< Hoseya 2 >

1 “Nena kwa abale ako kuti, ‘Ndinu anthu anga,’ kwa alongo ako kuti ‘Ndinu okondedwa anga.’”
Наричайте, прочее, братята си Аммий (Т. е., Люде мои), и сестрите си Рухама (Т. е., Придобила милост).
2 “Dzudzulani amayi anu, adzudzuleni iwo, pakuti si mkazi wanga, ndipo ine sindine mwamuna wake. Iyeyo achotse maonekedwe adama pa nkhope yake, ndi kusakhulupirika pa mawere ake.
Съдете се с майка си, съдете се; Защото тя не ми е жена, И аз не й съм мъж. Нека отмахне блудствата си от лицето си, И прелюбодействата си отмежду съсците си,
3 Akapanda kutero ndidzamuvula, ndipo adzakhala wamaliseche monga tsiku limene anabadwa; ndidzamuwumitsa ngati chipululu, adzakhala ngati dziko lopanda madzi, ndi kumupha ndi ludzu.
Да не би да я съблека гола, И я изложа както бе в деня, когато се е родила, И я направя като пустиня, И я поставя като безводна земя, И я уморя с жажда.
4 Sindidzaonetsa chikondi changa pa ana ake, chifukwa ndi ana a mʼchiwerewere.
Даже на чадата й няма да покажа милост, Понеже са чада от блудство.
5 Amayi awo akhala akuchita zachiwerewere ndipo anawabereka anawo akuchita zinthu zochititsa manyazi. Iwo anati, ‘Ine ndidzatsatira zibwenzi zanga, zimene zimandipatsa chakudya ndi madzi, ubweya ndi thonje, mafuta ndi chakumwa.’
Защото майка им блудства; Тая, която ги бе зачнала, постъпи срамотно; Защото рече: Ще отида след любовниците си, Които ми дават хляба ми и водата ми, Вълната ми и лена ми, маслото ми и питията ми.
6 Choncho njira yake ndidzayitseka ndi minga; ndidzamuzinga ndi khoma kotero kuti sadzapezanso njira yotulukira.
За това, ето, аз ще препреча пътя ти с плет от тръни, И ще направя преграда пред нея, За да не намери пътищата си.
7 Adzathamangira zibwenzi zake koma sadzazipeza; adzazifunafuna koma sadzazipeza. Pamenepo iye adzati, ‘Ndibwerera kwa mwamuna wanga woyamba uja, pakuti ndinali pabwino ndi iyeyo kusiyanitsa ndi pano.’
Тя ще се завтече след любовниците си, но няма да ги стигне; Ще ги потърси, но няма да ги намери; Тогава ще рече: Ще отида и ще се върна при първия си мъж, Защото ми беше по-добре тогава, отколкото сега.
8 Iye sanazindikire kuti ndine amene ndinkamupatsa tirigu, vinyo watsopano ndi mafuta. Ndine amene ndinkamukhuthulira siliva ndi golide, zimene ankapangira mafano a Baala.
И тя не знаеше, че Аз съм й давал житото, виното, и маслото, И умножил съм среброто и златото й, Което употребиха за Ваала.
9 “Choncho Ine ndidzamulanda tirigu wanga pa nthawi yokolola, ndi vinyo wanga watsopano pa nthawi yopsinya mphesa. Ndidzamulanda ubweya ndi thonje langa, zomwe akanaphimba nazo umaliseche wake.
За това, ще си взема назад житото на времето му, И виното си на определеното му време, И ще откъсна вълната си и лена си, Които трябваше да покриват голотата й.
10 Motero tsopano ndidzaonetsa maliseche ake pamaso pa zibwenzi zake; palibe ndi mmodzi yemwe adzamupulumutse mʼmanja mwanga.
И сега ще открия нечистотата й пред очите на любовниците й; И никой няма да я избави от ръката ми.
11 Ndidzathetsa zikondwerero zake zonse: zikondwerero zake za chaka ndi chaka, za mwezi watsopano, za pa masiku a Sabata ndi maphwando ake onse a pa masiku okhazikitsidwa.
И ще прекратя всичкото й веселие, - Тържествата й, новолунията й, съботите й, И всичките й определни празници.
12 Ndidzawononga mitengo yake ya mpesa ndi mitengo yake yamkuyu, imene iye ankanena kuti inali malipiro ake ochokera kwa zibwenzi zake. Ndidzayisandutsa chithukuluzi, ndipo zirombo zakuthengo zidzadya zipatsozo.
Ще опустоша и лозите й и смоковниците й, За които рече: Те са заплатата, Която ми дадоха любовниците ми. Ще ги обърна на лес, И полските животни ще ги пояждат.
13 Ndidzamulanga chifukwa cha masiku amene anafukiza lubani kwa Abaala; anadzikongoletsa povala mphete ndi mikanda yamtengowapatali ndipo anathamangira zibwenzi zake, koma Ine anandiyiwala,” akutero Yehova.
И ще я накажа за дните, които посвещаваше на Ваалимите, Когато им кадеше, Като се китеше с обеците си и огърлиците си И отиваше след любовниците си, А Мене забравяше, казва Госопд.
14 “Koma tsopano ndidzamukopa mkaziyo; ndidzapita naye ku chipululu ndipo ndidzamuyankhula mwachikondi.
Но, ето, Аз ще я привлека, И като я заведа в пустинята Ще й говоря по сърцето й.
15 Kumeneko ndidzamubwezera minda yake ya mpesa, ndipo ndidzasandutsa Chigwa cha Akori kukhala khomo la chiyembekezo. Kumeneko iye adzayimba nyimbo monga mʼmasiku a ubwana wake, monga tsiku limene anatuluka ku Igupto.
И още от там ще й дам Ханаанските лозя, И долината Ахор (Т. е., Смущение) за врата на надежда; И там тя ще се отзове както в дните на младостта си, И както в деня, когато възлезе из Египетската земя.
16 “Tsiku limeneli,” Yehova akuti, “udzandiyitana kuti, ‘Amuna anga;’ sudzandiyitananso kuti, ‘Mbuye wanga.’
В оня ден, казва Господ, Ще ме наричаш: Мъж ми; И няма да ме наричаш вече: Ваал ми. ( Т. е., Мой господар.)
17 Ndidzachotsa mayina a Abaala pakamwa pake; sadzatchulanso mayina awo popemphera.
Защото ще премахна имената на Ваалимите от устата й; И те няма вече да се поменуват с имената си.
18 Tsiku limenelo ndidzachita pangano ndi zirombo zakuthengo ndi mbalame zamumlengalenga ndiponso zolengedwa zokwawa pansi kuti ziyanjane ndi anthu anga. Ndidzachotsa mʼdzikomo uta, lupanga ndi zida zonse zankhondo, kuti onse apumule mwamtendere.
В оня ден ще направя за тях завет С полските зверове, С небесните птици, И със земните гадини; И като строша лък и меч и бой, и ги махна от земята, Ще ги населя в безопасност.
19 Ndidzakutomera kuti ukhale mkazi wanga mpaka muyaya; ndidzakutomera mwachilungamo, mwaungwiro, mwachikondi ndi mwachifundo.
И ще те сгодя за Себе Си завинаги; Да! Ще те сгодя за Себе Си в правда и в съдба, В милосърдие и в милости.
20 Ndidzakutomera mokhulupirika ndipo udzadziwa Yehova.
Ще те сгодя за Себе Си вьв вярност; И ще познаеш Господа.
21 “Tsiku limenelo Ine ndidzayankha,” akutero Yehova. “Ndidzayankha mlengalenga pempho lake lofuna mitambo ndipo mvula idzagwa pa dziko lapansi;
И в оня ден ще отговоря, казва Господ, Ще отговоря на небето, И то ще отговори на земята,
22 ndipo nthaka idzamvera kupempha kwa tirigu, vinyo ndi mafuta, ndipo zidzamvera Yezireeli.
И земята ще отговори на житото, на виното, и на маслото, И те ще отговорят на Израела.
23 Ndidzadzala Israeli mʼdziko kuti akhale wanga: ndidzaonetsa chikondi changa kwa anthu amene ndinkawatchula dzina loti, ‘Sakondedwa.’ Ndidzawawuza amene ndinkawatchula dzina loti, ‘Si anthu anga,’ kuti, ‘Ndinu anthu wanga;’ ndipo adzanena kuti, ‘ndinu Mulungu wathu,’”
И ще я насея за Себе Си на земята; И ще покажа милост към непомилваната; И на ония, които не бяха мои люде, ще река: Мои люде сте вие; И те ще рекат, всеки един: Ти си мой Бог.

< Hoseya 2 >