< Hoseya 2 >

1 “Nena kwa abale ako kuti, ‘Ndinu anthu anga,’ kwa alongo ako kuti ‘Ndinu okondedwa anga.’”
Ibagayo kadagiti kakabsatyo a lallaki, 'Dagiti tattaok!' ken kadagiti kakabsatyo a babbai, ''Naipakitan kadakayo ti asi.'''
2 “Dzudzulani amayi anu, adzudzuleni iwo, pakuti si mkazi wanga, ndipo ine sindine mwamuna wake. Iyeyo achotse maonekedwe adama pa nkhope yake, ndi kusakhulupirika pa mawere ake.
Idarumyo ti inayo, idarumyo, gapu ta saan nga isuna ti asawak, ken saan met a siak ti asawana. Iwaksina koma ti kinabalangkantisna, ken ti pannakikamalalana iti nagbaetan dagiti susona.
3 Akapanda kutero ndidzamuvula, ndipo adzakhala wamaliseche monga tsiku limene anabadwa; ndidzamuwumitsa ngati chipululu, adzakhala ngati dziko lopanda madzi, ndi kumupha ndi ludzu.
Ta no saan, labusakto isuna ket ipakitak ti kinalamolamona kas iti aldaw a pannakaipasngayna. Pagbalinekto isuna a kas iti let-ang, kas iti namaga a daga, ket papatayekto isuna gapu iti pannakawaw.
4 Sindidzaonetsa chikondi changa pa ana ake, chifukwa ndi ana a mʼchiwerewere.
Diakto kaasian dagiti annakna, gapu ta annak ida ti kinabalangkantis.
5 Amayi awo akhala akuchita zachiwerewere ndipo anawabereka anawo akuchita zinthu zochititsa manyazi. Iwo anati, ‘Ine ndidzatsatira zibwenzi zanga, zimene zimandipatsa chakudya ndi madzi, ubweya ndi thonje, mafuta ndi chakumwa.’
Ta maysa a balangkantis ti inada, ken nagtignay a nakababain ti nangisikog kadakuada. Kinunana, “Surotekto dagiti kaayan-ayatko, ta ik-ikkandak iti tinapay ken danumko, dagiti pagan-anayko a de lana ken linen, ti lanak ken inumek.”
6 Choncho njira yake ndidzayitseka ndi minga; ndidzamuzinga ndi khoma kotero kuti sadzapezanso njira yotulukira.
Ngarud, agaladakto kadagiti siit a mangserra iti dalanna. Mangipatakderakto iti pader tapno saanna a masarakan ti dalanna.
7 Adzathamangira zibwenzi zake koma sadzazipeza; adzazifunafuna koma sadzazipeza. Pamenepo iye adzati, ‘Ndibwerera kwa mwamuna wanga woyamba uja, pakuti ndinali pabwino ndi iyeyo kusiyanitsa ndi pano.’
Surotennanto dagiti kaayan-ayatna, ngem saannanto ida a makamatan. Sapulenna ida ngem saannanto ida a mabirokan. Ket ibagananto, “Agsubliak iti immuna nga asawak, ta nasaysayaat kaniak idi ngem ita.”
8 Iye sanazindikire kuti ndine amene ndinkamupatsa tirigu, vinyo watsopano ndi mafuta. Ndine amene ndinkamukhuthulira siliva ndi golide, zimene ankapangira mafano a Baala.
Ta saanna nga ammo a siak ti nangted kenkuana iti bukel, ti baro nga arak ken ti lana, ken nangted kenkuana iti aglaplapusanan a pirak ken balitok, nga inusarda a maipaay kenni Baal.
9 “Choncho Ine ndidzamulanda tirigu wanga pa nthawi yokolola, ndi vinyo wanga watsopano pa nthawi yopsinya mphesa. Ndidzamulanda ubweya ndi thonje langa, zomwe akanaphimba nazo umaliseche wake.
Isu nga alaekto me laeng dagiti bukelna iti tiempo ti panagaapit, ken ti baro nga arakko iti panawenna. Alaekto met laeng dagiti pagan-anayko a de lana ken linen a nausar a mangabbong iti kinalamolamona.
10 Motero tsopano ndidzaonetsa maliseche ake pamaso pa zibwenzi zake; palibe ndi mmodzi yemwe adzamupulumutse mʼmanja mwanga.
Kalpasanna, labusakto isuna iti sangoanan dagiti kaayan-ayatna, ket awanto ti mangispal kenkuana manipud iti imak.
11 Ndidzathetsa zikondwerero zake zonse: zikondwerero zake za chaka ndi chaka, za mwezi watsopano, za pa masiku a Sabata ndi maphwando ake onse a pa masiku okhazikitsidwa.
Pagsardengekto pay dagiti amin a panagrambakna— dagiti padayana, dagiti panagrambakna iti baro a bulan, dagiti Aldaw a Panaginanana, ken amin a naituding a fiestana.
12 Ndidzawononga mitengo yake ya mpesa ndi mitengo yake yamkuyu, imene iye ankanena kuti inali malipiro ake ochokera kwa zibwenzi zake. Ndidzayisandutsa chithukuluzi, ndipo zirombo zakuthengo zidzadya zipatsozo.
“Dadaelekto dagiti kaubasanna ken dagiti kayona nga igos, ti nangibagaanna a, “Dagitoy dagiti tangdanko nga inted kaniak dagiti kaayan-ayatko.” Pagbalinekto ida a kabakiran, ken kanento dagitoy dagiti ayup iti tay-ak.
13 Ndidzamulanga chifukwa cha masiku amene anafukiza lubani kwa Abaala; anadzikongoletsa povala mphete ndi mikanda yamtengowapatali ndipo anathamangira zibwenzi zake, koma Ine anandiyiwala,” akutero Yehova.
Dusaekto isuna gapu kadagiti aldaw a fiesta dagiti Baal, idi nangpuor isuna iti insenso para kadakuada, idi inarkosanna ti bagina kadagiti singsing ken alahasna, ket simmurot isuna kadagiti kaayan-ayatna ket linipatnak.” Daytoy ti pakaammo ni Yahweh.
14 “Koma tsopano ndidzamukopa mkaziyo; ndidzapita naye ku chipululu ndipo ndidzamuyankhula mwachikondi.
Isu a magun-odkonto manen isuna. Ipankonto isuna iti let-ang ket agsaoakto a siaalumanay kenkuana.
15 Kumeneko ndidzamubwezera minda yake ya mpesa, ndipo ndidzasandutsa Chigwa cha Akori kukhala khomo la chiyembekezo. Kumeneko iye adzayimba nyimbo monga mʼmasiku a ubwana wake, monga tsiku limene anatuluka ku Igupto.
Isublikto kenkuana dagiti kaubasanna, ken ti tanap ti Akor a kas ruangan ti namnama. Sungbatannakto sadiay a kas iti inaramidna idi panawen ti kinaagtutubona, kas kadagiti aldaw a rimmuar isuna iti daga ti Egipto.
16 “Tsiku limeneli,” Yehova akuti, “udzandiyitana kuti, ‘Amuna anga;’ sudzandiyitananso kuti, ‘Mbuye wanga.’
“Iti daytanto nga aldaw”— daytoy ti pakaammo ni Yahweh—”nga awagannakto a, 'Ti asawak,' ket saanakton a pulos nga awagan a, 'Ti Baalko.'
17 Ndidzachotsa mayina a Abaala pakamwa pake; sadzatchulanso mayina awo popemphera.
Ta ikkatekto dagiti nagan dagiti Baal iti ngiwatna; saanton a pulos a malagip dagiti naganda.”
18 Tsiku limenelo ndidzachita pangano ndi zirombo zakuthengo ndi mbalame zamumlengalenga ndiponso zolengedwa zokwawa pansi kuti ziyanjane ndi anthu anga. Ndidzachotsa mʼdzikomo uta, lupanga ndi zida zonse zankhondo, kuti onse apumule mwamtendere.
“Iti dayta nga aldaw, makitulagakto kadakuada ken kadagiti narungsot nga ayup iti tay-ak, kasta met kadagiti billit iti tangatang, ken kadagiti amin nga agkarkarayam iti daga. Ikkatekto ti bai, ti kampilan, ken ti gubat iti daga, ket paiddaenkanto iti kinatalged.
19 Ndidzakutomera kuti ukhale mkazi wanga mpaka muyaya; ndidzakutomera mwachilungamo, mwaungwiro, mwachikondi ndi mwachifundo.
Ikarik nga agbalinnakto nga asawam iti agnanayon. Ikarik nga agbalinakto nga asawam iti kinalinteg, iti hustisia, iti kinapudno iti tulag, ken iti asi.
20 Ndidzakutomera mokhulupirika ndipo udzadziwa Yehova.
Ikarik nga agbalinakto nga asawam iti kinapudno. Ket maam-ammonakto, siak a ni Yahweh.
21 “Tsiku limenelo Ine ndidzayankha,” akutero Yehova. “Ndidzayankha mlengalenga pempho lake lofuna mitambo ndipo mvula idzagwa pa dziko lapansi;
Ket iti dayta nga aldaw, sumungbatakto”—daytoy ti pakaammo ni Yahweh. “Sungbatakto dagiti langit, ket sungbatandanto ti daga.
22 ndipo nthaka idzamvera kupempha kwa tirigu, vinyo ndi mafuta, ndipo zidzamvera Yezireeli.
Sungbatanto ti daga ti bukel, ti baro nga arak ken ti lana, ket sungbatandanto ti Jezreel.
23 Ndidzadzala Israeli mʼdziko kuti akhale wanga: ndidzaonetsa chikondi changa kwa anthu amene ndinkawatchula dzina loti, ‘Sakondedwa.’ Ndidzawawuza amene ndinkawatchula dzina loti, ‘Si anthu anga,’ kuti, ‘Ndinu anthu wanga;’ ndipo adzanena kuti, ‘ndinu Mulungu wathu,’”
Imulakto isuna iti daga nga agpaay kaniak, ket kaasiakto ti Lo-ruhama. Ibagakto iti Lo-ammi, 'Dakayo dagiti Ammi-atta,' ket ibagadanto kaniak, 'Sika ti Diosko.”'

< Hoseya 2 >