzo ichi ndi chotsutsa inu: Inu munali ngati msampha ku Mizipa, munali ngati ukonde woyalidwa pa phiri la Tabori.
Hear ye this, O priests, and hearken, O ye house of Israel, and give ear, O house of the king: for there is a judgment against you, because you have been a snare to them whom you should have watched over, and a net spread upon Thabor.
2 Owukira azama mʼmoyo wakupha, Ine ndidzawalanga onsewo.
And you have turned aside victims into the depth: and I am, the teacher of them all.
3 Ndimadziwa zonse za Efereimu; Aisraeli ndi osabisika kwa Ine. Efereimu wayamba tsopano kuchita zachiwerewere; Israeli wadziyipitsa.
I know Ephraim, and Israel is not hid from me: for now Ephraim hath committed fornication, Israel is defiled.
4 “Ntchito zawo siziwalola kubwerera kwa Mulungu wawo. Mʼmitima mwawo muli mzimu wachiwerewere; Iwo sadziwa Yehova.
They will not set their thoughts to return to their God: for the spirit of fornication is in the midst of them, and they have not known the Lord.
5 Kudzikuza kwa Israeli kwakhala umboni womutsutsa; Aisraeli, ngakhale Aefereimu, anagwa mʼmachimo awo; Yudanso anagwa nawo pamodzi.
And the pride of Israel shall answer in his face: and Israel and Ephraim shall fall in their iniquity, Juda also shall fall with them.
6 Pamene adzapita ndi nkhosa zawo ndi ngʼombe zawo kukapereka nsembe kwa Yehova, iwo sadzamupeza; Iye wawachokera.
With their flocks, and with their herds, they shall go to seek the Lord, and shall not find him: he is withdrawn from them.
7 Iwo ndi osakhulupirika kwa Yehova; amabereka ana amʼchigololo ndipo chikondwerero chawo cha mwezi watsopano chidzawawononga pamodzi ndi minda yawo.
They have transgressed against the Lord, for they have begotten children that are strangers: now shall a month devour them with their portions.
8 “Womba lipenga mu Gibeya, liza mbetete mu Rama. Fuwulani mfuwu wankhondo mu Beti-Aveni; iwe Benjamini tsogolera.
Blow ye the cornet in Gabaa, the trumpet in Rama: howl ye in Bethaven, behind thy back, O Benjamin.
9 Efereimu adzasanduka bwinja pa tsiku la chilango. Ine ndikulengeza zomwe zidzachitikadi pakati pa mafuko a Israeli.
Ephraim shall be in desolation in the day of rebuke: among the tribes of Israel I have shewn that which shall surely be.
10 Atsogoleri a Yuda ali ngati anthu amene amasuntha miyala ya mʼmalire. Ndidzawakhutulira ukali wanga ngati madzi a chigumula.
The princes of Juda are become as they that take up the bound: I will pour out my wrath upon them like water.
11 Efereimu waponderezedwa, akulangidwa chifukwa chotsatira mafano.
Ephraim is under oppression, and broken in judgment: because he began to go after filthiness.
12 Ine ndili ngati njenjete kwa Efereimu, ngati chinthu chowola kwa anthu a ku Yuda.
And I will be like a moth to Ephraim: and like rottenness to the house of Juda.
13 “Efereimu ataona nthenda yake, ndi Yuda ataona zilonda zake, pamenepo Efereimu anatembenukira kwa Asiriya, ndipo anawatumizira mfumu yayikulu kudzawathandiza. Koma mfumuyo singathe kukuchizani, singathe kuchiritsa mabala anu.
And Ephraim saw his sickness, and Juda his band: and Ephraim went to the Assyrian, and sent to the avenging king: and he shall not be able to heal you, neither shall he be able to take off the band from you.
14 Pakuti Ine ndidzakhala ngati mkango kwa Efereimu. Ngati mkango wamphamvu kwa Yuda. Ndidzawakhadzula nʼkuchokapo; ndidzawatenga ndipo palibe amene adzawalanditse.
For I will be like a lioness to Ephraim, and like a lion’s whelp to the house of Juda: I, I will catch, and go: I will take away, and there is none that can rescue.
15 Ndipo ndidzabwerera ku malo anga mpaka anthu anga atavomereza kulakwa kwawo. Ndipo iwo adzafunafuna nkhope yanga; mʼmasautso awo adzandifunitsitsa Ine.”
I will go and return to my place: until you are consumed, and seek my face.

< Hoseya 5 >