< Hoseya 2 >

1 “Nena kwa abale ako kuti, ‘Ndinu anthu anga,’ kwa alongo ako kuti ‘Ndinu okondedwa anga.’”
« Dis à tes frères: « Mon peuple »! et à tes sœurs: « Mon bien-aimé ».
2 “Dzudzulani amayi anu, adzudzuleni iwo, pakuti si mkazi wanga, ndipo ine sindine mwamuna wake. Iyeyo achotse maonekedwe adama pa nkhope yake, ndi kusakhulupirika pa mawere ake.
Contestez avec votre mère! Contestez, car elle n'est pas ma femme, je ne suis pas non plus son mari; et qu'elle fasse disparaître sa prostitution de son visage, et ses adultères d'entre ses seins;
3 Akapanda kutero ndidzamuvula, ndipo adzakhala wamaliseche monga tsiku limene anabadwa; ndidzamuwumitsa ngati chipululu, adzakhala ngati dziko lopanda madzi, ndi kumupha ndi ludzu.
de peur que je ne la déshabille, et la rendre nue comme au jour de sa naissance, et la rendre comme une nature sauvage, et l'a placée comme une terre sèche, et la tuer par la soif.
4 Sindidzaonetsa chikondi changa pa ana ake, chifukwa ndi ana a mʼchiwerewere.
En effet, je n'aurai aucune pitié pour ses enfants, car ils sont les enfants de l'infidélité.
5 Amayi awo akhala akuchita zachiwerewere ndipo anawabereka anawo akuchita zinthu zochititsa manyazi. Iwo anati, ‘Ine ndidzatsatira zibwenzi zanga, zimene zimandipatsa chakudya ndi madzi, ubweya ndi thonje, mafuta ndi chakumwa.’
Car leur mère s'est prostituée. Celle qui les a conçus a commis une faute; car elle a dit: « Je vais suivre mes amants », qui me donnent mon pain et mon eau, ma laine et mon lin, mon huile et ma boisson.
6 Choncho njira yake ndidzayitseka ndi minga; ndidzamuzinga ndi khoma kotero kuti sadzapezanso njira yotulukira.
C'est pourquoi voici, je vais couvrir d'épines ton chemin, et je construirai un mur contre elle, qu'elle ne peut pas trouver son chemin.
7 Adzathamangira zibwenzi zake koma sadzazipeza; adzazifunafuna koma sadzazipeza. Pamenepo iye adzati, ‘Ndibwerera kwa mwamuna wanga woyamba uja, pakuti ndinali pabwino ndi iyeyo kusiyanitsa ndi pano.’
Elle suivra ses amants, mais elle ne les dépassera pas; et elle les cherchera, mais ne les trouvera pas. Elle dira alors: « Je m'en vais et je retourne chez mon premier mari, car j'étais alors mieux avec moi que maintenant.
8 Iye sanazindikire kuti ndine amene ndinkamupatsa tirigu, vinyo watsopano ndi mafuta. Ndine amene ndinkamukhuthulira siliva ndi golide, zimene ankapangira mafano a Baala.
Car elle ne savait pas que je lui avais donné le grain, le vin nouveau et l'huile, et lui ont multiplié l'argent et l'or, qu'ils utilisaient pour Baal.
9 “Choncho Ine ndidzamulanda tirigu wanga pa nthawi yokolola, ndi vinyo wanga watsopano pa nthawi yopsinya mphesa. Ndidzamulanda ubweya ndi thonje langa, zomwe akanaphimba nazo umaliseche wake.
C'est pourquoi je reprendrai mon blé en son temps, et mon vin nouveau en sa saison, et il arrachera ma laine et mon lin qui auraient dû couvrir sa nudité.
10 Motero tsopano ndidzaonetsa maliseche ake pamaso pa zibwenzi zake; palibe ndi mmodzi yemwe adzamupulumutse mʼmanja mwanga.
Maintenant, je découvrirai son impudicité aux yeux de ses amants, et personne ne la délivrera de ma main.
11 Ndidzathetsa zikondwerero zake zonse: zikondwerero zake za chaka ndi chaka, za mwezi watsopano, za pa masiku a Sabata ndi maphwando ake onse a pa masiku okhazikitsidwa.
Je ferai aussi cesser toutes ses célébrations: ses fêtes, ses nouvelles lunes, ses sabbats, et toutes ses assemblées solennelles.
12 Ndidzawononga mitengo yake ya mpesa ndi mitengo yake yamkuyu, imene iye ankanena kuti inali malipiro ake ochokera kwa zibwenzi zake. Ndidzayisandutsa chithukuluzi, ndipo zirombo zakuthengo zidzadya zipatsozo.
Je détruirai ses vignes et ses figuiers, dont elle a dit: « Voici le salaire que m'ont donné mes amants ». et je leur ferai une forêt, et les animaux des champs les mangeront.
13 Ndidzamulanga chifukwa cha masiku amene anafukiza lubani kwa Abaala; anadzikongoletsa povala mphete ndi mikanda yamtengowapatali ndipo anathamangira zibwenzi zake, koma Ine anandiyiwala,” akutero Yehova.
Je visiterai sur elle les jours des Baals, à laquelle elle a brûlé de l'encens quand elle s'est parée de ses boucles d'oreilles et de ses bijoux, et est allée chercher ses amants et m'ont oublié », dit Yahvé.
14 “Koma tsopano ndidzamukopa mkaziyo; ndidzapita naye ku chipululu ndipo ndidzamuyankhula mwachikondi.
« Voici donc que je vais la séduire, et l'amener dans le désert, et lui parler tendrement.
15 Kumeneko ndidzamubwezera minda yake ya mpesa, ndipo ndidzasandutsa Chigwa cha Akori kukhala khomo la chiyembekezo. Kumeneko iye adzayimba nyimbo monga mʼmasiku a ubwana wake, monga tsiku limene anatuluka ku Igupto.
Je lui donnerai des vignes à partir de là, et la vallée d'Achor pour une porte d'espoir; et elle y répondra comme au temps de sa jeunesse, et comme au jour où elle est sortie du pays d'Égypte.
16 “Tsiku limeneli,” Yehova akuti, “udzandiyitana kuti, ‘Amuna anga;’ sudzandiyitananso kuti, ‘Mbuye wanga.’
Il en sera ainsi en ce jour-là, dit Yahvé, « que tu m'appelles 'mon mari', et ne m'appelle plus « mon maître ».
17 Ndidzachotsa mayina a Abaala pakamwa pake; sadzatchulanso mayina awo popemphera.
Car j'ôterai de sa bouche les noms des Baals, et ils ne seront plus mentionnés par leur nom.
18 Tsiku limenelo ndidzachita pangano ndi zirombo zakuthengo ndi mbalame zamumlengalenga ndiponso zolengedwa zokwawa pansi kuti ziyanjane ndi anthu anga. Ndidzachotsa mʼdzikomo uta, lupanga ndi zida zonse zankhondo, kuti onse apumule mwamtendere.
En ce jour-là, je conclurai pour eux une alliance avec les animaux des champs, et avec les oiseaux du ciel, et avec les reptiles du sol. Je briserai l'arc, l'épée et la bataille hors du pays, et les fera se coucher en toute sécurité.
19 Ndidzakutomera kuti ukhale mkazi wanga mpaka muyaya; ndidzakutomera mwachilungamo, mwaungwiro, mwachikondi ndi mwachifundo.
Je te fiancerai à moi pour toujours. Oui, je te fiancerai à moi dans la droiture, la justice, la bonté et la compassion.
20 Ndidzakutomera mokhulupirika ndipo udzadziwa Yehova.
Je te fiancerai même à moi dans la fidélité; et vous connaîtrez Yahvé.
21 “Tsiku limenelo Ine ndidzayankha,” akutero Yehova. “Ndidzayankha mlengalenga pempho lake lofuna mitambo ndipo mvula idzagwa pa dziko lapansi;
Il arrivera en ce jour-là que je répondrai, dit Yahvé. « Je vais répondre aux cieux, et ils répondront à la terre;
22 ndipo nthaka idzamvera kupempha kwa tirigu, vinyo ndi mafuta, ndipo zidzamvera Yezireeli.
et la terre répondra au grain, au vin nouveau et à l'huile; et ils répondront à Jezreel.
23 Ndidzadzala Israeli mʼdziko kuti akhale wanga: ndidzaonetsa chikondi changa kwa anthu amene ndinkawatchula dzina loti, ‘Sakondedwa.’ Ndidzawawuza amene ndinkawatchula dzina loti, ‘Si anthu anga,’ kuti, ‘Ndinu anthu wanga;’ ndipo adzanena kuti, ‘ndinu Mulungu wathu,’”
Je la sèmerai pour moi dans la terre; et j'aurai pitié de celle qui n'avait pas obtenu de pitié; et je dirai à ceux qui n'étaient pas mon peuple: « Vous êtes mon peuple ». et ils diront: « Tu es mon Dieu ».

< Hoseya 2 >