< Hoseya 2 >

1 “Nena kwa abale ako kuti, ‘Ndinu anthu anga,’ kwa alongo ako kuti ‘Ndinu okondedwa anga.’”
Sakait uz saviem brāļiem: Mani ļaudis, - un uz savām māsām: Ak apžēlotas!
2 “Dzudzulani amayi anu, adzudzuleni iwo, pakuti si mkazi wanga, ndipo ine sindine mwamuna wake. Iyeyo achotse maonekedwe adama pa nkhope yake, ndi kusakhulupirika pa mawere ake.
Ejat tiesāties ar savu māti, ejat tiesāties, jo tā nav Mana sieva, un Es neesmu viņas vīrs, lai viņa savu maucību noliek no sava vaiga un savu laulības pārkāpšanu no savām krūtīm,
3 Akapanda kutero ndidzamuvula, ndipo adzakhala wamaliseche monga tsiku limene anabadwa; ndidzamuwumitsa ngati chipululu, adzakhala ngati dziko lopanda madzi, ndi kumupha ndi ludzu.
Ka Es to nenovelku pliku un viņu nenostādu kā tai dienā, kad viņa piedzima, un viņu nedaru par tuksnesi un nelieku par sausu zemi un viņu nenonāvēju caur tvīkšanu,
4 Sindidzaonetsa chikondi changa pa ana ake, chifukwa ndi ana a mʼchiwerewere.
Un ka neapžēlojos par viņas bērniem, jo tie ir maukas bērni.
5 Amayi awo akhala akuchita zachiwerewere ndipo anawabereka anawo akuchita zinthu zochititsa manyazi. Iwo anati, ‘Ine ndidzatsatira zibwenzi zanga, zimene zimandipatsa chakudya ndi madzi, ubweya ndi thonje, mafuta ndi chakumwa.’
Jo viņu māte dzen maucību, viņu dzemdētāja ir negodīga; jo tā saka: es iešu saviem drauģeļiem pakaļ, kas man dod manu maizi un manu ūdeni, manu vilnu un manus linus, manu eļļu un manu dzērienu.
6 Choncho njira yake ndidzayitseka ndi minga; ndidzamuzinga ndi khoma kotero kuti sadzapezanso njira yotulukira.
Tādēļ redzi, Es tavu ceļu aiztaisīšu ar ērkšķiem un darīšu tur sienu priekšā, ka viņa savas tekas nevar atrast.
7 Adzathamangira zibwenzi zake koma sadzazipeza; adzazifunafuna koma sadzazipeza. Pamenepo iye adzati, ‘Ndibwerera kwa mwamuna wanga woyamba uja, pakuti ndinali pabwino ndi iyeyo kusiyanitsa ndi pano.’
Un viņa dzīsies saviem drauģeļiem pakaļ, bet tos nepanāks, un viņa tos meklēs, bet neatradīs; tad viņa sacīs: es iešu un atgriezīšos pie sava pirmā vīra, jo to brīdi man bija labāki nekā tagad.
8 Iye sanazindikire kuti ndine amene ndinkamupatsa tirigu, vinyo watsopano ndi mafuta. Ndine amene ndinkamukhuthulira siliva ndi golide, zimene ankapangira mafano a Baala.
Jo viņa neatzīst, ka Es tas esmu, kas viņai devis labību un vīnu un eļļu, un vairojis viņas sudrabu un zeltu, ko tie priekš Baāla ir lietojuši.
9 “Choncho Ine ndidzamulanda tirigu wanga pa nthawi yokolola, ndi vinyo wanga watsopano pa nthawi yopsinya mphesa. Ndidzamulanda ubweya ndi thonje langa, zomwe akanaphimba nazo umaliseche wake.
Tādēļ Es atkal atņemšu Savu labību savā laikā un Savu vīnu savā brīdī, un atraušu Savu vilnu un Savus linus, ar ko tie apseguši savu plikumu.
10 Motero tsopano ndidzaonetsa maliseche ake pamaso pa zibwenzi zake; palibe ndi mmodzi yemwe adzamupulumutse mʼmanja mwanga.
Un nu Es viņas kaunu atklāšu priekš viņas drauģeļu acīm, un neviens viņu neizglābs no Manas rokas.
11 Ndidzathetsa zikondwerero zake zonse: zikondwerero zake za chaka ndi chaka, za mwezi watsopano, za pa masiku a Sabata ndi maphwando ake onse a pa masiku okhazikitsidwa.
Un Es nobeigšu visu viņas līksmību, viņas svētkus, viņas jaunos mēnešus un viņas svētdienas un visus viņas svētos laikus.
12 Ndidzawononga mitengo yake ya mpesa ndi mitengo yake yamkuyu, imene iye ankanena kuti inali malipiro ake ochokera kwa zibwenzi zake. Ndidzayisandutsa chithukuluzi, ndipo zirombo zakuthengo zidzadya zipatsozo.
Un Es postīšu viņas vīna koku un vīģes koku, par ko viņa saka: tā ir mana maukas alga, ko man mani drauģeļi devuši; bet Es tos darīšu par mežu, un zvēriem laukā tos būs ēst.
13 Ndidzamulanga chifukwa cha masiku amene anafukiza lubani kwa Abaala; anadzikongoletsa povala mphete ndi mikanda yamtengowapatali ndipo anathamangira zibwenzi zake, koma Ine anandiyiwala,” akutero Yehova.
Un Es pie viņas piemeklēšu tās Baālu dienas, ka viņa tiem ir kvēpinājusi un greznojusies ar savām sprādzēm un glītumiem un dzinusies pakaļ saviem drauģeļiem, bet Mani ir aizmirsuši, saka Tas Kungs.
14 “Koma tsopano ndidzamukopa mkaziyo; ndidzapita naye ku chipululu ndipo ndidzamuyankhula mwachikondi.
Tādēļ redzi, Es viņu labināšu un viņu vedīšu tuksnesī un runāšu mīlīgi ar viņu.
15 Kumeneko ndidzamubwezera minda yake ya mpesa, ndipo ndidzasandutsa Chigwa cha Akori kukhala khomo la chiyembekezo. Kumeneko iye adzayimba nyimbo monga mʼmasiku a ubwana wake, monga tsiku limene anatuluka ku Igupto.
Un Es tai atdošu viņas vīna dārzus no tejienes un to Ahora ieleju par cerības durvīm. Un tur viņa dziedās kā savas jaunības dienās, un kā tai laikā, kad viņa cēlās no Ēģiptes zemes.
16 “Tsiku limeneli,” Yehova akuti, “udzandiyitana kuti, ‘Amuna anga;’ sudzandiyitananso kuti, ‘Mbuye wanga.’
Un tai dienā, saka Tas Kungs, tu sauksi: mans vīrs, un tu Mani vairs nesauksi: mans Baāl.
17 Ndidzachotsa mayina a Abaala pakamwa pake; sadzatchulanso mayina awo popemphera.
Un Es Baālu vārdus izraušu no viņas mutes, ka tos ar viņu vārdiem vairs nepieminēs.
18 Tsiku limenelo ndidzachita pangano ndi zirombo zakuthengo ndi mbalame zamumlengalenga ndiponso zolengedwa zokwawa pansi kuti ziyanjane ndi anthu anga. Ndidzachotsa mʼdzikomo uta, lupanga ndi zida zonse zankhondo, kuti onse apumule mwamtendere.
Un tai dienā Es darīšu priekš viņiem derību ar zvēriem laukā un ar putniem apakš debess un ar tārpiem virs zemes, un salauzīšu stopu un zobenu un karu no zemes, un likšu tiem droši dzīvot.
19 Ndidzakutomera kuti ukhale mkazi wanga mpaka muyaya; ndidzakutomera mwachilungamo, mwaungwiro, mwachikondi ndi mwachifundo.
Un Es ar tevi saderēšos uz mūžību, un Es ar tevi saderēšos taisnībā un tiesā un žēlastībā un apžēlošanā.
20 Ndidzakutomera mokhulupirika ndipo udzadziwa Yehova.
Un Es ar tevi saderēšos ticībā, un tu atzīsi To Kungu.
21 “Tsiku limenelo Ine ndidzayankha,” akutero Yehova. “Ndidzayankha mlengalenga pempho lake lofuna mitambo ndipo mvula idzagwa pa dziko lapansi;
Un tai dienā Es paklausīšu, saka Tas Kungs; Es paklausīšu debesi, un tā paklausīs zemi.
22 ndipo nthaka idzamvera kupempha kwa tirigu, vinyo ndi mafuta, ndipo zidzamvera Yezireeli.
Un zeme paklausīs labību un vīnu un eļļu, un tie paklausīs Jezreēli.
23 Ndidzadzala Israeli mʼdziko kuti akhale wanga: ndidzaonetsa chikondi changa kwa anthu amene ndinkawatchula dzina loti, ‘Sakondedwa.’ Ndidzawawuza amene ndinkawatchula dzina loti, ‘Si anthu anga,’ kuti, ‘Ndinu anthu wanga;’ ndipo adzanena kuti, ‘ndinu Mulungu wathu,’”
Un Es tos darīšu Sev par dzimumu virs zemes un apžēlošos par to neapžēloto un sacīšu uz tiem, kas nebija Mani ļaudis: jūs esat Mani ļaudis; un tie sacīs: mans Dievs!

< Hoseya 2 >