< Hoseya 4 >
1 Inu Aisraeli, imvani mawu a Yehova, chifukwa Yehova ali ndi mlandu ndi inu amene mumakhala mʼdzikoli: “Mʼdziko mwanu mulibe kukhulupirika, mulibe chikondi mulibe kulabadira za Mulungu.
Écoutez la parole du Seigneur, fils d’Israël, parce que voici venir le jugement du Seigneur avec les habitants de la terre; car il n’y a pas de vérité, et il n’y a pas de miséricorde, et il n’y a pas de science de Dieu sur la terre.
2 Muli kutemberera kokha, kunama ndi kupha. Kuba ndi kuchita chigololo; machimo achita kunyanya ndipo akungokhalira kuphana.
L’imprécation, et le mensonge, et l’homicide, et le vol, et l’adultère, ont inondé la terre, et le sang s’est mêlé au sang.
3 Chifukwa chake dziko likulira ndipo onse amene amakhalamo akuvutika; zirombo zakuthengo ndi mbalame zamumlengalenga ndiponso nsomba zamʼnyanja zikufa.
À cause de cela, la terre sera dans le deuil, et quiconque l’habite languira avec la bête de la campagne, et avec l’oiseau du ciel; et même les poissons de la mer seront enveloppés dans cette ruine.
4 “Koma wina asapeze mnzake chifukwa, wina aliyense asayimbe mlandu mnzake, pakuti anthu ako ali ngati anthu amene amayimba mlandu wansembe.
Mais cependant que personne ne juge, et qu’aucun homme ne soit repris; car ton peuple est comme ceux qui contredisent le prêtre.
5 Mumapunthwa usana ndi usiku ndipo aneneri amapunthwa nanu pamodzi. Choncho ndidzawononga amayi anu.
Et tu succomberas aujourd’hui, et succombera aussi le prophète avec toi: la nuit j’ai réduit ta mère au silence.
6 Anthu anga akuwonongeka chifukwa chosadziwa. “Pakuti mwakana kudziwa, Inenso ndidzakukanani monga ansembe anga; chifukwa mwayiwala lamulo la Mulungu wanu, Inenso ndidzayiwala ana anu.
Mon peuple s’est tu à cause qu’il n’a pas eu la science; parce que toi, tu as rejeté la science, je te rejetterai, afin que tu n’exerces pas le sacerdoce pour moi; et comme tu as oublié la loi de ton Dieu, j’oublierai tes enfants, moi aussi.
7 Ansembe ankati akachuluka iwo ankandichimwiranso kwambiri; iwo anasinthanitsa ulemerero wawo ndi chinthu china chonyansa.
À proportion de leur multitude, ils ont péché contre moi; je changerai leur gloire en ignominie.
8 Amalemererapo pa machimo a anthu anga ndipo amafunitsitsa kuti anthuwo azipitiriza kuchimwa.
Ils se nourriront des péchés de mon peuple, et ils encourageront leurs âmes dans leurs iniquités.
9 Ndipo zidzakhala motere: zochitikira anthu ena, zidzachitikiranso ansembe. Ndidzawalanga onsewo chifukwa cha njira zawo, ndidzawabwezera chifukwa cha machitidwe awo.
Et comme sera le peuple, ainsi sera le prêtre; et je visiterai sur lui sa voie, et je lui rendrai selon ses pensées.
10 “Iwo azidzadya koma sadzakhuta; azidzachita zachiwerewere koma sadzachulukana, chifukwa anasiya Yehova kuti adzipereke
Et ils mangeront, et ils ne seront pas rassasiés; ils ont forniqué, et ils n’ont pas cessé, parce qu’ils ont abandonné le Seigneur en ne gardant point sa loi.
11 ku zachiwerewere, ku vinyo wakale ndi watsopano, zimene zimachotsa nzeru zomvetsa zinthu
La fornication, et le vin, et l’ivresse emportent le cœur.
12 za anthu anga. Anthu anga amapempha nzeru ku fano lamtengo ndipo ndodo yawo yamtengo imawayankha. Mzimu wachiwerewere umawasocheretsa; iwo sakukhulupirika kwa Mulungu wawo.
Mon peuple a interrogé son bois, et son bâton lui a annoncé l’avenir, car l’esprit de fornication les a déçus; et ils ont forniqué en se séparant de leur Dieu.
13 Amapereka nsembe pamwamba pa mapiri ndi kufukiza lubani pa zitunda, pa tsinde pa mtengo wa thundu, mnjale ndi mkundi, pamene pali mthunzi wabwino. Nʼchifukwa chake ana anu aakazi akuchita zachiwerewere ndipo akazi a ana anu akuchita zigololo.
Sur les sommets des montagnes ils sacrifiaient; et sur les collines ils brûlaient de l’encens; sous un chêne, et un peuplier, et un térébinthe, parce que bonne en était l’ombre; pour cela forniqueront vos filles, et vos femmes seront adultères.
14 “Ine sindidzalanga ana anu aakazi pamene iwo adzachita zachiwerewere, kapena akazi a ana anu pamene adzachita zigololo. Paja inu nomwe amunanu mumayenda ndi akazi achiwerewere, ndipo mumapereka nsembe pamodzi ndi akazi achiwerewere a ku malo opembedzerako. Anthu amene alibe nzeru adzawonongeka ndithu!
Je ne punirai pas vos filles lorsqu’elles auront forniqué, ni vos femmes lorsqu’elles auront commis l’adultère; puisqu’eux mêmes vivaient avec des femmes de mauvaise vie, et qu’avec des efféminés ils sacrifiaient, et qu’un peuple non intelligent sera châtié.
15 “Ngakhale umachita chigololo, iwe Israeli, Yuda asapezeke ndi mlandu wotere. “Usapite ku Giligala. Usapite ku Beti-Aveni. Ndipo usalumbire kuti, ‘Pali Yehova wamoyo!’
Si tu forniques, toi, Israël, que Juda au moins ne pèche point, et n’entre pas à Galgala, et ne monte pas à Bethaven, et ne jure pas: Le Seigneur vit.
16 Aisraeli ndi nkhutukumve, ngosamva ngati ana angʼombe. Kodi Yehova angathe kuwaweta bwanji ngati ana ankhosa pa msipu wabwino?
Puisque, comme une génisse bondissante, Israël s’est détourné, maintenant le Seigneur les fera paître comme un agneau dans une vaste campagne.
17 Efereimu waphathana ndi mafano; mulekeni!
Ephraïm est attaché aux idoles; abandonne-le.
18 Ngakhale pamene zakumwa zawo zatha, amapitiriza kuchita zachiwerewere; atsogoleri awo amakonda kwambiri njira zawo zochititsa manyazi.
Leur festin est séparé du vôtre; ils ont forniqué par la fornication; ses protecteurs ont aimé à le couvrir d’ignominie.
19 Adzachotsedwa ndi kamvuluvulu ndipo adzachita manyazi chifukwa cha nsembe zawo.
Un vent l’a enveloppé dans ses ailes, et ils seront confondus par leurs sacrifices.