< Hoseya 4 >
1 Inu Aisraeli, imvani mawu a Yehova, chifukwa Yehova ali ndi mlandu ndi inu amene mumakhala mʼdzikoli: “Mʼdziko mwanu mulibe kukhulupirika, mulibe chikondi mulibe kulabadira za Mulungu.
Écoutez la parole de Yahvé, enfants d'Israël, car Yahvé a une charge contre les habitants du pays: « En effet, il n'y a pas de vérité, ni de bonté, ni la connaissance de Dieu dans le pays.
2 Muli kutemberera kokha, kunama ndi kupha. Kuba ndi kuchita chigololo; machimo achita kunyanya ndipo akungokhalira kuphana.
Il y a la malédiction, le mensonge, le meurtre, le vol et l'adultère; ils brisent les frontières, et les effusions de sang provoquent des effusions de sang.
3 Chifukwa chake dziko likulira ndipo onse amene amakhalamo akuvutika; zirombo zakuthengo ndi mbalame zamumlengalenga ndiponso nsomba zamʼnyanja zikufa.
C'est pourquoi le pays sera dans le deuil, et tous ceux qui l'habitent dépériront, avec tous les êtres vivants en elle, même les animaux des champs et les oiseaux du ciel; oui, les poissons de la mer meurent aussi.
4 “Koma wina asapeze mnzake chifukwa, wina aliyense asayimbe mlandu mnzake, pakuti anthu ako ali ngati anthu amene amayimba mlandu wansembe.
« Que personne ne porte plainte, que personne n'accuse; car ton peuple est comme ceux qui portent plainte contre un prêtre.
5 Mumapunthwa usana ndi usiku ndipo aneneri amapunthwa nanu pamodzi. Choncho ndidzawononga amayi anu.
Vous trébucherez le jour, et le prophète aussi trébuchera avec vous dans la nuit; et je détruirai ta mère.
6 Anthu anga akuwonongeka chifukwa chosadziwa. “Pakuti mwakana kudziwa, Inenso ndidzakukanani monga ansembe anga; chifukwa mwayiwala lamulo la Mulungu wanu, Inenso ndidzayiwala ana anu.
Mon peuple est détruit par manque de connaissance. Parce que vous avez rejeté la connaissance, je vous rejetterai aussi, pour que vous ne soyez pas un prêtre pour moi. Parce que vous avez oublié la loi de votre Dieu, J'oublierai aussi vos enfants.
7 Ansembe ankati akachuluka iwo ankandichimwiranso kwambiri; iwo anasinthanitsa ulemerero wawo ndi chinthu china chonyansa.
Comme ils se sont multipliés, ils ont péché contre moi. Je changerai leur gloire en honte.
8 Amalemererapo pa machimo a anthu anga ndipo amafunitsitsa kuti anthuwo azipitiriza kuchimwa.
Ils se nourrissent du péché de mon peuple, et ont mis leur cœur dans leur iniquité.
9 Ndipo zidzakhala motere: zochitikira anthu ena, zidzachitikiranso ansembe. Ndidzawalanga onsewo chifukwa cha njira zawo, ndidzawabwezera chifukwa cha machitidwe awo.
Il sera comme un peuple, comme un prêtre; et je les punirai pour leur conduite, et leur rendra la monnaie de leur pièce.
10 “Iwo azidzadya koma sadzakhuta; azidzachita zachiwerewere koma sadzachulukana, chifukwa anasiya Yehova kuti adzipereke
Ils mangeront, et n'auront pas assez. Ils joueront les prostituées, et n'augmenteront pas; parce qu'ils ont abandonné l'écoute de Yahvé.
11 ku zachiwerewere, ku vinyo wakale ndi watsopano, zimene zimachotsa nzeru zomvetsa zinthu
La prostitution, le vin et le vin nouveau enlèvent l'intelligence.
12 za anthu anga. Anthu anga amapempha nzeru ku fano lamtengo ndipo ndodo yawo yamtengo imawayankha. Mzimu wachiwerewere umawasocheretsa; iwo sakukhulupirika kwa Mulungu wawo.
Mon peuple consulte son idole de bois, et répondre à un bâton de bois. En effet, l'esprit de prostitution les a égarés, et ils ont été infidèles à leur Dieu.
13 Amapereka nsembe pamwamba pa mapiri ndi kufukiza lubani pa zitunda, pa tsinde pa mtengo wa thundu, mnjale ndi mkundi, pamene pali mthunzi wabwino. Nʼchifukwa chake ana anu aakazi akuchita zachiwerewere ndipo akazi a ana anu akuchita zigololo.
Ils sacrifient sur les sommets des montagnes, et brûlent de l'encens sur les collines, sous les chênes, les peupliers et les térébinthes, parce que sa teinte est bonne. C'est pourquoi vos filles jouent les prostituées, et vos épouses commettent l'adultère.
14 “Ine sindidzalanga ana anu aakazi pamene iwo adzachita zachiwerewere, kapena akazi a ana anu pamene adzachita zigololo. Paja inu nomwe amunanu mumayenda ndi akazi achiwerewere, ndipo mumapereka nsembe pamodzi ndi akazi achiwerewere a ku malo opembedzerako. Anthu amene alibe nzeru adzawonongeka ndithu!
Je ne punirai pas vos filles lorsqu'elles se prostituent, ni vos épouses quand elles commettent l'adultère; parce que les hommes fréquentent des prostituées, et ils sacrifient avec les prostituées du sanctuaire; ainsi les gens sans compréhension viendront à la ruine.
15 “Ngakhale umachita chigololo, iwe Israeli, Yuda asapezeke ndi mlandu wotere. “Usapite ku Giligala. Usapite ku Beti-Aveni. Ndipo usalumbire kuti, ‘Pali Yehova wamoyo!’
« Bien que toi, Israël, tu joues les prostituées, mais ne laissez pas Judah s'offenser; et ne venez pas à Gilgal, ni aller jusqu'à Beth Aven, ni de jurer: « Comme Yahvé vit ».
16 Aisraeli ndi nkhutukumve, ngosamva ngati ana angʼombe. Kodi Yehova angathe kuwaweta bwanji ngati ana ankhosa pa msipu wabwino?
Car Israël s'est montré extrêmement têtu, comme une génisse obstinée. Alors comment Yahvé les nourrira-t-il comme un agneau dans une prairie?
17 Efereimu waphathana ndi mafano; mulekeni!
Ephraïm est attaché aux idoles. Laissez-le tranquille!
18 Ngakhale pamene zakumwa zawo zatha, amapitiriza kuchita zachiwerewere; atsogoleri awo amakonda kwambiri njira zawo zochititsa manyazi.
Leur boisson est devenue aigre. Ils jouent continuellement la prostituée. Ses gouvernants aiment beaucoup leur manière honteuse.
19 Adzachotsedwa ndi kamvuluvulu ndipo adzachita manyazi chifukwa cha nsembe zawo.
Le vent l'a enveloppée dans ses ailes; et ils seront déçus à cause de leurs sacrifices.