< Hoseya 4 >

1 Inu Aisraeli, imvani mawu a Yehova, chifukwa Yehova ali ndi mlandu ndi inu amene mumakhala mʼdzikoli: “Mʼdziko mwanu mulibe kukhulupirika, mulibe chikondi mulibe kulabadira za Mulungu.
Winjuru wach Jehova Nyasaye, un jo-Israel, nikech Jehova Nyasaye nigi wach modonjonugo, un ji modak e piny: “Onge adiera, onge hera, bende udagi yie ni Nyasaye nitie e piny.
2 Muli kutemberera kokha, kunama ndi kupha. Kuba ndi kuchita chigololo; machimo achita kunyanya ndipo akungokhalira kuphana.
Nitie mana kwongʼ, miriambo kod nek, kuo gi chode; kendo giketho singruok duto, kendo chwero remo timore monwore.
3 Chifukwa chake dziko likulira ndipo onse amene amakhalamo akuvutika; zirombo zakuthengo ndi mbalame zamumlengalenga ndiponso nsomba zamʼnyanja zikufa.
Nikech ma, piny opongʼ gi kuyo kendo ji modak e iye dhero kendo tho; ondiegi manie thim gi winy mafuyo e kor polo gi rech manie nembe tho.
4 “Koma wina asapeze mnzake chifukwa, wina aliyense asayimbe mlandu mnzake, pakuti anthu ako ali ngati anthu amene amayimba mlandu wansembe.
“Kik ngʼato kel wach mar donjo, kik ngʼato donjne wadgi, nimar jou chalo mana ka joma donjo ni jadolo.
5 Mumapunthwa usana ndi usiku ndipo aneneri amapunthwa nanu pamodzi. Choncho ndidzawononga amayi anu.
Uchwanyoru odiechiengʼ gotieno to jonabi bende chwanyore mana kaka un. Omiyo abiro tieko minu.
6 Anthu anga akuwonongeka chifukwa chosadziwa. “Pakuti mwakana kudziwa, Inenso ndidzakukanani monga ansembe anga; chifukwa mwayiwala lamulo la Mulungu wanu, Inenso ndidzayiwala ana anu.
Joga itieko nikech chando ngʼeyo. “Nikech utamoru dwaro ngʼeyo, an bende adagiu kaka jodolona; nikech usejwangʼo chike mag Nyasachu, an bende anajwangʼ nyithindu.
7 Ansembe ankati akachuluka iwo ankandichimwiranso kwambiri; iwo anasinthanitsa ulemerero wawo ndi chinthu china chonyansa.
Kaka jodolo medore, e kaka gimedo timo richo e nyima; gisewilo duongʼ margi gi gima kelo wichkuot.
8 Amalemererapo pa machimo a anthu anga ndipo amafunitsitsa kuti anthuwo azipitiriza kuchimwa.
Giyiengʼ gi richo mag joga, bende gimor gi timbegi maricho.
9 Ndipo zidzakhala motere: zochitikira anthu ena, zidzachitikiranso ansembe. Ndidzawalanga onsewo chifukwa cha njira zawo, ndidzawabwezera chifukwa cha machitidwe awo.
Kendo obiro bet ni: Kaka ji chalo e kaka jodolo bende chalo. To abiro kumogi kuom yoregigo, kendo anachulgi machal gi timbegi.
10 “Iwo azidzadya koma sadzakhuta; azidzachita zachiwerewere koma sadzachulukana, chifukwa anasiya Yehova kuti adzipereke
“Gibiro chiemo to ok giniyiengʼ; gibiro chodo to ok gini nywolre, nikech giseweyo Jehova Nyasaye, mondo gichiwre
11 ku zachiwerewere, ku vinyo wakale ndi watsopano, zimene zimachotsa nzeru zomvetsa zinthu
ne chode, ne kongʼo machon kod kongʼo manyien, magolo winjo mar joga.
12 za anthu anga. Anthu anga amapempha nzeru ku fano lamtengo ndipo ndodo yawo yamtengo imawayankha. Mzimu wachiwerewere umawasocheretsa; iwo sakukhulupirika kwa Mulungu wawo.
Gipenjo wach kuom nyasaye molos gi bao kendo idwokogi gi yien mopa. Chuny mar chode terogi mabor; ok gin jo-adier ne Nyasachgi.
13 Amapereka nsembe pamwamba pa mapiri ndi kufukiza lubani pa zitunda, pa tsinde pa mtengo wa thundu, mnjale ndi mkundi, pamene pali mthunzi wabwino. Nʼchifukwa chake ana anu aakazi akuchita zachiwerewere ndipo akazi a ana anu akuchita zigololo.
Gitimo misango ewi gode maboyo kendo gitimo Sewni kuonde motingʼore gi malo, e tiend yiend ober, gi omburi kod yiende mamoko madongo dongo kendo boyo, kama otimo tipo maber. Emomiyo nyiu lokore ochode to mond yawuotu to donjo e chode.
14 “Ine sindidzalanga ana anu aakazi pamene iwo adzachita zachiwerewere, kapena akazi a ana anu pamene adzachita zigololo. Paja inu nomwe amunanu mumayenda ndi akazi achiwerewere, ndipo mumapereka nsembe pamodzi ndi akazi achiwerewere a ku malo opembedzerako. Anthu amene alibe nzeru adzawonongeka ndithu!
“Ok anakum nyiu ka gibedo ochode, kata mond yawuotu ka terore, nikech chwo giwegi ema dhi ir mon ma jochode, gi mon manie hekalu mar Baal. Joma onge ngʼeyo biro yudo chandruok!
15 “Ngakhale umachita chigololo, iwe Israeli, Yuda asapezeke ndi mlandu wotere. “Usapite ku Giligala. Usapite ku Beti-Aveni. Ndipo usalumbire kuti, ‘Pali Yehova wamoyo!’
“Yaye Israel, kata obedo ni utimo anjawo mar chode, kik umi Juda donj e timbego. “Kik udhi Gilgal; kik udhi Beth Aven. Kendo kik ukwongʼru kuwacho niya, ‘Akwongʼora gi nying Jehova Nyasaye mangima!’
16 Aisraeli ndi nkhutukumve, ngosamva ngati ana angʼombe. Kodi Yehova angathe kuwaweta bwanji ngati ana ankhosa pa msipu wabwino?
Jo-Israel wigi tek mana ka roya bwongʼ ma wiye tek. Ere kaka Jehova Nyasaye nyalo kwayogi e lek kaka ikwayo rombe e lek man-gi lum?
17 Efereimu waphathana ndi mafano; mulekeni!
Jo-Efraim oriwore gi nyiseche manono; weyeuru kamano!
18 Ngakhale pamene zakumwa zawo zatha, amapitiriza kuchita zachiwerewere; atsogoleri awo amakonda kwambiri njira zawo zochititsa manyazi.
Kata ka kong-gi orumo, to gidhi nyime gi timbegi mag chode; jotendgi ohero timbe makelo wichkuot.
19 Adzachotsedwa ndi kamvuluvulu ndipo adzachita manyazi chifukwa cha nsembe zawo.
Kalausi biro tingʼogi matergi mabor, kendo misenginigi nokelnegi wichkuot.”

< Hoseya 4 >