< Hoseya 5 >
1 “Ansembe inu, imvani izi! Inu Aisraeli, tcherani khutu! Inu nyumba yaufumu, mvetserani! Chiweruzo ichi ndi chotsutsa inu: Inu munali ngati msampha ku Mizipa, munali ngati ukonde woyalidwa pa phiri la Tabori.
Slyštež to, ó kněží, a pozorujte, dome Izraelský, i dome královský, poslouchejte, nebo proti vám soud tento jest, proto že jste osídlo v Masfa, a sítka rozestřená na vrchu Tábor.
2 Owukira azama mʼmoyo wakupha, Ine ndidzawalanga onsewo.
Nýbrž k zabíjení uchylujíce se, připadají k zemi, ale já ztresci každého z nich.
3 Ndimadziwa zonse za Efereimu; Aisraeli ndi osabisika kwa Ine. Efereimu wayamba tsopano kuchita zachiwerewere; Israeli wadziyipitsa.
Známť já Efraima, a Izrael není ukryt přede mnou; nebo nyní smilníš, Efraime, poškvrňuje se Izrael.
4 “Ntchito zawo siziwalola kubwerera kwa Mulungu wawo. Mʼmitima mwawo muli mzimu wachiwerewere; Iwo sadziwa Yehova.
Nemají se k tomu, aby se obrátili k Bohu svému, proto že duch smilství mezi nimi jest, Hospodina pak znáti nechtějí,
5 Kudzikuza kwa Israeli kwakhala umboni womutsutsa; Aisraeli, ngakhale Aefereimu, anagwa mʼmachimo awo; Yudanso anagwa nawo pamodzi.
Tak že hrdost Izraelova svědčí vůči proti němu; protož Izrael i Efraim padnou pro nepravost svou, padne také i Juda s nimi.
6 Pamene adzapita ndi nkhosa zawo ndi ngʼombe zawo kukapereka nsembe kwa Yehova, iwo sadzamupeza; Iye wawachokera.
S stády bravů a skotů svých půjdou hledati Hospodina, však nenaleznou; vzdáliltě se od nich.
7 Iwo ndi osakhulupirika kwa Yehova; amabereka ana amʼchigololo ndipo chikondwerero chawo cha mwezi watsopano chidzawawononga pamodzi ndi minda yawo.
Hospodinu se zpronevěřili, nebo syny cizí zplodili; jižť je zžíře měsíc i s jměním jejich.
8 “Womba lipenga mu Gibeya, liza mbetete mu Rama. Fuwulani mfuwu wankhondo mu Beti-Aveni; iwe Benjamini tsogolera.
Trubte trubou v Gabaa, a na pozoun v Ráma; křičte v Betaven: Po tobě, ó Beniamine.
9 Efereimu adzasanduka bwinja pa tsiku la chilango. Ine ndikulengeza zomwe zidzachitikadi pakati pa mafuko a Israeli.
Efraim zpuštěn bude v den kázně, v němž po pokoleních Izraelských uvedu v známost pravdu.
10 Atsogoleri a Yuda ali ngati anthu amene amasuntha miyala ya mʼmalire. Ndidzawakhutulira ukali wanga ngati madzi a chigumula.
Knížata Judská jsou podobná těm, kteříž přenášejí mezník; vyleji na ně jako vodu prchlivost svou.
11 Efereimu waponderezedwa, akulangidwa chifukwa chotsatira mafano.
Utištěn jest Efraim, potřín soudem, však sobě libuje choditi za rozkazem.
12 Ine ndili ngati njenjete kwa Efereimu, ngati chinthu chowola kwa anthu a ku Yuda.
Protož i já byl jsem jako mol Efraimovi, a jako hnis domu Judovu.
13 “Efereimu ataona nthenda yake, ndi Yuda ataona zilonda zake, pamenepo Efereimu anatembenukira kwa Asiriya, ndipo anawatumizira mfumu yayikulu kudzawathandiza. Koma mfumuyo singathe kukuchizani, singathe kuchiritsa mabala anu.
Pročež vida Efraim neduh svůj, a Juda nežit svůj, utekl se Efraim k Assurovi, a poslal k králi, kterýž by se o něj zasadil. Ale on nebude moci zhojiti vás, ani uzdraviti vás od nežitů.
14 Pakuti Ine ndidzakhala ngati mkango kwa Efereimu. Ngati mkango wamphamvu kwa Yuda. Ndidzawakhadzula nʼkuchokapo; ndidzawatenga ndipo palibe amene adzawalanditse.
Nebo já jsem jako lítý lev Efraimovi, a jako lvíče domu Judovu; já, já uchvátím a ujdu, vezmu, a žádný nevytrhne.
15 Ndipo ndidzabwerera ku malo anga mpaka anthu anga atavomereza kulakwa kwawo. Ndipo iwo adzafunafuna nkhope yanga; mʼmasautso awo adzandifunitsitsa Ine.”
Odejda, navrátím se na místo své, až se vinni dadí, a hledati budou tváři mé.