< Hoseya 3 >
1 Yehova anati kwa ine, “Pita kamukondenso mkazi wako, ngakhale ali pa chibwenzi ndi wina ndi kuti ndi wachigololo. Mukonde iyeyo monga momwe Yehova amakondera Aisraeli, ngakhale iwo amapita kukapembedza milungu ina ndi kukonda nsembe za keke zamphesa zowuma.”
И Господ ми рече: Иди пак, залюби жена си, която, ако и да е залюбена от мъжа си, е прелюбодейца, също както Господ люби Израиляните, при все че гледат към чужди богове, и обичат млинове с грозде.
2 Motero ndinamukwatira popereka ndalama khumi ndi zisanu zasiliva, ndiponso mitanga isanu ndi iwiri ya barele.
И тъй, аз си я наех за петнадесет сребърника, и за кор ечемик, и половин кор ечемик.
3 Kenaka ndinamuwuza mkaziyo kuti, “Ukhale nane masiku ambiri; usachitenso zachiwerewere kapena chigololo ndi munthu wina, ndipo ine ndidzakhala nawe.”
И рекох й: Остани за мене за дълго време; да не блудстваш, нито да бъдеш жена на другиго, така и аз ще бъда за тебе.
4 Pakuti Aisraeli adzakhala masiku ambiri opanda mfumu kapena kalonga, osapereka nsembe kapena kuyimika miyala yachipembedzo, wopanda efodi kapena fano.
Защото Израиляните ще останат за дълго време без цар и без началник, без идолски стълп, без ефод и без домашни богове.
5 Pambuyo pake Aisraeli adzabwerera ndi kufunafuna Yehova Mulungu wawo ndi Davide mfumu yawo. Adzabwera kwa Yehova akunjenjemera ndipo adzalandira madalitso mʼmasiku awo otsiriza.
После Израиляните наново ще потърсят Господа своя Бог и царя си Давида; и в послешните дни ще дойдат със страхопочитание при Господа и при неговата благост.