< Hoseya 3 >

1 Yehova anati kwa ine, “Pita kamukondenso mkazi wako, ngakhale ali pa chibwenzi ndi wina ndi kuti ndi wachigololo. Mukonde iyeyo monga momwe Yehova amakondera Aisraeli, ngakhale iwo amapita kukapembedza milungu ina ndi kukonda nsembe za keke zamphesa zowuma.”
Og Herren sagde til mig: Gak endnu hen, elsk en Kvinde, som elskes af sin Ven og dog bedriver Hor; ligesom Herren elsker Israels Børn, og disse dog vende sig til fremmede Guder og elske Rosinkager.
2 Motero ndinamukwatira popereka ndalama khumi ndi zisanu zasiliva, ndiponso mitanga isanu ndi iwiri ya barele.
Og jeg købte mig hende for femten Sekel Sølv og en Homer Byg og en Lethek Byg.
3 Kenaka ndinamuwuza mkaziyo kuti, “Ukhale nane masiku ambiri; usachitenso zachiwerewere kapena chigololo ndi munthu wina, ndipo ine ndidzakhala nawe.”
Og jeg sagde til hende: I mange Dage skal du sidde hen for mig, ikke skal du bedrive Hor og ikke tilhøre nogen Mand; saaledes vil ogsaa jeg holde mig over for dig.
4 Pakuti Aisraeli adzakhala masiku ambiri opanda mfumu kapena kalonga, osapereka nsembe kapena kuyimika miyala yachipembedzo, wopanda efodi kapena fano.
Thi i mange Dage skulle Israels Børn sidde hen uden Konge og uden Fyrste og uden Offer og uden Billedstøtte og uden præstelig Livkjortel og Husguder.
5 Pambuyo pake Aisraeli adzabwerera ndi kufunafuna Yehova Mulungu wawo ndi Davide mfumu yawo. Adzabwera kwa Yehova akunjenjemera ndipo adzalandira madalitso mʼmasiku awo otsiriza.
Derefter skulle Israels Børn vende om og søge Herren, deres Gud, og David, deres Konge, og med Frygt skulle de komme til Herren og til hans gode Gaver i de sidste Dage.

< Hoseya 3 >