< Hoseya 2 >

1 “Nena kwa abale ako kuti, ‘Ndinu anthu anga,’ kwa alongo ako kuti ‘Ndinu okondedwa anga.’”
Say ye to your brothers, Ammi, and to your sisters, Ruhamah.
2 “Dzudzulani amayi anu, adzudzuleni iwo, pakuti si mkazi wanga, ndipo ine sindine mwamuna wake. Iyeyo achotse maonekedwe adama pa nkhope yake, ndi kusakhulupirika pa mawere ake.
Contend with your mother. Contend, for she is not my wife, nor am I her husband. And let her put away her whoredoms from her face, and her adulteries from between her breasts,
3 Akapanda kutero ndidzamuvula, ndipo adzakhala wamaliseche monga tsiku limene anabadwa; ndidzamuwumitsa ngati chipululu, adzakhala ngati dziko lopanda madzi, ndi kumupha ndi ludzu.
lest I strip her naked, and set her as in the day that she was born, and make her as a wilderness, and set her like a dry land, and kill her with thirst.
4 Sindidzaonetsa chikondi changa pa ana ake, chifukwa ndi ana a mʼchiwerewere.
Yea, I will have no mercy upon her sons, for they are sons of whoredom,
5 Amayi awo akhala akuchita zachiwerewere ndipo anawabereka anawo akuchita zinthu zochititsa manyazi. Iwo anati, ‘Ine ndidzatsatira zibwenzi zanga, zimene zimandipatsa chakudya ndi madzi, ubweya ndi thonje, mafuta ndi chakumwa.’
for their mother has played the harlot. She who conceived them has done shamefully, for she said, I will go after my lovers, who give me my bread and my water, my wool and my flax, my oil and my drink.
6 Choncho njira yake ndidzayitseka ndi minga; ndidzamuzinga ndi khoma kotero kuti sadzapezanso njira yotulukira.
Therefore, behold, I will hedge up thy way with thorns, and I will build a wall against her, that she shall not find her paths.
7 Adzathamangira zibwenzi zake koma sadzazipeza; adzazifunafuna koma sadzazipeza. Pamenepo iye adzati, ‘Ndibwerera kwa mwamuna wanga woyamba uja, pakuti ndinali pabwino ndi iyeyo kusiyanitsa ndi pano.’
And she shall follow after her lovers, but she shall not overtake them. And she shall seek them, but shall not find them. Then she shall say, I will go and return to my first husband, for it was better with me then than now.
8 Iye sanazindikire kuti ndine amene ndinkamupatsa tirigu, vinyo watsopano ndi mafuta. Ndine amene ndinkamukhuthulira siliva ndi golide, zimene ankapangira mafano a Baala.
For she did not know that I gave her the grain, and the new wine, and the oil, and multiplied to her silver and gold, which they used for Baal.
9 “Choncho Ine ndidzamulanda tirigu wanga pa nthawi yokolola, ndi vinyo wanga watsopano pa nthawi yopsinya mphesa. Ndidzamulanda ubweya ndi thonje langa, zomwe akanaphimba nazo umaliseche wake.
Therefore I will take back my grain in the time of it, and my new wine in the season of it, and will pluck away my wool and my flax which should have covered her nakedness.
10 Motero tsopano ndidzaonetsa maliseche ake pamaso pa zibwenzi zake; palibe ndi mmodzi yemwe adzamupulumutse mʼmanja mwanga.
And now I will uncover her lewdness in the sight of her lovers, and none shall deliver her out of my hand.
11 Ndidzathetsa zikondwerero zake zonse: zikondwerero zake za chaka ndi chaka, za mwezi watsopano, za pa masiku a Sabata ndi maphwando ake onse a pa masiku okhazikitsidwa.
I will also cause all her mirth to cease, her feasts, her new moons, and her sabbaths, and all her solemn assemblies.
12 Ndidzawononga mitengo yake ya mpesa ndi mitengo yake yamkuyu, imene iye ankanena kuti inali malipiro ake ochokera kwa zibwenzi zake. Ndidzayisandutsa chithukuluzi, ndipo zirombo zakuthengo zidzadya zipatsozo.
And I will lay waste her vines and her fig trees, of which she has said, These are my hire that my lovers have given me. And I will make them a forest, and the beasts of the field shall eat them.
13 Ndidzamulanga chifukwa cha masiku amene anafukiza lubani kwa Abaala; anadzikongoletsa povala mphete ndi mikanda yamtengowapatali ndipo anathamangira zibwenzi zake, koma Ine anandiyiwala,” akutero Yehova.
And I will visit upon her the days of the Baalim, to which she burned incense when she decked herself with her earrings and her jewels, and went after her lovers, and forgot me, says Jehovah.
14 “Koma tsopano ndidzamukopa mkaziyo; ndidzapita naye ku chipululu ndipo ndidzamuyankhula mwachikondi.
Therefore, behold, I will allure her, and bring her into the wilderness, and speak soothingly to her.
15 Kumeneko ndidzamubwezera minda yake ya mpesa, ndipo ndidzasandutsa Chigwa cha Akori kukhala khomo la chiyembekezo. Kumeneko iye adzayimba nyimbo monga mʼmasiku a ubwana wake, monga tsiku limene anatuluka ku Igupto.
And I will give her her vineyards from there, and the valley of Achor for a door of hope. And she shall make answer there, as in the days of her youth, and as in the day when she came up out of the land of Egypt.
16 “Tsiku limeneli,” Yehova akuti, “udzandiyitana kuti, ‘Amuna anga;’ sudzandiyitananso kuti, ‘Mbuye wanga.’
And it shall be at that day, says Jehovah, that thou shall call me Ishi, and shall no more call me Baali.
17 Ndidzachotsa mayina a Abaala pakamwa pake; sadzatchulanso mayina awo popemphera.
For I will take away the names of the Baalim out of her mouth, and they shall no more be mentioned by their name.
18 Tsiku limenelo ndidzachita pangano ndi zirombo zakuthengo ndi mbalame zamumlengalenga ndiponso zolengedwa zokwawa pansi kuti ziyanjane ndi anthu anga. Ndidzachotsa mʼdzikomo uta, lupanga ndi zida zonse zankhondo, kuti onse apumule mwamtendere.
And in that day I will make a covenant for them with the beasts of the field, and with the birds of the heavens, and with the creeping things of the ground. And I will break the bow and the sword and the battle out of the land, and will make them to lie down safely.
19 Ndidzakutomera kuti ukhale mkazi wanga mpaka muyaya; ndidzakutomera mwachilungamo, mwaungwiro, mwachikondi ndi mwachifundo.
And I will betroth thee to me forever. Yea, I will betroth thee to me in righteousness, and in justice, and in loving kindness, and in mercies.
20 Ndidzakutomera mokhulupirika ndipo udzadziwa Yehova.
I will even betroth thee to me in faithfulness, and thou shall know Jehovah.
21 “Tsiku limenelo Ine ndidzayankha,” akutero Yehova. “Ndidzayankha mlengalenga pempho lake lofuna mitambo ndipo mvula idzagwa pa dziko lapansi;
And it shall come to pass in that day, I will answer, says Jehovah. I will answer the heavens, and they shall answer the earth,
22 ndipo nthaka idzamvera kupempha kwa tirigu, vinyo ndi mafuta, ndipo zidzamvera Yezireeli.
and the earth shall answer the grain, and the new wine, and the oil, and they shall answer Jezreel.
23 Ndidzadzala Israeli mʼdziko kuti akhale wanga: ndidzaonetsa chikondi changa kwa anthu amene ndinkawatchula dzina loti, ‘Sakondedwa.’ Ndidzawawuza amene ndinkawatchula dzina loti, ‘Si anthu anga,’ kuti, ‘Ndinu anthu wanga;’ ndipo adzanena kuti, ‘ndinu Mulungu wathu,’”
And I will sow her to me in the earth. And I will have mercy upon her who had not obtained mercy. And I will say to those who were not my people, Thou are my people, and they shall say, My God.

< Hoseya 2 >