< Hoseya 4 >
1 Inu Aisraeli, imvani mawu a Yehova, chifukwa Yehova ali ndi mlandu ndi inu amene mumakhala mʼdzikoli: “Mʼdziko mwanu mulibe kukhulupirika, mulibe chikondi mulibe kulabadira za Mulungu.
Аскултаць кувынтул Домнулуй, копиий луй Исраел, кэч Домнул аре о жудекатэ ку локуиторий цэрий, пентру кэ ну есте адевэр, ну есте ындураре, ну есте куноштинцэ де Думнезеу ын царэ:
2 Muli kutemberera kokha, kunama ndi kupha. Kuba ndi kuchita chigololo; machimo achita kunyanya ndipo akungokhalira kuphana.
„Фиекаре журэ стрымб ши минте, учиде, фурэ ши прякурвеште, нэпэстуеште ши фаче оморурь дупэ оморурь,
3 Chifukwa chake dziko likulira ndipo onse amene amakhalamo akuvutika; zirombo zakuthengo ndi mbalame zamumlengalenga ndiponso nsomba zamʼnyanja zikufa.
де ачея, цара се ва жели, тоць чей че о локуеск вор тынжи ымпреунэ ку фяреле кымпулуй ши пэсэриле черулуй; кяр ши пештий мэрий вор пери.
4 “Koma wina asapeze mnzake chifukwa, wina aliyense asayimbe mlandu mnzake, pakuti anthu ako ali ngati anthu amene amayimba mlandu wansembe.
Дар нимень сэ ну черте пе алтул, нимень сэ ну мустре пе алтул, кэч попорул тэу есте ка чей че се чартэ ку преоций.
5 Mumapunthwa usana ndi usiku ndipo aneneri amapunthwa nanu pamodzi. Choncho ndidzawononga amayi anu.
Те вей потикни зиуа, пророкул се ва потикни ши ел ымпреунэ ку тине ноаптя ши пе мама та о вой нимичи.
6 Anthu anga akuwonongeka chifukwa chosadziwa. “Pakuti mwakana kudziwa, Inenso ndidzakukanani monga ansembe anga; chifukwa mwayiwala lamulo la Mulungu wanu, Inenso ndidzayiwala ana anu.
Попорул Меу пере дин липсэ де куноштинцэ. Фииндкэ ай лепэдат куноштинца, ши Еу те вой лепэда ши ну-Мь вей май фи преот. Фииндкэ ай уйтат Леӂя Думнезеулуй тэу, вой уйта ши Еу пе копиий тэй!
7 Ansembe ankati akachuluka iwo ankandichimwiranso kwambiri; iwo anasinthanitsa ulemerero wawo ndi chinthu china chonyansa.
Ку кыт с-ау ынмулцит, ку атыт ау пэкэтуит ымпотрива Мя. Де ачея, ле вой префаче слава ын окарэ.
8 Amalemererapo pa machimo a anthu anga ndipo amafunitsitsa kuti anthuwo azipitiriza kuchimwa.
Ей се хрэнеск дин жертфеле пентру пэкателе попорулуй Меу ши сунт лакомь де нелеӂюириле луй.
9 Ndipo zidzakhala motere: zochitikira anthu ena, zidzachitikiranso ansembe. Ndidzawalanga onsewo chifukwa cha njira zawo, ndidzawabwezera chifukwa cha machitidwe awo.
Дар ши преотулуй и се ва ынтымпла ка ши попорулуй; ыл вой педепси дупэ умблетеле луй ши-л вой рэсплэти дупэ фаптеле луй.
10 “Iwo azidzadya koma sadzakhuta; azidzachita zachiwerewere koma sadzachulukana, chifukwa anasiya Yehova kuti adzipereke
Вор мынка ши тот ну се вор сэтура, вор курви ши тот ну се вор ынмулци, пентру кэ ау пэрэсит пе Домнул ши порунчиле Луй.
11 ku zachiwerewere, ku vinyo wakale ndi watsopano, zimene zimachotsa nzeru zomvetsa zinthu
Курвия, винул ши мустул яу минциле омулуй.
12 za anthu anga. Anthu anga amapempha nzeru ku fano lamtengo ndipo ndodo yawo yamtengo imawayankha. Mzimu wachiwerewere umawasocheretsa; iwo sakukhulupirika kwa Mulungu wawo.
Попорул Меу ышь ынтрябэ лемнул луй ши тоягул луй ый пророчеште, кэч духул курвей ый дуче ын рэтэчире ши сунт некрединчошь Думнезеулуй лор.
13 Amapereka nsembe pamwamba pa mapiri ndi kufukiza lubani pa zitunda, pa tsinde pa mtengo wa thundu, mnjale ndi mkundi, pamene pali mthunzi wabwino. Nʼchifukwa chake ana anu aakazi akuchita zachiwerewere ndipo akazi a ana anu akuchita zigololo.
Адук жертфе пе вырфул мунцилор, ард тэмые пе дялурь, суб стежарь, плопь ши теребинць, а кэрор умбрэ есте плэкутэ. Де ачея, фетеле воастре курвеск ши нурориле воастре сунт прякурве.
14 “Ine sindidzalanga ana anu aakazi pamene iwo adzachita zachiwerewere, kapena akazi a ana anu pamene adzachita zigololo. Paja inu nomwe amunanu mumayenda ndi akazi achiwerewere, ndipo mumapereka nsembe pamodzi ndi akazi achiwerewere a ku malo opembedzerako. Anthu amene alibe nzeru adzawonongeka ndithu!
Ну пот педепси пе фетеле воастре пентру кэ сунт курве, нич пе нурориле воастре пентру кэ сунт прякурве, кэч ей ыншишь се дук ла о парте ку ниште курве ши жертфеск ымпреунэ ку десфрынателе дин темпле. Попорул фэрэ минте аляргэ спре пеире.
15 “Ngakhale umachita chigololo, iwe Israeli, Yuda asapezeke ndi mlandu wotere. “Usapite ku Giligala. Usapite ku Beti-Aveni. Ndipo usalumbire kuti, ‘Pali Yehova wamoyo!’
Дакэ ту курвешть, Исраеле, мэкар Иуда сэ ну се факэ виноват. Ну вэ дучець мэкар ла Гилгал, ну вэ суиць ла Бет-Авен ши ну жураць зикынд: ‘Виу есте Домнул!’
16 Aisraeli ndi nkhutukumve, ngosamva ngati ana angʼombe. Kodi Yehova angathe kuwaweta bwanji ngati ana ankhosa pa msipu wabwino?
Пентру кэ Исраел дэ дин пичоаре ка о мынзатэ неымблынзитэ, ши сэ-л май паскэ Домнул акум ка пе ун мел ын имашурь ынтинсе!
17 Efereimu waphathana ndi mafano; mulekeni!
Ефраим с-а липит де идоль: ласэ-л ын паче!
18 Ngakhale pamene zakumwa zawo zatha, amapitiriza kuchita zachiwerewere; atsogoleri awo amakonda kwambiri njira zawo zochititsa manyazi.
Абя ау ынчетат сэ бя ши се дедау ла курвие; кырмуиторий лор сунт лакомь, да, сунт лакомь дупэ рушине!
19 Adzachotsedwa ndi kamvuluvulu ndipo adzachita manyazi chifukwa cha nsembe zawo.
Вынтул ый ва стрынӂе ку арипиле луй ши вор фи даць де рушине ку алтареле лор!