< Hoseya 2 >

1 “Nena kwa abale ako kuti, ‘Ndinu anthu anga,’ kwa alongo ako kuti ‘Ndinu okondedwa anga.’”
Реците браћи својој: Народе мој; и сестрама својим: Помилована.
2 “Dzudzulani amayi anu, adzudzuleni iwo, pakuti si mkazi wanga, ndipo ine sindine mwamuna wake. Iyeyo achotse maonekedwe adama pa nkhope yake, ndi kusakhulupirika pa mawere ake.
Прите се с матером својом, прите се, јер ми није жена, нити сам јој ја муж; нека одбаци курварства своја од лица свог, и прељубе своје од дојака својих,
3 Akapanda kutero ndidzamuvula, ndipo adzakhala wamaliseche monga tsiku limene anabadwa; ndidzamuwumitsa ngati chipululu, adzakhala ngati dziko lopanda madzi, ndi kumupha ndi ludzu.
Да је не бих свукао голу и учинио је каква је била онај дан кад се родила, и да је не бих поставио да буде као пустиња и обратио је да буде као земља сасушена, и уморио је жеђу.
4 Sindidzaonetsa chikondi changa pa ana ake, chifukwa ndi ana a mʼchiwerewere.
И нећу се смиловати на децу њену, јер су копилад.
5 Amayi awo akhala akuchita zachiwerewere ndipo anawabereka anawo akuchita zinthu zochititsa manyazi. Iwo anati, ‘Ine ndidzatsatira zibwenzi zanga, zimene zimandipatsa chakudya ndi madzi, ubweya ndi thonje, mafuta ndi chakumwa.’
Јер се мати њихова курва, срамоти се родитељка њихова; јер говори: Ићи ћу за милосницима својим који ми дају хлеб мој и воду моју, вуну моју и лан мој, уље моје и пиће моје.
6 Choncho njira yake ndidzayitseka ndi minga; ndidzamuzinga ndi khoma kotero kuti sadzapezanso njira yotulukira.
Зато ево ја ћу јој заградити пут трњем и зазидаћу зидом да не нађе стаза својих.
7 Adzathamangira zibwenzi zake koma sadzazipeza; adzazifunafuna koma sadzazipeza. Pamenepo iye adzati, ‘Ndibwerera kwa mwamuna wanga woyamba uja, pakuti ndinali pabwino ndi iyeyo kusiyanitsa ndi pano.’
И трчаће за својим милосницима, али их неће стигнути; и тражиће их, али их неће наћи; па ће рећи: Идем да се вратим к првом мужу свом, јер ми беше боље онда него сада.
8 Iye sanazindikire kuti ndine amene ndinkamupatsa tirigu, vinyo watsopano ndi mafuta. Ndine amene ndinkamukhuthulira siliva ndi golide, zimene ankapangira mafano a Baala.
Јер она не зна да сам јој ја давао жито и вино и уље, и умножавао јој сребро и злато, од ког начинише Вала.
9 “Choncho Ine ndidzamulanda tirigu wanga pa nthawi yokolola, ndi vinyo wanga watsopano pa nthawi yopsinya mphesa. Ndidzamulanda ubweya ndi thonje langa, zomwe akanaphimba nazo umaliseche wake.
Зато ћу узети натраг жито своје, кад буде време, и вино своје, кад буде време, и узећу вуну своју и лан свој, којим би покривала голотињу своју.
10 Motero tsopano ndidzaonetsa maliseche ake pamaso pa zibwenzi zake; palibe ndi mmodzi yemwe adzamupulumutse mʼmanja mwanga.
И открићу ругобу њену пред милосницима њеним, и нико је неће избавити из моје руке.
11 Ndidzathetsa zikondwerero zake zonse: zikondwerero zake za chaka ndi chaka, za mwezi watsopano, za pa masiku a Sabata ndi maphwando ake onse a pa masiku okhazikitsidwa.
И укинућу сваку радост њену, светковине њене, младине њене и суботе њене и све празнике њене.
12 Ndidzawononga mitengo yake ya mpesa ndi mitengo yake yamkuyu, imene iye ankanena kuti inali malipiro ake ochokera kwa zibwenzi zake. Ndidzayisandutsa chithukuluzi, ndipo zirombo zakuthengo zidzadya zipatsozo.
И потрћу чокоте њене и смокве, за које говори: Плата су ми, што ми дадоше милосници моји; и обратићу их у шуму да их једе зверје пољско.
13 Ndidzamulanga chifukwa cha masiku amene anafukiza lubani kwa Abaala; anadzikongoletsa povala mphete ndi mikanda yamtengowapatali ndipo anathamangira zibwenzi zake, koma Ine anandiyiwala,” akutero Yehova.
И походићу на њој дане валимске, у које им је кадила и китила се обоцима и гривнама, и ишла за својим милосницима, и мене заборавила, говори Господ.
14 “Koma tsopano ndidzamukopa mkaziyo; ndidzapita naye ku chipululu ndipo ndidzamuyankhula mwachikondi.
Али ево, ја ћу је примамити и одвешћу је у пустињу, и говорићу с њом лепо.
15 Kumeneko ndidzamubwezera minda yake ya mpesa, ndipo ndidzasandutsa Chigwa cha Akori kukhala khomo la chiyembekezo. Kumeneko iye adzayimba nyimbo monga mʼmasiku a ubwana wake, monga tsiku limene anatuluka ku Igupto.
И даћу јој винограде њене од тог места, и долину Ахор за врата надању, и онде ће певати као за младости своје и као кад је ишла из Мисира.
16 “Tsiku limeneli,” Yehova akuti, “udzandiyitana kuti, ‘Amuna anga;’ sudzandiyitananso kuti, ‘Mbuye wanga.’
И тада ћеш ме, говори Господ, звати: Мужу мој; а нећеш ме више звати: Вале мој.
17 Ndidzachotsa mayina a Abaala pakamwa pake; sadzatchulanso mayina awo popemphera.
Јер ћу уклонити из уста њених имена Валова; и неће им се више помињати имена.
18 Tsiku limenelo ndidzachita pangano ndi zirombo zakuthengo ndi mbalame zamumlengalenga ndiponso zolengedwa zokwawa pansi kuti ziyanjane ndi anthu anga. Ndidzachotsa mʼdzikomo uta, lupanga ndi zida zonse zankhondo, kuti onse apumule mwamtendere.
И тада ћу им учинити завет са зверјем пољским и са птицама небеским и с бубинама земаљским; и поломићу лук и мач и рат да их нестане у земљи, и учинићу да леже без страха.
19 Ndidzakutomera kuti ukhale mkazi wanga mpaka muyaya; ndidzakutomera mwachilungamo, mwaungwiro, mwachikondi ndi mwachifundo.
И заручићу те себи довека, заручићу те себи правдом и судом и милошћу и милосрђем.
20 Ndidzakutomera mokhulupirika ndipo udzadziwa Yehova.
И заручићу те себи вером, и познаћеш Господа.
21 “Tsiku limenelo Ine ndidzayankha,” akutero Yehova. “Ndidzayankha mlengalenga pempho lake lofuna mitambo ndipo mvula idzagwa pa dziko lapansi;
И тада ћу се одазвати, говори Господ, одазваћу се небесима, а она ће се одазвати земљи.
22 ndipo nthaka idzamvera kupempha kwa tirigu, vinyo ndi mafuta, ndipo zidzamvera Yezireeli.
А земља ће се одазвати житу и вину и уљу, а то ће се одазвати Језраелу.
23 Ndidzadzala Israeli mʼdziko kuti akhale wanga: ndidzaonetsa chikondi changa kwa anthu amene ndinkawatchula dzina loti, ‘Sakondedwa.’ Ndidzawawuza amene ndinkawatchula dzina loti, ‘Si anthu anga,’ kuti, ‘Ndinu anthu wanga;’ ndipo adzanena kuti, ‘ndinu Mulungu wathu,’”
И посејаћу је себи на земљи, и смиловаћу се на Лорухаму, и рећи ћу Лоамији: Ти си мој народ, и он ће рећи: Боже мој!

< Hoseya 2 >