< Hoseya 3 >

1 Yehova anati kwa ine, “Pita kamukondenso mkazi wako, ngakhale ali pa chibwenzi ndi wina ndi kuti ndi wachigololo. Mukonde iyeyo monga momwe Yehova amakondera Aisraeli, ngakhale iwo amapita kukapembedza milungu ina ndi kukonda nsembe za keke zamphesa zowuma.”
L’Eternel me dit encore: "Va derechef, accorde ton amour à une femme qui est aimée d’un autre et coupable d’adultère, tout comme Dieu aime les enfants d’Israël tandis qu’ils se tournent, eux, vers des dieux étrangers et raffolent de gâteaux de raisin.
2 Motero ndinamukwatira popereka ndalama khumi ndi zisanu zasiliva, ndiponso mitanga isanu ndi iwiri ya barele.
Je m’acquis cette femme pour quinze pièces d’argent, un homer plus un létec d’orge.
3 Kenaka ndinamuwuza mkaziyo kuti, “Ukhale nane masiku ambiri; usachitenso zachiwerewere kapena chigololo ndi munthu wina, ndipo ine ndidzakhala nawe.”
Et je lui dis: "Tu me demeureras fidèle pendant de longs jours, sans te débaucher ni appartenir à aucun homme, de même en userai-je à ton égard."
4 Pakuti Aisraeli adzakhala masiku ambiri opanda mfumu kapena kalonga, osapereka nsembe kapena kuyimika miyala yachipembedzo, wopanda efodi kapena fano.
Car de longs jours, les enfants d’Israël demeureront isolés sans roi ni chef, sans sacrifice ni stèle, sans Ephod ni Pénates.
5 Pambuyo pake Aisraeli adzabwerera ndi kufunafuna Yehova Mulungu wawo ndi Davide mfumu yawo. Adzabwera kwa Yehova akunjenjemera ndipo adzalandira madalitso mʼmasiku awo otsiriza.
Après cela, les enfants d’Israël se remettront à rechercher l’Eternel, leur Dieu, et David, leur roi; ils accourront, le cœur ému, auprès de l’Eternel et de sa grâce, dans la suite des temps.

< Hoseya 3 >