< Hoseya 4 >

1 Inu Aisraeli, imvani mawu a Yehova, chifukwa Yehova ali ndi mlandu ndi inu amene mumakhala mʼdzikoli: “Mʼdziko mwanu mulibe kukhulupirika, mulibe chikondi mulibe kulabadira za Mulungu.
Écoutez la parole de l'Éternel, enfants d'Israël! Car l'Éternel a un procès avec les habitants du pays, parce qu'il n'y a ni vérité, ni bonté, ni connaissance de Dieu, dans le pays.
2 Muli kutemberera kokha, kunama ndi kupha. Kuba ndi kuchita chigololo; machimo achita kunyanya ndipo akungokhalira kuphana.
Il n'y a que parjures et mensonges; meurtres, vols et adultères; on use de violence, et un meurtre touche l'autre.
3 Chifukwa chake dziko likulira ndipo onse amene amakhalamo akuvutika; zirombo zakuthengo ndi mbalame zamumlengalenga ndiponso nsomba zamʼnyanja zikufa.
C'est pourquoi le pays sera dans le deuil, et tous ses habitants dans la langueur, avec les bêtes des champs et les oiseaux des cieux; même les poissons de la mer périront.
4 “Koma wina asapeze mnzake chifukwa, wina aliyense asayimbe mlandu mnzake, pakuti anthu ako ali ngati anthu amene amayimba mlandu wansembe.
Mais que nul ne conteste, et que nul ne reprenne! Car ton peuple est comme ceux qui disputent avec le sacrificateur.
5 Mumapunthwa usana ndi usiku ndipo aneneri amapunthwa nanu pamodzi. Choncho ndidzawononga amayi anu.
Tu tomberas de jour; le prophète aussi tombera avec toi de nuit; et je détruirai ta mère.
6 Anthu anga akuwonongeka chifukwa chosadziwa. “Pakuti mwakana kudziwa, Inenso ndidzakukanani monga ansembe anga; chifukwa mwayiwala lamulo la Mulungu wanu, Inenso ndidzayiwala ana anu.
Mon peuple est détruit, faute de connaissance. Puisque toi tu as rejeté la connaissance, je te rejetterai, afin que tu n'exerces plus devant moi le sacerdoce; puisque tu as oublié la loi de ton Dieu, moi aussi j'oublierai tes enfants.
7 Ansembe ankati akachuluka iwo ankandichimwiranso kwambiri; iwo anasinthanitsa ulemerero wawo ndi chinthu china chonyansa.
Plus ils se sont multipliés, plus ils ont péché contre moi: je changerai leur gloire en ignominie!
8 Amalemererapo pa machimo a anthu anga ndipo amafunitsitsa kuti anthuwo azipitiriza kuchimwa.
Ils se nourrissent des péchés de mon peuple; ils sont avides de ses iniquités.
9 Ndipo zidzakhala motere: zochitikira anthu ena, zidzachitikiranso ansembe. Ndidzawalanga onsewo chifukwa cha njira zawo, ndidzawabwezera chifukwa cha machitidwe awo.
Aussi il en sera du sacrificateur comme du peuple; je le punirai selon ses voies et lui rendrai selon ses œuvres.
10 “Iwo azidzadya koma sadzakhuta; azidzachita zachiwerewere koma sadzachulukana, chifukwa anasiya Yehova kuti adzipereke
Ils mangeront, et ne seront pas rassasiés; ils se prostitueront, et ne multiplieront pas. Car ils ont abandonné l'Éternel, pour ne pas observer sa loi.
11 ku zachiwerewere, ku vinyo wakale ndi watsopano, zimene zimachotsa nzeru zomvetsa zinthu
La fornication, le vin et le moût ôtent l'entendement.
12 za anthu anga. Anthu anga amapempha nzeru ku fano lamtengo ndipo ndodo yawo yamtengo imawayankha. Mzimu wachiwerewere umawasocheretsa; iwo sakukhulupirika kwa Mulungu wawo.
Mon peuple consulte son bois, et son bâton lui prophétise; car l'esprit de fornication égare, et ils se prostituent en abandonnant leur Dieu.
13 Amapereka nsembe pamwamba pa mapiri ndi kufukiza lubani pa zitunda, pa tsinde pa mtengo wa thundu, mnjale ndi mkundi, pamene pali mthunzi wabwino. Nʼchifukwa chake ana anu aakazi akuchita zachiwerewere ndipo akazi a ana anu akuchita zigololo.
Ils sacrifient sur le sommet des montagnes; sur les coteaux, ils font fumer le parfum; sous le chêne, le peuplier, le térébinthe, dont l'ombre est agréable. C'est pourquoi vos filles se prostituent, et vos belles-filles commettent adultère.
14 “Ine sindidzalanga ana anu aakazi pamene iwo adzachita zachiwerewere, kapena akazi a ana anu pamene adzachita zigololo. Paja inu nomwe amunanu mumayenda ndi akazi achiwerewere, ndipo mumapereka nsembe pamodzi ndi akazi achiwerewere a ku malo opembedzerako. Anthu amene alibe nzeru adzawonongeka ndithu!
Je ne punirai point vos filles parce qu'elles se prostituent, ni vos belles-filles parce qu'elles commettent adultère. Car eux-mêmes se retirent avec des prostituées, et sacrifient avec les femmes consacrées à l'impudicité; et le peuple sans intelligence court à sa ruine.
15 “Ngakhale umachita chigololo, iwe Israeli, Yuda asapezeke ndi mlandu wotere. “Usapite ku Giligala. Usapite ku Beti-Aveni. Ndipo usalumbire kuti, ‘Pali Yehova wamoyo!’
Si tu te prostitues, Israël, que Juda ne se rende pas coupable! N'entrez pas à Guilgal! Et ne montez point à Beth-Aven! Et ne jurez point: “L'Éternel est vivant! “
16 Aisraeli ndi nkhutukumve, ngosamva ngati ana angʼombe. Kodi Yehova angathe kuwaweta bwanji ngati ana ankhosa pa msipu wabwino?
Parce qu'Israël a été rebelle comme une génisse indomptée, maintenant l'Éternel les fera paître comme un agneau dans des lieux spacieux.
17 Efereimu waphathana ndi mafano; mulekeni!
Éphraïm s'est associé aux idoles: abandonne-le!
18 Ngakhale pamene zakumwa zawo zatha, amapitiriza kuchita zachiwerewere; atsogoleri awo amakonda kwambiri njira zawo zochititsa manyazi.
Ont-ils fini de boire, les voilà à la fornication. Les chefs d'Israël n'aiment que l'ignominie.
19 Adzachotsedwa ndi kamvuluvulu ndipo adzachita manyazi chifukwa cha nsembe zawo.
Le vent les attachera à ses ailes, et ils auront honte de leurs sacrifices.

< Hoseya 4 >