< Hoseya 2 >

1 “Nena kwa abale ako kuti, ‘Ndinu anthu anga,’ kwa alongo ako kuti ‘Ndinu okondedwa anga.’”
to say to/for brother: compatriot your people my and to/for sister your to have compassion
2 “Dzudzulani amayi anu, adzudzuleni iwo, pakuti si mkazi wanga, ndipo ine sindine mwamuna wake. Iyeyo achotse maonekedwe adama pa nkhope yake, ndi kusakhulupirika pa mawere ake.
to contend in/on/with mother your to contend for he/she/it not woman: wife my and I not man: husband her and to turn aside: remove fornication her from face her and adultery her from between breast her
3 Akapanda kutero ndidzamuvula, ndipo adzakhala wamaliseche monga tsiku limene anabadwa; ndidzamuwumitsa ngati chipululu, adzakhala ngati dziko lopanda madzi, ndi kumupha ndi ludzu.
lest to strip her naked and to set her like/as day to beget she and to set: make her like/as wilderness and to set: make her like/as land: country/planet dryness and to die her in/on/with thirst
4 Sindidzaonetsa chikondi changa pa ana ake, chifukwa ndi ana a mʼchiwerewere.
and [obj] son: child her not to have compassion for son: child fornication they(masc.)
5 Amayi awo akhala akuchita zachiwerewere ndipo anawabereka anawo akuchita zinthu zochititsa manyazi. Iwo anati, ‘Ine ndidzatsatira zibwenzi zanga, zimene zimandipatsa chakudya ndi madzi, ubweya ndi thonje, mafuta ndi chakumwa.’
for to fornicate mother their be ashamed to conceive them for to say to go: went after to love: lover me to give: give food: bread my and water my wool my and flax my oil my and drink my
6 Choncho njira yake ndidzayitseka ndi minga; ndidzamuzinga ndi khoma kotero kuti sadzapezanso njira yotulukira.
to/for so look! I to hedge [obj] way: journey your in/on/with thorn and to wall up/off [obj] wall her and path her not to find
7 Adzathamangira zibwenzi zake koma sadzazipeza; adzazifunafuna koma sadzazipeza. Pamenepo iye adzati, ‘Ndibwerera kwa mwamuna wanga woyamba uja, pakuti ndinali pabwino ndi iyeyo kusiyanitsa ndi pano.’
and to pursue [obj] to love: lover her and not to overtake [obj] them and to seek them and not to find and to say to go: went and to return: return to(wards) man: husband my [the] first for be pleasing to/for me then from now
8 Iye sanazindikire kuti ndine amene ndinkamupatsa tirigu, vinyo watsopano ndi mafuta. Ndine amene ndinkamukhuthulira siliva ndi golide, zimene ankapangira mafano a Baala.
and he/she/it not to know for I to give: give to/for her [the] grain and [the] new wine and [the] oil and silver: money to multiply to/for her and gold to make: offer to/for Baal
9 “Choncho Ine ndidzamulanda tirigu wanga pa nthawi yokolola, ndi vinyo wanga watsopano pa nthawi yopsinya mphesa. Ndidzamulanda ubweya ndi thonje langa, zomwe akanaphimba nazo umaliseche wake.
to/for so to return: return and to take: take grain my in/on/with time his and new wine my in/on/with meeting: time appointed his and to rescue wool my and flax my to/for to cover [obj] nakedness her
10 Motero tsopano ndidzaonetsa maliseche ake pamaso pa zibwenzi zake; palibe ndi mmodzi yemwe adzamupulumutse mʼmanja mwanga.
and now to reveal: uncover [obj] lewdness her to/for eye: seeing to love: lover her and man: anyone not to rescue her from hand: power my
11 Ndidzathetsa zikondwerero zake zonse: zikondwerero zake za chaka ndi chaka, za mwezi watsopano, za pa masiku a Sabata ndi maphwando ake onse a pa masiku okhazikitsidwa.
and to cease all rejoicing her feast her month: new moon her and Sabbath her and all meeting: festival her
12 Ndidzawononga mitengo yake ya mpesa ndi mitengo yake yamkuyu, imene iye ankanena kuti inali malipiro ake ochokera kwa zibwenzi zake. Ndidzayisandutsa chithukuluzi, ndipo zirombo zakuthengo zidzadya zipatsozo.
and be desolate: destroyed vine her and fig her which to say wages they(masc.) to/for me which to give: pay to/for me to love: lover me and to set: make them to/for wood and to eat them living thing [the] land: country
13 Ndidzamulanga chifukwa cha masiku amene anafukiza lubani kwa Abaala; anadzikongoletsa povala mphete ndi mikanda yamtengowapatali ndipo anathamangira zibwenzi zake, koma Ine anandiyiwala,” akutero Yehova.
and to reckon: punish upon her [obj] day [the] Baal which to offer: offer to/for them and to adorn ring her and jewelry her and to go: follow after to love: lover her and [obj] me to forget utterance LORD
14 “Koma tsopano ndidzamukopa mkaziyo; ndidzapita naye ku chipululu ndipo ndidzamuyankhula mwachikondi.
to/for so behold I to entice her and to go: take her [the] wilderness and to speak: speak (upon *L(abh)*) heart her
15 Kumeneko ndidzamubwezera minda yake ya mpesa, ndipo ndidzasandutsa Chigwa cha Akori kukhala khomo la chiyembekezo. Kumeneko iye adzayimba nyimbo monga mʼmasiku a ubwana wake, monga tsiku limene anatuluka ku Igupto.
and to give: give to/for her [obj] vineyard her from there and [obj] Valley (of Achor) (Valley of) Achor to/for entrance hope and to answer there [to] like/as day youth her and like/as day to ascend: rise she from land: country/planet Egypt
16 “Tsiku limeneli,” Yehova akuti, “udzandiyitana kuti, ‘Amuna anga;’ sudzandiyitananso kuti, ‘Mbuye wanga.’
and to be in/on/with day [the] he/she/it utterance LORD to call: call by man: husband my and not to call: call by to/for me still Baal my
17 Ndidzachotsa mayina a Abaala pakamwa pake; sadzatchulanso mayina awo popemphera.
and to turn aside: remove [obj] name [the] Baal from lip her and not to remember still in/on/with name their
18 Tsiku limenelo ndidzachita pangano ndi zirombo zakuthengo ndi mbalame zamumlengalenga ndiponso zolengedwa zokwawa pansi kuti ziyanjane ndi anthu anga. Ndidzachotsa mʼdzikomo uta, lupanga ndi zida zonse zankhondo, kuti onse apumule mwamtendere.
and to cut: make(covenant) to/for them covenant in/on/with day [the] he/she/it with living thing [the] land: country and with bird [the] heaven and creeping [the] land: soil and bow and sword and battle to break from [the] land: country/planet and to lie down: lay down them to/for security
19 Ndidzakutomera kuti ukhale mkazi wanga mpaka muyaya; ndidzakutomera mwachilungamo, mwaungwiro, mwachikondi ndi mwachifundo.
and to betroth you to/for me to/for forever: enduring and to betroth you to/for me in/on/with righteousness and in/on/with justice and in/on/with kindness and in/on/with compassion
20 Ndidzakutomera mokhulupirika ndipo udzadziwa Yehova.
and to betroth you to/for me in/on/with faithfulness and to know [obj] LORD
21 “Tsiku limenelo Ine ndidzayankha,” akutero Yehova. “Ndidzayankha mlengalenga pempho lake lofuna mitambo ndipo mvula idzagwa pa dziko lapansi;
and to be in/on/with day [the] he/she/it to answer utterance LORD to answer [obj] [the] heaven and they(masc.) to answer [obj] [the] land: country/planet
22 ndipo nthaka idzamvera kupempha kwa tirigu, vinyo ndi mafuta, ndipo zidzamvera Yezireeli.
and [the] land: country/planet to answer [obj] [the] grain and [obj] [the] new wine and [obj] [the] oil and they(masc.) to answer [obj] Jezreel
23 Ndidzadzala Israeli mʼdziko kuti akhale wanga: ndidzaonetsa chikondi changa kwa anthu amene ndinkawatchula dzina loti, ‘Sakondedwa.’ Ndidzawawuza amene ndinkawatchula dzina loti, ‘Si anthu anga,’ kuti, ‘Ndinu anthu wanga;’ ndipo adzanena kuti, ‘ndinu Mulungu wathu,’”
and to sow her to/for me in/on/with land: country/planet and to have compassion [obj] not to have compassion and to say to/for not people my people my you(m. s.) and he/she/it to say God my

< Hoseya 2 >