< Hoseya 3 >

1 Yehova anati kwa ine, “Pita kamukondenso mkazi wako, ngakhale ali pa chibwenzi ndi wina ndi kuti ndi wachigololo. Mukonde iyeyo monga momwe Yehova amakondera Aisraeli, ngakhale iwo amapita kukapembedza milungu ina ndi kukonda nsembe za keke zamphesa zowuma.”
Le hoe t’Iehovà amako; Akia irehe: Ikokò ty rakemba ikokoan-tsakeza’e, ie toe karapilo, manahake ty fikokoa’ Iehovà o ana’ Israeleo, ie mitolik’ aman-drahare ila’e vaho mpitea mofom-balòboke.
2 Motero ndinamukwatira popereka ndalama khumi ndi zisanu zasiliva, ndiponso mitanga isanu ndi iwiri ya barele.
Aa le viniliko ho ahiko re ami’ty volafoty folo-lim’amby naho ampemba omere raike naho tampa’e;
3 Kenaka ndinamuwuza mkaziyo kuti, “Ukhale nane masiku ambiri; usachitenso zachiwerewere kapena chigololo ndi munthu wina, ndipo ine ndidzakhala nawe.”
le hoe iraho ama’e, Himoneñe amako andro maro irehe; fa tsy hihisa ankarapiloañe ka, naho tsy hiharo amy t’indaty ila’e; le hoe izay ka izaho ama’o.
4 Pakuti Aisraeli adzakhala masiku ambiri opanda mfumu kapena kalonga, osapereka nsembe kapena kuyimika miyala yachipembedzo, wopanda efodi kapena fano.
Amy te himoneñe andro maro tsy amam-panjàka tsy aman-Talè, tsy aman-tsòroñe, tsy aman-tsamposampo, tsy aman’efode vaho tsy aman-terafeme o nte-Israeleo.
5 Pambuyo pake Aisraeli adzabwerera ndi kufunafuna Yehova Mulungu wawo ndi Davide mfumu yawo. Adzabwera kwa Yehova akunjenjemera ndipo adzalandira madalitso mʼmasiku awo otsiriza.
Ie modo izay, le himpoly o ana’ Israeleo, hipay Iehovà Andrianañahare’ iareo, naho i Davide mpanjaka’ iareo; vaho hañeveñe am’ Iehovà naho i fatariha’ey amo andro sehanga’eo.

< Hoseya 3 >