< Hoseya 14 >
1 Iwe Israeli bwerera kwa Yehova Mulungu wako. Machimo anu ndi amene akugwetsani!
Tanrın RAB'be dön, ey İsrail, Çünkü suçlarından ötürü tökezledin.
2 Bweretsani zopempha zanu ndipo bwererani kwa Yehova. Munene kwa Iye kuti, “Tikhululukireni machimo athu onse ndi kutilandira mokoma mtima, kuti tithe kukuyamikani ndi mawu a pakamwa pathu.
Dualarla gidin, RAB'be dönün, O'na, “Bağışla bütün suçlarımızı” deyin, “Lütfet, kabul et bizi, Öyle ki, dudaklarımızın kurbanını sunalım.
3 Asiriya sangatipulumutse; ife sitidzakwera pa akavalo ankhondo, sitidzanenanso kuti, ‘Milungu yathu’ kwa zimene manja athu omwe anazipanga, pakuti ndinu amene mumachitira chifundo ana amasiye.”
Asur kurtaramaz bizi, Savaş atlarına binmeyeceğiz. Artık ellerimizle yaptığımıza ‘Tanrımız’ demeyeceğiz, Çünkü öksüz sende merhamet bulur.”
4 Ine ndidzachiza kusakhulupirika kwawo ndipo ndidzawakonda mwaufulu pakuti ndaleka kuwakwiyira.
“Onların dönekliğini düzelteceğim, Gönülden seveceğim onları, Çünkü onlara karşı öfkem dindi.
5 Ndidzakhala ngati mame kwa Israeli Ndipo iye adzachita maluwa ngati kakombo. Adzazika mizu yake pansi ngati mkungudza wa ku Lebanoni;
Çiy gibi olacağım İsrail'e; Zambak gibi çiçek açacak, Lübnan sediri gibi kök salacaklar.
6 mphukira zake zidzakula. Kukongola kwake kudzakhala ngati mtengo wa olivi, kununkhira kwake ngati mkungudza wa ku Lebanoni.
Dallanıp budaklanacaklar, Görkemleri zeytin ağacını, Kokuları Lübnan sedirini andıracak.
7 Anthu adzakhalanso mu mthunzi wake. Iye adzakula bwino ngati tirigu. Adzachita maluwa ngati mphesa ndipo kutchuka kwake kudzakhala ngati vinyo wochokera ku Lebanoni.
Yine insanlar oturacak gölgesinde; Buğday gibi gelişecek, Asma gibi serpilecekler; Lübnan şarabı kadar ün kazanacaklar.
8 Efereimu adzati, “Ndidzachita nawonso chiyani mafano? Ine ndidzamuyankha ndi kumusamalira. Ine ndili ngati mtengo wa payini wobiriwira; zipatso zako zimachokera kwa Ine.”
Ey Efrayim, artık ne işim var putlarla? Yanıtlayacak, seninle ilgileneceğim. Yeşil çam gibiyim ben, Senin verimliliğin benden kaynaklanıyor.”
9 Ndani ali ndi nzeru? Adzazindikire zinthu izi. Ndani amene amamvetsa zinthu? Adzamvetse izi. Njira za Yehova ndi zolungama; anthu olungama amayenda mʼmenemo, koma anthu owukira amapunthwamo.
Bilge kişi kavrasın bunları, Anlayan anlasın. Çünkü RAB'bin yolları adildir; Bu yollarda yürür doğrular, Ama başkaldıranlar bu yollarda sendeler.