< Hoseya 2 >
1 “Nena kwa abale ako kuti, ‘Ndinu anthu anga,’ kwa alongo ako kuti ‘Ndinu okondedwa anga.’”
“Diga a seus irmãos: “Meu povo! e a suas irmãs, “Minha amada!”.
2 “Dzudzulani amayi anu, adzudzuleni iwo, pakuti si mkazi wanga, ndipo ine sindine mwamuna wake. Iyeyo achotse maonekedwe adama pa nkhope yake, ndi kusakhulupirika pa mawere ake.
Contend com sua mãe! Contender, pois ela não é minha esposa, nem eu sou seu marido; e deixá-la afastar a prostituição de seu rosto, e seus adultérios de entre seus seios;
3 Akapanda kutero ndidzamuvula, ndipo adzakhala wamaliseche monga tsiku limene anabadwa; ndidzamuwumitsa ngati chipululu, adzakhala ngati dziko lopanda madzi, ndi kumupha ndi ludzu.
lest Eu a despojo nua, e fazê-la nua como no dia em que ela nasceu, e fazê-la como um sertão selvagem, e a colocaram como uma terra seca, e matá-la com sede.
4 Sindidzaonetsa chikondi changa pa ana ake, chifukwa ndi ana a mʼchiwerewere.
De fato, em seus filhos eu não terei misericórdia, pois eles são filhos da infidelidade.
5 Amayi awo akhala akuchita zachiwerewere ndipo anawabereka anawo akuchita zinthu zochititsa manyazi. Iwo anati, ‘Ine ndidzatsatira zibwenzi zanga, zimene zimandipatsa chakudya ndi madzi, ubweya ndi thonje, mafuta ndi chakumwa.’
Pois sua mãe fez o papel da prostituta. Ela que os concebeu fez vergonhosamente; pois ela disse: “Eu irei atrás de meus amantes”, que me dão meu pão e minha água, minha lã e meu linho, meu óleo e minha bebida”.
6 Choncho njira yake ndidzayitseka ndi minga; ndidzamuzinga ndi khoma kotero kuti sadzapezanso njira yotulukira.
Por isso, eis que eu vou cercar seu caminho com espinhos, e vou construir um muro contra ela, que ela não consegue encontrar seu caminho.
7 Adzathamangira zibwenzi zake koma sadzazipeza; adzazifunafuna koma sadzazipeza. Pamenepo iye adzati, ‘Ndibwerera kwa mwamuna wanga woyamba uja, pakuti ndinali pabwino ndi iyeyo kusiyanitsa ndi pano.’
Ela seguirá depois de seus amantes, mas ela não vai ultrapassá-los; e ela as buscará, mas não as encontrará. Então ela dirá: 'Eu irei e voltarei para meu primeiro marido', pois naquela época era melhor comigo do que agora”.
8 Iye sanazindikire kuti ndine amene ndinkamupatsa tirigu, vinyo watsopano ndi mafuta. Ndine amene ndinkamukhuthulira siliva ndi golide, zimene ankapangira mafano a Baala.
Pois ela não sabia que eu lhe dava o grão, o vinho novo e o óleo, e se multiplicaram para sua prata e ouro, que usaram para Baal.
9 “Choncho Ine ndidzamulanda tirigu wanga pa nthawi yokolola, ndi vinyo wanga watsopano pa nthawi yopsinya mphesa. Ndidzamulanda ubweya ndi thonje langa, zomwe akanaphimba nazo umaliseche wake.
Portanto, vou recuperar meu grão em seu tempo, e meu novo vinho em sua estação, e arrancará minha lã e meu linho, que deveriam ter coberto sua nudez.
10 Motero tsopano ndidzaonetsa maliseche ake pamaso pa zibwenzi zake; palibe ndi mmodzi yemwe adzamupulumutse mʼmanja mwanga.
Agora vou desvendar sua lascívia aos olhos de seus amantes, e ninguém a entregará de minhas mãos.
11 Ndidzathetsa zikondwerero zake zonse: zikondwerero zake za chaka ndi chaka, za mwezi watsopano, za pa masiku a Sabata ndi maphwando ake onse a pa masiku okhazikitsidwa.
Também farei cessar todas as suas comemorações: suas festas, suas luas novas, seus sábados, e todas as suas assembléias solenes.
12 Ndidzawononga mitengo yake ya mpesa ndi mitengo yake yamkuyu, imene iye ankanena kuti inali malipiro ake ochokera kwa zibwenzi zake. Ndidzayisandutsa chithukuluzi, ndipo zirombo zakuthengo zidzadya zipatsozo.
Desperdiçarei suas videiras e suas figueiras, sobre o qual ela disse: “Estes são os meus salários que os meus amantes me deram”. e eu farei deles uma floresta, e os animais do campo devem comê-los.
13 Ndidzamulanga chifukwa cha masiku amene anafukiza lubani kwa Abaala; anadzikongoletsa povala mphete ndi mikanda yamtengowapatali ndipo anathamangira zibwenzi zake, koma Ine anandiyiwala,” akutero Yehova.
I visitará nela os dias dos Baals, para o qual ela queimou incenso quando ela se adornou com seus brincos e suas jóias, e foi atrás de seus amantes e me esqueceu”, diz Yahweh.
14 “Koma tsopano ndidzamukopa mkaziyo; ndidzapita naye ku chipululu ndipo ndidzamuyankhula mwachikondi.
“Portanto, eis que eu a atrairei, e trazê-la para o deserto, e falar ternamente com ela.
15 Kumeneko ndidzamubwezera minda yake ya mpesa, ndipo ndidzasandutsa Chigwa cha Akori kukhala khomo la chiyembekezo. Kumeneko iye adzayimba nyimbo monga mʼmasiku a ubwana wake, monga tsiku limene anatuluka ku Igupto.
Eu lhe darei vinhedos a partir daí, e o vale de Achor por uma porta de esperança; e ela responderá lá como nos dias de sua juventude, e como no dia em que ela saiu da terra do Egito.
16 “Tsiku limeneli,” Yehova akuti, “udzandiyitana kuti, ‘Amuna anga;’ sudzandiyitananso kuti, ‘Mbuye wanga.’
Será nesse dia”, diz Yahweh, “que você me chamará de 'meu marido', e não mais me chamar de “meu mestre”.
17 Ndidzachotsa mayina a Abaala pakamwa pake; sadzatchulanso mayina awo popemphera.
Pois eu tirarei da boca dela os nomes dos Baals, e eles não serão mais mencionados pelo nome.
18 Tsiku limenelo ndidzachita pangano ndi zirombo zakuthengo ndi mbalame zamumlengalenga ndiponso zolengedwa zokwawa pansi kuti ziyanjane ndi anthu anga. Ndidzachotsa mʼdzikomo uta, lupanga ndi zida zonse zankhondo, kuti onse apumule mwamtendere.
Nesse dia farei um pacto para eles com os animais do campo, e com os pássaros do céu, e com as coisas rastejantes do chão. Vou quebrar o arco, a espada e a batalha para fora da terra, e os fará deitar em segurança.
19 Ndidzakutomera kuti ukhale mkazi wanga mpaka muyaya; ndidzakutomera mwachilungamo, mwaungwiro, mwachikondi ndi mwachifundo.
Eu te desposarei para sempre comigo. Sim, eu vos desposarei comigo em retidão, em justiça, em bondade amorosa, e em compaixão.
20 Ndidzakutomera mokhulupirika ndipo udzadziwa Yehova.
Eu até desposarei vocês comigo em fidelidade; e você deve conhecer Yahweh.
21 “Tsiku limenelo Ine ndidzayankha,” akutero Yehova. “Ndidzayankha mlengalenga pempho lake lofuna mitambo ndipo mvula idzagwa pa dziko lapansi;
Acontecerá naquele dia, que eu vou responder”, diz Yahweh. “Eu responderei aos céus, e eles responderão à terra;
22 ndipo nthaka idzamvera kupempha kwa tirigu, vinyo ndi mafuta, ndipo zidzamvera Yezireeli.
e a terra responderá ao grão, e ao novo vinho, e ao óleo; e eles responderão a Jezreel.
23 Ndidzadzala Israeli mʼdziko kuti akhale wanga: ndidzaonetsa chikondi changa kwa anthu amene ndinkawatchula dzina loti, ‘Sakondedwa.’ Ndidzawawuza amene ndinkawatchula dzina loti, ‘Si anthu anga,’ kuti, ‘Ndinu anthu wanga;’ ndipo adzanena kuti, ‘ndinu Mulungu wathu,’”
Eu a semearei para mim na terra; e eu terei piedade dela que não obteve misericórdia; e direi àqueles que não eram meu povo: “Vocês são meu povo”. e dirão: 'Você é meu Deus'”!